umodzi womwe khristu anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/pdfs/umodzi.pdf · umodzi...

70
Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha kumabatiza anthu ambiri ndi kukhazikitsa malo a mpingo ochuruka, koma popanda umodzi, ntchito yonseyo sidzapindula kanthu. M’Moyo wathu wathupi wauchimo, kumakhala kosabvuta kupatukana. Koma mwa Mzimu Woyera wokha ndimo tingathe kusunga umodzi. Mulungu amafuna mpingo utakhala wolimba ndi wangwiro ndikuti ukafikire ndi kuthandiza mizimu yambiri yotayika ndi kuibweretsa kwa Yesu. Cholinga chathu chenicheni mu maphunzirowa ndikufuna kuphunzira za ubwino ndi kufunika kwa umodzi, kumvetsa zomwe Baibulo limaphunzitsa za umodzi ndinso kuphunzira momwe tingathetsere zolimbana ndi makangano pakati pathu ndi kukhala amodzi mwa Khristu. Mutu 1: Umodzi ndi Wofunika Koposa 1. Sanafe, Yesu anapempherera umodzi wa omtsatira ake, kuphatikizirapo ifenso lero lino – Yohane 17:11,20,21. Kodi Yesu amamva bwanji akamaona ife tikugawanika? Nanga muganiza amamva bwanji akamaona ife tikuonetsa umodzi? A. Imfa ya Yesu inali pafupi kwambiri. Iye anali ndi kanthawi kochepa kwambiri asanamwalire koti apemphere. Choncho anayenera kupempherera zinthu zokhazo zomwe zinali zofunikira kwambiri m’moyo wake. Umodzi chinali chinthu chofunikira kwambiri pa pemphero lake. Yesu anasiya malo ake aulemu kumwamba ndi cholinga chofuna kupulumutsa dziko lapansi. Iye anagwira ntchito molimbika pa nthawi ya utumiki wake. Anali atatsala pang’ono kukapereka moyo wake pamtanda. Yesu sanafune kuti ntchito yake ndi imfa yake kuti ingopita pachabe. Iye anafuna uthenga wake wa chipulumutso ukhale wopambana padziko lonse. B. Zikanakhala bwanji ngati ophunzira a Yesu akadapanda kulemekeza pemphero limeneli? Zikadakhala bwanji ngati wophunzira aliyense akadayambitsa mpingo wake wake wa payekha ndi kupatuka pa anzake ena onse. Kodi anthu akadakhulupirira uthenga womwe ophunzirawa akadamalalikira? Kodi muganiza kuti uthenga umenewu bwenzi tikumaumva monga tichitira leromu? C. Yesu anapemphera “kuti dziko likhulupirire.” Kupatukana kwathu kumatchinjiriza anthu kuti asakhulupirire uthenga wabwino. Tiyenera kuonetsa mwa kuchita chikondi ndi mtendere womwe tiulalikira. Kodi muganiza ndi anthu angati omwe akadalandira chipulumutso ngati Akhristu akadapanda kugawikana? D. Yesu anati nyumba kapena ufumu uliwonse womwe ugawikana wokha sungaime ayi – Mateyu 12:25. 2. Paulo anafuna kuti Afilipi akhalirane mwa mtendere ndi umodzi kuti awalire dziko lapansi monga kuunika – Afilipi 2:14-16. Ngati Afilipi aja sakadasunga umodzi, ndiye kuti utumiki wa Paulo pa uthenga wabwino ukadakhala wopanda phindu. Ngati palibe chikondi ndi mtendere pakati pa Akhristu pamenepo palibenso kuunika. 3. Baibulo limatilamula ife kuti tisunge umodzi pakati pathu – 1 Akorinto 1:10; Aefeso 4:1-6. A. Umodzi ndi ganizo limene timalipanga. Ndi chinthu chimene timasankha. B. Umodzi wa Chikhristu sutanthauza kuti tonse tikhale ndi ganizo lofanana pa zinthu zazing’ono m’Baibulomo. Koma utanthauza kugwirizana mu zikhulupiriro ndi zolinga zazikulu mwa chikondi pa wina ndi mnzake ndiponso pa otaika. C. Umodzi wa thupi la Khristu ndi chimodzi mwa zinthu zisanu ndi ziwiri za ziphunzitso zazikulu za chikhulupiriro cha Chikhristu – Aefeso 4:4-6. D. Pamene tigawanikana mosasamalira bwino, ndiye kuti sitimvera malamulo a Khristu ndi Atumwi aja.

Upload: others

Post on 19-Jan-2020

6 views

Category:

Documents


0 download

TRANSCRIPT

Page 1: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 11/29/12

Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera

Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha kumabatiza anthu ambiri ndi kukhazikitsa malo a mpingo ochuruka, koma popanda umodzi, ntchito yonseyo sidzapindula kanthu. M’Moyo wathu wathupi wauchimo,

kumakhala kosabvuta kupatukana. Koma mwa Mzimu Woyera wokha ndimo tingathe kusunga umodzi.

Mulungu amafuna mpingo utakhala wolimba ndi wangwiro ndikuti ukafikire ndi kuthandiza mizimu yambiri

yotayika ndi kuibweretsa kwa Yesu.

Cholinga chathu chenicheni mu maphunzirowa ndikufuna kuphunzira za ubwino ndi kufunika kwa umodzi,

kumvetsa zomwe Baibulo limaphunzitsa za umodzi ndinso kuphunzira momwe tingathetsere zolimbana ndi

makangano pakati pathu ndi kukhala amodzi mwa Khristu.

Mutu 1: Umodzi ndi Wofunika Koposa

1. Sanafe, Yesu anapempherera umodzi wa omtsatira ake, kuphatikizirapo ifenso lero lino – Yohane

17:11,20,21. Kodi Yesu amamva bwanji akamaona ife tikugawanika? Nanga muganiza amamva bwanji

akamaona ife tikuonetsa umodzi?

A. Imfa ya Yesu inali pafupi kwambiri. Iye anali ndi kanthawi kochepa kwambiri asanamwalire koti

apemphere. Choncho anayenera kupempherera zinthu zokhazo zomwe zinali zofunikira kwambiri

m’moyo wake. Umodzi chinali chinthu chofunikira kwambiri pa pemphero lake. Yesu anasiya malo

ake aulemu kumwamba ndi cholinga chofuna kupulumutsa dziko lapansi. Iye anagwira ntchito

molimbika pa nthawi ya utumiki wake. Anali atatsala pang’ono kukapereka moyo wake pamtanda.

Yesu sanafune kuti ntchito yake ndi imfa yake kuti ingopita pachabe. Iye anafuna uthenga wake wa

chipulumutso ukhale wopambana padziko lonse.

B. Zikanakhala bwanji ngati ophunzira a Yesu akadapanda kulemekeza pemphero limeneli? Zikadakhala

bwanji ngati wophunzira aliyense akadayambitsa mpingo wake wake wa payekha ndi kupatuka pa

anzake ena onse. Kodi anthu akadakhulupirira uthenga womwe ophunzirawa akadamalalikira? Kodi

muganiza kuti uthenga umenewu bwenzi tikumaumva monga tichitira leromu?

C. Yesu anapemphera “kuti dziko likhulupirire.” Kupatukana kwathu kumatchinjiriza anthu kuti

asakhulupirire uthenga wabwino. Tiyenera kuonetsa mwa kuchita chikondi ndi mtendere womwe

tiulalikira. Kodi muganiza ndi anthu angati omwe akadalandira chipulumutso ngati Akhristu

akadapanda kugawikana?

D. Yesu anati nyumba kapena ufumu uliwonse womwe ugawikana wokha sungaime ayi – Mateyu 12:25.

2. Paulo anafuna kuti Afilipi akhalirane mwa mtendere ndi umodzi kuti awalire dziko lapansi monga kuunika

– Afilipi 2:14-16. Ngati Afilipi aja sakadasunga umodzi, ndiye kuti utumiki wa Paulo pa uthenga wabwino

ukadakhala wopanda phindu. Ngati palibe chikondi ndi mtendere pakati pa Akhristu pamenepo palibenso kuunika.

3. Baibulo limatilamula ife kuti tisunge umodzi pakati pathu – 1 Akorinto 1:10; Aefeso 4:1-6.

A. Umodzi ndi ganizo limene timalipanga. Ndi chinthu chimene timasankha.

B. Umodzi wa Chikhristu sutanthauza kuti tonse tikhale ndi ganizo lofanana pa zinthu zazing’ono

m’Baibulomo. Koma utanthauza kugwirizana mu zikhulupiriro ndi zolinga zazikulu mwa chikondi pa

wina ndi mnzake ndiponso pa otaika.

C. Umodzi wa thupi la Khristu ndi chimodzi mwa zinthu zisanu ndi ziwiri za ziphunzitso zazikulu za

chikhulupiriro cha Chikhristu – Aefeso 4:4-6.

D. Pamene tigawanikana mosasamalira bwino, ndiye kuti sitimvera malamulo a Khristu ndi Atumwi aja.

Page 2: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 2

4. Umodzi ndi wofunika kwambiri chifukwa Mulungu amakonda mpingo wake ndi kudana komanso

kuweruza omwe amayambitsa mipatuko – Miyambo 6:16-19; Tito 3:10,11; Aroma 16:17,18.

Sindikondwera pamene wina abvutitsa ndi kupweteka thupi langa. Ndimakwiya pamene wina asokoneza

banja langa ndi kuyambitsa mabvuto. Kugawikana kumaononga ndi kubvulaza thupi la Khristu.

Kumasokoneza ndi kugawanitsa banja la Mulungu. Kugawikana kumapunthwitsa anthu otayika ndipo

kumawalepheretsa kukhulupirira mwa Khristu. Mulungu amawakonda otayikawo. Mulungutu amalikonda banja lake. Choncho chiweruzo chake chimakhala chokhwima kwa omwe amabweretsa kapena kuyambitsa

malekano. Tamvetserani momwe Mulungu amaweruzira nkhani za malekano:

A. Pamene kulimbana ndikugawanikana kubwera mu mpingo, Akhristu ambiri amapwetekedwa mumtima

kapena kusowa mtendere wa mtima ndipo kenako amasiya kutsatira Yesu. Yesutu anatichenjeza kuti

tisachite zinthu zomwe zingachimwitse anthu ndi kuwapangitsa kusiya kumvera Khristu.

Ngati wina apangitsa mmodzi wa aang’ono awa omwe amakhulupirira ine kuti achimwe, kukanakhala

bwino kuti woteroyo akolekedwe mkhosi mwake ndi mwala wamphero waukulu ndiumizidwa m'nyanja

yakuya kwambiri. Tsoka dziko lapansi chifukwa cha zinthu zomwe zichimwitsa anthu! Ngati dzanja

lako kapena phazi lako likuchimwitsa ndi bwino kulidula ndi kulitaya. Pakuti kuli bwino kulowa

m’moyo wopunduka kapena wopanda dzanja kapena phazi koposa kuponyedwa m'moto wa nthawi

zonse uli ndi manja kapena mapazi awiri. Ndipo ngati diso lako likuchimwitsa, likolowole ndi kulitaya.

Kuli bwino kwa iwe kulowa m'moyo ndi diso limodzi koposa kukhala ndi maso awiri ndi kuponyedwa

m’gehena wa moto – Mateyu 18:6-9.

B. Mulungu adzaononga iwo omwe adzaononge kachisi wake. Paulo analemba za anthu omwe anaononga

mpingo, kachisi wa Mulungu, poyambitsa mipatuko.

Kodi simudziwa kuti inu ndinu kachisi wa Mulungu ndikuti Mzimu wa Mulungu akhala mwa inu? Ngati

wina aliyense awononga kachisi wa Mulungu, Mulungunso adzamuononga popeza kachisi wa Mulungu

ndiwopatulika ndipo inu ndinu kachisiyo – 1 Akorinto 3:16,17.

Ngati tilimbana ndi kumagawanikana moona osapembedza ndiye kuti tikukana uthenga wabwino womwe

tiulalika. Ngati timakondana, ndiye kuti anthu onse adzadziwa kuti ndifedi ophunzira a Khristu. Palibe chinthu

chomwe chimaphwanya ndikuononga ntchito ya uthenga wabwino koposa malekano athu. Kodi muganiza

dziko lathuli likadakhala lotani lero ngati Akhristu onse pamodzi akadakhala amodzi ndi ogwirizana ndi

kumalalikira uthenga wabwino ndi mphamvu zonse?

Mafunso okambirana: � Nchifukwa chiyani timangolimbikira pa ziphunzitso zina koposa momwe tichitira pa chiphunzitso cha

umodzi?

� Tafotokozani momwe kugawanikana kwalepheretsa ndi kutchinjirizira uthenga wabwino m’dera lanu.

� Tafotokozani momwe umodzi wolimbikitsira ulaliki wa uthenga wabwino m'chigawo kapena dera lanu.

Mutu 2 - Zomwe Baibulo Linena pa za Chiphunzitso cha Umodzi.

Mawu oyamba: Baibulo lonse limaphunzitsa za umodzi. Mulungu adalenga mwamuna ndi mkazi ndipo anati

iwo akhale thupi limodzi (Genesis 2). Ndipo Yesu adati, ”Chomwe Mulungu wa chimanga, munthu

asachilekanitse” – Mateyu (. Abrahamu anati kwa Loti “Pasakhale kukangana pakati pa iwe ndi ine, pakuti tiri

abale” – Genesis 13. Pamene Kora, Datani ndi Abrahamu anayeserera kugawa Israyeli pogalukira Mose ndi

Aroni, Mulungu anang’amba nthaka ndipo onse ogalukirawo anamezedwa pomwepo. Davide analemba kuti

“Zimakhala zosangalatsa kwambiri pamene abale akhala pamodzi mwa umodzi!” – Masalmo 133. Umodzi wa

thupi la Yesu ndi chiphunzitso chofunikira kwambiri cha m’Chipangano Chatsopano. Tiyenera kumvera

chiphunzitso chimenechi. Ngati timakhulupirira ndi kuphunzitsa ziphunzitso zinanso za m’Chipangano

Chatsopano, tiyeneranso kukhulupirira ndi kuphunzitsa chiphunzitso cha umodzi.

1. M’Chipangano Chatsopano, umodzi uli ndi maziko awiri, maziko a uzimu ndi maziko a chiphunzitso.

Page 3: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 3

A. Pa Aefeso 4:1-3 timawerenga za umodzi wokhazikika pamaziko auzimu.

Monga wamndende wa Ambuye, ndi kudandaulirani ine tsopano, kuti muyende molingana ndi

moyenera maitanidwe omwe unaitanidwa n awo, ndipo onetsetsani kuti mukudzichepetsa

ndiponso muli ofatsa; khalani opirira; ololerana wina ndi mnzake mwachikondi. Samalirani

kwambiri poonetsetsa kuti mukusunga umodzi wa mzimu podzimangirira pa mtendere nthawi zonse.

Umodzitu ndi wa Mzimu. Kudzichepetsa monga Khristu ndiko kumachititsa kuti umodzi utheke.

Chilengedwe chathu chathupi cholakwa chimakonda moyo wopatukana. Tawerengani mndandanda wa

“ntchito za thupi” mu Agalatiya 5:19-21. Mukuona kuti madano, ndeu, kaduka, zopsa mtima,

kukhumba zonyansa, zotetana, magawano, mipatuko ndi njiru zaikidwa mu gulu limodzi ndi chigololo,

kuledzera ndi nyanga. Theka la machimo omwe atchulidwa mu mndandanda umenewu amapezeka

pafupifupi m'malekano a mumpingo uliwonse, ndi mukulekana kwa banja liri lonse. Koma tawerengani

mndandanda wa “chipatso cha mzimu mu Agalatiya 5:22,23. Umodzi umakhala wosavuta ngati anthu

akhala otere.

Popanda chipatso cha Mzimu Woyera, chimene chimagonjetsa khalidwe lakale ndi kusintha ife kuti

tifanane Khristu, sitingathe kusunga umodzi. Ngakhale tigwirizane ndi ziphunzitso zonse, koma

khalidwe lathu la kudzikonda lidzapezabe njira ya kutilekanitsa ngati tikuyenda m’thupi. Makolo a

gulu la chibwezero, limene Mpingo wa Khristu mmene tiri kukhalamo lero, anayetsetsa kugwirizanitsa

okhulupirira malembo. Anatisonyeza ife mmene tingagwirizanirane mwa ziphunzitso zenizeni za

Baibulo. Koma sanaphunzitse zambiri za malekano ochitidwa mwa uzimu. Koma tiyenera kuphunzira.

B. Mu Aefeso 4:4-6 Paulo ali kutipatsa ife madziko a chiphunzitso cha umodzi. Watchula ziphunzitso

zazikulu zisanu ndi ziwiri zimene tiyenera kuzikhulupirira m’malo mwakuti tikhale amodzi.

Pali thupi limodzi ndi Mzimu mmodzi—monga momwe munaitanidwa ku chiyembekezo

chimodzi pamene munaitanidwa—Ambuye mmodzi, chikhulupiriro chimodzi, ubatizo umodzi;

Mulungu mmodzi ndi Atate wa onse, amene ali pamwamba pa onse ndi mwa onse ndi mkati

mwa zonse.

Tafanizirani 1 Akorinto 15:1-8 pamene Paulo waika mndandanda wa zinthu zofunika kwambiri mu

uthengamo.

Pakuti chimene ndinalandira ndinapereka kwa inu monga chofunika choyambirira: kuti

Khristu anafera zoipa zathu monga mwa malembo, ndikuti anaikidwa, ndikuti anauka pa tsiku lachitatu monga mwa malembo, ndi kuti anaonekera kwa Petro, ndi kwa khumi ndi awiriwa.

Izi ndi zoonadi zolimba zimene zitipanga ife kukhala monga momwe tiri. Chotsani ngakhale chimodzi

mwa izo ndipo sitingakhalenso mpingo wa Ambuye. Tiyenera kulandira zonsezo m’malo mwakuti

tikhale amodzi ndi kulandirana wina ndi mnzake. Tiribe ufulu wakugwirizana ndi wina aliyense

wokana ngakhale chimodzi mwa zoonadi zimenezi. Sitingathenso kusiya chimodzi mwa zoonadi

zimenezi m’malo mwakuti tisunge umodzi.

Malembonso akuphunzitsa kuti sitingakhale amodzi ndi Akhristu amene achita mitundu ya uchimo

yoipa ndipo sakulapa – 1 Akorinto 5; Mateyu 16:15-20; Aroma 16:17,18.

2. Umodzi wakhazikika pa chisomo. Tiri amodzi ndi Mulungu pachifukwa cha chikhululukiro cha chisomo

chake. Tiri amodzi ndi Iye osati chifukwa ife tiri olungama koma chifukwa zochimwa zathu zakutidwa ndi

mwazi wa Khristu. M’njira yomweyo, tiri amodzi wina ndi mnzake kupyolera m’chisomo ndi

chikhululukiro.

Mulandirane wina ndi mnzake, monga momwe Khristu anakulandirani inu, m’malo mwakuti tichitire

Mulungu ulemu. – Aroma 15:7.

Mulungu anatilandira ife monga anthu osakonzeka, ndipo momwemonso ife tilandirane wina ndi mnzake

monganso anthu osakonzeka.

Page 4: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 4

Monga momwe ndakukonderani inu, inunso mukondane wina ndi mnzake – Yohane 13:34.

Yesu anatikonda ngakhale tinali wochimwa koteronso tikondane wina ndi mnzake. Umodzitu umadalira

chisomo. Mulungu watipatsa ife malamulo ena ndipo tiyenera kuwalemekeza. Komatu nkhani ya

Chikhristu simalamulo ayi. Koma ndi nkhani ya chikondi, ubale wokhulupirika ndi Mulungu. Kulekana

kwakukulu pakati pa Chikhristu ndi zipembedzo zina zonse kuli pa chisomo. Mulungu adzatiweruza popanda chifundo ngati tiribe chifundo pa ubale wathu ndi anzathu. – Yakobo 2:13.

A. Taonani kuti pali ziphunzitso zina zofunika kwambiri zomwe tonse tiyenera kudzikhulupirira ndipo

ngati tipanda kutero sikungatheke kuti tikhale amodzi – Aefeso 4:4-6; 1 Akorinto 15:3-8; 5:1-13.

Tiyenera kupatuka pa wina aliyense yemwe akana ziphunzitso zofunikirazi.

B. Komanso Baibulo limafotokozera ndi kuzindikiritsa kuti alipo magawo ena ndi nkhani zina

zazing’ono zomwe Akhristu okhulupirika ndi oona angathe kumva mosiyana ndikutsatira mosiyana

komabe nakhala amodzi mu mtendere ndi Mulungu, wina ndi mnzake – Aroma 14. Ichitu ndi

chiphunzitso chofunikira koposa chomwe Baibulo liphunzitsa za umodzi.

1) Yesu amati pali malamulo ena omwe amakhala ofunikira kuposanso ena – Mateyu 23:23; 22:35-

40; 40:19. Tiyenera kumasamalira malamulo ena onse koma ena ndi ofunika kuwasamalira

kwambiri chifukwa ali ndi maziko osiyana ndi ena.

2) Ziphunzitso zina zomamveka bwino ndimalemba ake koma zina zimakhala zovuta kumvetsa

kwake – 2 Petro 3:16. Ziphunzitso zomwe zimakhudza chipulumutso chathu zimakhala zomveka

mosavuta. Nkhani zomwe ziri zovuta kutanthauzira kwake kapena kumvetsa, nkhani zomwe

zimadalira kwambiri pa umunthu wathu wolephera ndi nzeru zathu za umunthu sizingakhale

nkhani za chipulumutso kapena zifukwa zoti tilekane.

3) Malamulo ena a m’malembo amangokhala ndi cholinga chofuna kufotokozera tanthauzo lokhala

Mkhristu ndi mwana wa Mulungu. Malamulo ena amangokhudzidwa ndi nkhani zazing’ono ndi

zosakhala zakuya kwenikweni. Ziphunzitso za chikondi, ndi chikhulupiriro ndi kukhulupirika ndi

zomwe ziri zotumikira koposa ziphunzitso zofotokozera za dongosolo la chipembedzo.

Kulakwitsa moona pa zakutalika kwa tsitsi lamkazi sikuli kuopsa kwambiri monga zingaopsere

ngati munthu sakhulupirira za “kuuka”. Afarisi anali otanganidwa ndi okhudzidwa kwambiri ndi

zinthu zooneka kunja kwa thupi ndi mtima monga za miyambo yosiyanasiyana ndi kusamba

munthawi zokonzedwa. Yesu anawasonyeza malemba oti, “ndifuna chifundo, osati nsembe ayi –

Mateyu 12:1-7; 9:10-13.

4) Mulungu amadziwa kuti popeza tiri nako kufooka kwathu kwa umunthu, ndiponso chifukwa

choti tonse sitiri okhwima m’chikhulupiriro, sitingathe kuona bwinobwino, ndimvetsa bwino

mawu ake. Munkhani zoterozo, iye amangotipatsa mwa chisomo chake ndipo amatilamula ife

kuti tiwachitirenso anzathu zomwezo – Aroma 14:1-15; 7. Izi zimakhudzanso nkhani zomwe

timakhulupirira ndi kuzolowera kuchita m’mipingo mwathu. Pamene tidzapita kumwamba

tidzatulukira kuti tonse tidalakwitsa m'zinthu zina zazing’ono zing’ono zomwe tidazikhulupirira.

Palibe ndi mmodzi yemwe amamvetsa bwino ndi kumvera malembo onse mwachindunji. Nkhani

ndi yoti tiri opulumutsidwa mwa chisomo.

Nkhani zambiri zomwe timalimbana nazo ndi kumakanganira mpaka kumagawanikana nazo

mumpingo sinkhani za chipulumutso konse. Koma umodzi ndi nkhani ya chipulumutso. Ichi ndi

chiphunzitso chofunikira zedi. Komabe palinso choonadi chomwe Baibulo limafotokoza pa za

umodzi chomwe anthu ambiri satha kuchimvetsa. Zitsanzo:

(a) Sitiri oyenera ngakhale kulandira mbale wofooka, womangiririka zinthu zazing’ono

zoti tingathe kuchita nazo kapena osachita nazo.

(b) Akhristu omwe ali a maganizo awiri osiyana pa nkhani zimenezi, angathe kukhala nafe

pamodzibe ngakhale mmodzi wa iwo ali wolakwa. Ichi chitanthauza kuti mu nkhani

Page 5: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 5

zomwe mpata umakhalapo pakati pa abale okhulupirika kuti akhale ndi maganizo

olekana pa nkhani zina, sizingakhale nkhani za chipulumutso ayi.

(c) Pamene mbale asiyana ndi ine pa momwe titanthauzira malembo, sichitanthauza kuti

iyeyo saopa Mulungu kapena akuyesetsa kusamvera

Mulungu mwa muyezo uliwonse.

(d) Lamulo la Paulo mu Aroma 14 loti tilorerane limakhudza zambiri zoposa khalidwe

lakelake la munthu. Kukhulupirira masiku oyera ndi opatulika kunakhudzanso

misonkhano ya mipingo zochitika chitika pa nthawi ya chipembedzo.

(e) Mbale amene ali womangiridwa ku chikumbumtima chake yemwe amaweruza mbale

wake “pochita zoipa” akubweretsa magawano chimodzimodzi monga momwe mbale

yemwe achita zomwe zikhumudwitsa ubale wake womangiririka ku chikumbumtima

chake uja. M’mbuyomo takhala tikutsutsa yemwe amayambitsa zinthu zatsopano

monga woyambitsa mipatuko. Uku kunali kulakwa. Mu Aroma 14 sitiphunzira motero.

5) Pamene tiwerenga bwino ndi kumvetsa bwino Aroma 14,15 timaloledwa kukhalabe amodzi

ngakhale pali nkhani zina zazing’ono zomwe tikulephera kumva mofanana. Choncho ndi

malembo amenewa titha kuona ndi kumvetsa bwino nkhani imeneyi kuti:

a.) Mulungu amatilamulira kuti tipitirirebe kugwira ntchito pamodzi chifukwa cha nkhani

zofunikira kwambiri zomwe timazimva mofanana ndi kusiya zina zazing’onozing’ono

zomwe tingathe kuchita popanda izozo kuti Mulungu ndiye aweruze.

b.) Ndingathe kugwiri ntchito ndi abale ena mumpingo ngakhale pali zina zomwe

sitizimva mofanana pa mfundo zina zomwe iwo achita ndi kukhulupirira.

c.) Nkhani itha kukhala ndi magawo abwino ndi oipa ngakhale ndiikulupirira koposa.

Ngati pafika poti kumasulira kwa umunthu wathu wooka kugwiritsidwa ntchito

nkutheka kuti nditha kukhala wolakwa m’chikhulupiriro changa.

C. Makolo athu akale pa nthawi yawo yobwezeretsa anasonkhanitsa chiphunzitso cha m'Chipangano

Chatsopano cha umodzi m’mawu oti, “M’chikhulupiriro, umodzi; malingaliro, ufulu; m'zonse,

chikondi."

D. Ngakhale kulekana kwina ndi kofunika chifukwa kumakhudza za ziphunzitso zofunikira, nthawi zambiri kulekana kumakhalapo chifukwa sitimvetsa zomwe Baibulo limaphunzitsa za chisomo.

1) Chisomo ndi choonadi siziri zinthu zotsutsana china ndi chinzake ayi. Zonsezi zimagwirizana

ntchito yofotokozera za khalidwe ndi moyo wa Yesu – Yohane 1:14. Yesu anasakaniza chisomo

chopusa ndi kuleza, pamodzi kukhudzidwa koposa kwa choonadi.

2) Paulo anawauza Akhristu kuti “simuli pansi pa lamulo koma pansi pa chisomo.” – Aroma 6:14.

Anthu powerenga mawu amenewa amaganiza kuti chisomocho chimatanthauza kuti azichita ziri

zonse zomwe zingawakomere koma Paulo akukanitsitsa zimenezi. Sitiyenera kumaopa momwe

chisomo chingakhudzire kumvera kwa pachoonadi. Chisomo nthawi zonse chimapereka kumvera

kwakukulu kuposa chilamulo chomwe chimangotsamira pa zowerengeka za malamulo akunja kwa

thupi ndi mtima. Chisomotu chimasintha mitima yathu ndipo chimatipangitsa kukhala omafuna

kukondweretsa Mulungu.

3) Pamene tiwalandira iwo amene tisiyana nawo maganizo pa nkhani zina zazing’ono sikutanthauza

kuti tikugwirizana ndi zomwe tikuona ngati iwo akulakwitsa ayi. Sizitanthauza kuti tasiya kumvera

lemba la m’Baibulo ndi limodzi lomwe. Tiyenera kumakhala osamalira kwambiri potsatira

maganizo athu m’makhalidwe athu ndi kumaphunzitsa ena zomwe tikukhulupirira kuti ndi zomwe

malemba akutanthauza.

Page 6: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 6

Koma ngati sakumvetsabe chomwe tikutanthauza pa nkhani yomwe tikuwauzayo ngati iri

yaing’ono, tiyeni tipitirezebe kuwakonda ndi kugwira nawo ntchito pamodzi. Mu Aroma 14

timamva kuti tiyenera kusiyira Mulungu kuti aweruze nkhani zina zomwe ife talephera.

Kusunga umodzi pakati pathu ndi omwe tisiyana nawo maganizo ndi lamulonso pa lokha, ndi

chinthu choyenera kuchikhulupirira, ndi gawo la chiphunzitso cha Chipangano Chatsopano.

Baibulo limatiphunzitsa kuti anthu onse, kuphatikizapo akulu ampingo angathe ndipo ayenera kumagwira ntchito pamodzi, ndipo sikuti zingatheke kuti azikhala ofanana m’maganizo pa mfundo

zonse angakumana nazo. Mpingo ungathe kukula koposa anthu zana limodzi (100) popanda

kulekana maganizo. Koma kuti izi zitheke, pamafunika kuti tikhale ndi luso lozindikira msanga

nkhani zoti titha kulolerana popeza ndi zazing’ono.

Mutu 3: Zoyambitsa Kulekana.

Nthawi zina m’mudzi mumagwa mliri. Anthu amavutika ndipo ena amafa. Madotolo ndi akatswiri ena

amabwera kuti afufuze choyambitsa kapena chomwe chikufalitsa matendawo. Pamene atulukira ndi kumvetsa

bwino gwero la matendawo, ndi pomwe angathe kuthetsa matendawo ndi kuwatchinjirizanso. Momwemonso

ngati timvetsa bwino chomwe chimayambitsa kapena komwe kumachokera moyo wolekana, ndi pomwe

tingathe kuchiza ndi kutchinjiriza bvuto limeneli. Malingana ndi malemba, zoyambitsa kulekana zina ndi:-

1. Kukana kukhulupirira zinthu zofunikira kwambiri ndi malamulo a m’Baibulo.

A. Yohane analemba kuti Akhristu asamalandire m’nyumba zawo aphunzitsi omwe ankati Yesu

sanabwera monga munthu wathupi – 1 Yohane 2:22,23; 4:1-3; 2 Yohane 7-11; tawerengani ndipo

mufanizire 1 Akorinto 13:3; Aefeso 4:4-6; 1 Akorinto 15:3,4; 5:1-13.

B. Mulungu satitsutsa ife ngati tidzilekanitsa kwa aphunzitsi onyenga oterewa. Tiri oyenera kupatuka pa

amenewa.

2. Moyo wathu wauchimo “thupi” – Agalatiya 5:19-21; 3 Yohane 9,10. Timanena kuti kupatukana kwathu

sikuli koyipa chifukwa tichita zomwe malembo anena, koma zoona ndi zoti nthawi zambiri nkhani

imakhala yokanganira ukulu ndi mphamvu, kapena nthawi zina kuwawirana mtima ndi kusakhululukirana

chabe.

3. Kukonda kuchititsana makani pa zinthu zopanda pake ndi zosamveka – 1 Timoteo 1:3-7; 4:7; 6:3-5,20,21;

2 Timoteo 2:15-17,23-26; 4:3,4; Tito 1:10-15; 3:9-11.

4. Kusamvetsa bwino zomwe Baibulo liphunzitsa za umodzi – kapena za umodzi weniweni womwe Baibulo

limafotokoza – Aefeso 4:16; Aroma 14:1-15; 7

5. Kukulitsa ndi kulemekeza zinthu zina koposa Khristu ndi mtanda – 1 Akorinto 1:10 – 4:1. Anthu a ku

Korinto anagawanikana chifukwa anakhulupirira ndikutsatira kwambiri alaliki koposa Yesu Khristu. Ife

mwina tikhoza kumakhulupirira kwambiri ndi kutamanda koposa mlaliki wodziwa kuyankhula bwino,

mphunzitsi mwanzeru, dzina, nyumba, chiphunzitso, kapena mwambo. Zonse ndi zomwe zimalekanitsa

Akhristu, (Paulo adati Akorinto anayenera kukhala nalo gulu lomwe ankadziwika nalo kuti aonetse ndi uti

anali wobvomerezeka kwa Mulungu – 1 Akorinto 11:9). Chirichonse (ngakhale chiphunzitso) chomwe

chimalowetsedwa m’malo mwa Khristu monga nkhani yaikulu, chimakhala fano

6. Kukhulupirira malamulo, kukhulupirira kuti timalandira chipulumutso mwa zintchito zabwino zomwe

tichita koposa chisomo cha mtanda.

Moyo wathu wauchimo wathupi, nthawi zonse umafuna kutenga dongosolo la uthenga wa chisomo ndi

kuusandutsa kuti ukhale monga lamulo chabe, dongosolo lomwe anthu amalandira chipulumutso chifukwa

chotsatira malamulo chabe. Izitu zinawachitikira ena aja a mumpingo woyamba uja. Taonani Machitidwe

15 ndinso kalata ya kwa Agalatiya. Ndipo zakhala zikuchitikanso mumpingo mu mazana mazana a zaka

kuyambira munthawi ya atumwi. Anthu omwe amalimbana ati pofuna kuteteza dongosolo la malamulo,

nthawi zambiri amalakwitsa poganiza kuti, malinga ndi chikhulupiriro chawo, iwo amachita zimenezi

pofuna kuvutikira uthenga wabwino ndi chikhulupiriro cha Chikhristu, komanso ati amachita zimenezi

polimbikitsa uthenga wabwino ndi Chikhristu.

Page 7: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 7

A. Chipangano Chatsopano chimaphunzitsa kuti palibe yemwe angalandire chipulumutso chifukwa

chosunga lamulo,, chifukwa palibe ndi mmodzi yemwe, amene amasunga malamulo mwachindunji ndi

mosamala. Tonse tinachimwa ndipo taperewera mu ulemerero wa Mulungu, komabe timawerengedwa

olungama chifukwa Yesu analipira machimo athu ndi mwazi wake pa mtanda – Aroma 3:20-28.

B. Kufananiza pakati pa kuweruzidwa mwa lamulo ndi kuweruzidwa mwa chisomo

Kuyeretsedwa mwa Lamulo Kuyeretsedwa mwa Chisomo

Zochita zathu za ife eni Zochitidwa ndi Mulungu

Kudalira pa ntchito zabwino - Kudalira ntchito yomwe Yesu anachita

Agalatiya 3:10; Yakobo 2:10.

Kuchita bwino kwa ife eni. Kuchita bwino kochokera kwa Mulungu.

Kutukumuka chifukwa chochita bwino Kukweza ndi kulemekeza Mulungu

Kulandira chipulumutso “chomwe- Chipulumutso mphatso yomwe Mulungu ayenera

kutipatsa” sitinali oyenera kuilandira.

Ukapolo Ufulu

Kukhudza zolembedwa zokhazo basi Kukhudza mzimu ndi maganizo amkati.

Mwa zintchito, zochitika Mwa chikhulupiriro

Kuchita bwino chifukwa cholamulidwa- Kuchita bwino chifukwa moyo wathu watsopano

ufuna kutero.

Kungochita ndikutsata zingapo zoti- Kuchita zonse zabwino zomwe tingathe

zomwe tifuna.

Onse analephera Onse angalandire.

C. Komabe anthu ena amaganizirabe kuti adzalandira chipulumutso posunga bwino malamulo a Mulungu.

Mwa chilengedwe chathu, mipatuko imabadwa chifukwa chotsamira pa malamulo. Taonani zina za

zinthu zomwe munthu wotsamira pa malamulo amachita:

1) Amasankha ena a malamulo a milungu yomwe ndi yodziwika ndi yokondedwa ndi iyeyo kapena

ziphunzitso zina za malembo ndi kuzigwiritsa ntchito monga muyezo woonera chikhulupiriro

koma panthawi yomweyo akutaya ndi kuiwala malamulo ambiri a Mulungu ndi ziphunzitso

zomwe (makamaka zamkati mwa mtima ndi za uzimu).

2) Amawatenga onse omwe amasamala bwino malamulo omwe iye anawasankhawa monga

olungama ndi okhulupirika kwa Mulungu ndipo ena onse omwe sasunga zimenezi monga

“olakwa” Ichi chitanthauza kuti iwowa amene ali “olungama ndi okhulupirikawa”, sali olakwa.

Alibe tchimo. Izi zimaonetsa kulakwitsa posasamala mfundo yoti tonse timalephera kumvera

Mulungu m'zinthu zambiri chifukwa cha kusadziwa kapena kufooka, ndipo onse ayenera kudalira

chisomo.

3) Amalimbikira pa malamulo oyang’ana zakunja kwa thupi ndi kumvera kwake kopanda ungwiro

koposa malamulo amkati mwa mtima ndi kumvera kwa mkatikati kwa Mulungu.

4) Amakhazikitsa maganizo ambirimbiri a anthu ndi miyambo ya anthu monga malamulo ena

owonjezedwa pa malamulo a Mulungu – Taonani Mateyu 15:1-20. Ngati munthu ali wotetezeka

ndi kusunga malamulo kwake koposa chisomo, pamenepa, iye amaona kuti zingamuyendere

bwino ngati aonjezerabe malamulo ena awiri atatu monga linga lomuteteza, m’malo mongotsata

Page 8: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 8

ndi kuchita zinthu momveka bwino monga momwe malemba afotokozera. Miyambo ina

imaonjezeredwa ndi cholinga choti zioneke zoonadi. Ichitu ndi chifukwa chake mipingo ina

ipezeka kuti nthawi zonse ikulekana pa mfundo zina zatsopano.

5) Amalimbikira za mgwirizano wathu ndi malamulo koposa mgwirizano wathu ndi Mulungu

yemwe anapereka malamulowo. Akhristu otsamira kwambiri pa malamulo nthawi zambiri amakhala ofooka pa momwe iwo eni ayendera ndi Mulungu.

D. Nchifukwa chiyani moyo wathu wauchimo umakonda kutsatira ndi kusamala malamulo koposa

chisomo?

1) Titha kukhala ndi chipembedzo cholamulidwa ndi ife eni, chokhala ndi dongosolo

lomangoyang’ana ndi kutsamira pa mndandanda wa malamulo osankhika ndi ziphunzitso

zokonzedwa. (Pamene munthu ali pa ubale iye ndi Mulungu, zinthu sizikhala pansi pa

ulamuliro wake ayi; Mulungu amatitengerabe ife nthawi zoti zomayeserera ndi kuchita

chifuniro chake ku miyoyo yathu.

2) Kudalira pa malamulo kumatipatsa moyo wodzitcha apamwamba. Ife tiri okhulupirika ndi

omvera ndipo enawo ali olakwa – tafanizirani ndi mawu opezeka pa Luka 18:9-14.

3) Zimatipangitsa kuti tidzinyenge tokha poganiza kuti tiri otetezeka. Popeza tikungoyang'ana pa

zofunikira za Mulungu zowerengeka chabe osati pa zofuna zake zonse, timaona ngati tikuchita

bwino pa kumvera.

4) Timangolimbikira kuchita zinthu zingapo zoonekera kunja mokhoza (kapena kungosunga

ziphunzitso zingapo chabe zolondola), osati kusinthika kwa mitima yathu (ntchito ya pamoyo

wathu wonse yotheka chifukwa cha thandizo la chisomo cha Mulungu chokha basi).

5) Pamene tiri pansi pa ulamuliro wa chilamulo timakhala ndi lamulo lochitira chiri chonse ndipo

sitisowanso kuvutika ndi kuganiza. Pamene kwa munthu yemwe ali pansi pa chisomo ayenera

kugwiritsa ntchito mfundo zauzimu pofuna kuyankha Mafunso ambiri omwe malembo

sanafotokozere mwatchutchutchu, ndipo izi zimafunika kuti ife tikhale olimba ndi oganiza

mozama kwambiri.

6) Ndi kosabvuta kusamalira dongosolo la malamulo koposa kusamalira Mulungu amoyo ndi

woopsa.

E. Zoopsya Zapadera Zodalira Malamulo

1) Zimatamanda kuchita bwino kwa ife eni ndi kumvetsa kwathu ndi kuchotsa chitamandochi

kwa mwini wake Yesu ndi mtanda – taonani 1 Akorinto 1:31; 2:2.

2) Zimatipangitsa kukhala otukumuka ndi onyada m’malo mokhala odzichepetsa. Timakhala

okonzekera kuweruza ndikutsutsa anzathu enanso.

3) Zimabereka kugawikana kosiyanasiyana m’thupi la Khristu, kusokoneza pemphero la Ambuye

wathu lija la Umodzi. Umodzi pakati pa anthu operewera pa ufumu wa Mulungu umatheka

mwa chisomo.

4) Zimalinganitsa maganizo athu aumunthu ndi chikhalidwe chathu malamulo a Mulungu ndipo

potero zmatipangitsa kuti kupembedza kwathu kwa Mulungu kusakhale kobvomerezeka –

Mateyu 15:1-20.

5) Zimatipatsa nthawi yoti tidzinyengeka poganiza kuti ndifedi omvera Mulungu, potsamira

kwambiri pa malamulo pang’ono osankhidwa mosaganizira bwino. (Kodi ndi chiyani chomwe

chimapangitsa kuti malamulo ochepa amenewa akhale ofunika kuposa ena onsewo? Kodi ndi

Page 9: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 9

chiyani chimapangitsa kuti nkhani zina za ziphunzitso zikhale ndi mphamvu koposa malamulo

ake amkatikati mwake?)

6) Zimanyalanyaza malamulo a Mulungu pa za mtima ndi mzimu, ndipo amakhala wokhutitsidwa

ndi kungomvera lamulo Lolembedwa popanda kuganizira mzimu ndi cholinga cha lamulolo.

7) Timangodzidalira tokha m’malo modalira Mulungu.

8) Timalowetsa ubale wathu ku malamulo angapo omwe timawasankha m’malo molimbikitsa

ubale ndi Mulungu. Timadziwa zambiri za malamulo koposa Mulungu yemwe anapereka

malamulowo.

9) Pali malamulo ena omwe timawakonda ndi kuwazolowera ndi maganizo ena, ngakhale akhale

abwino powagwiritsa ntchito monga mwa cholinga cha Mulungu. Amasanduka mafano kwa ife

chifukwa amalowa m’malo mwa Ambuye ndi mtanda wa Khristu pa ziphunzitso zathu. Palibe

lamulo kapena chiphunzitso chomwe chingakhale ndi tanthauzo ngati chiri chongodziimira

pachokha pambali pa Umbuye wa Khristu.

10) Kudalira ndi kutsamira pa malamulo kumabvala kumvera koperewera kwa Mulungu chifukwa

kumanyalanyazitsa malamulo ambiri a Mulungu ndipo amangotsala ochepa okha, chifukwa

kumanyalanyazitsa nkhani za mkatikati za kumvera ndi kulemekeza zakunja zooneka ndi

maso. Mwa chisomo, wokhulupirira amakhala wotengeka pomvera Mulungu chifukwa iye

amachita ichi pobvomereza chikondi cha mtanda, ubale wake wa iye ndi Ambuye wake.

11) Zikapitirira, kutsamira pa malamulo kumadzapherezera potilekanitsa ife ndi chisomo cha

Mulungu. “Inu amene muyetsedwa olungama ndi lamulo, mulibe kanthu popeza

munasiyanitsidwa ndi Khristu; Mudagwa posiyana nacho chisomo” – Agalatiya 5:4.

Simungathe kukhulupirira ntchito zonse za Khristu ngati mukhulupirira kwambiri pa kuchita

bwino kwanu kwa inu eni kapena kulungama kwanu. Ntchito ya kukhululukira ndi kuombola

inachitika chifukwa cha ochimwa, osati chifukwa cha iwo ali angwiro.

Komatu zonsezi sizitanthauza kuti Mulungu alibe nafe ntchito kapena kuti kumvera kwathu kuli

kosafunika. Cholinga chenicheni cha chisomo ndicho chofuna kukhazikitsa mwa ife moyo wodzadza

ndi kumvera koposaposa. Monga momwe mkulu wina ananenera, “Mulungu amakukondani monga

momwe muliri komatu amakukondani koposa kotero kuti sangathe kukusiyani pomwe muliripo.”

Mutu 4: Umodzi Pakati pa Ogwira Ntchito

Gawo loyamba: Kusunga Ubale Wabwino.

Mawu oyamba: Satana amafuna kugawanitsa ndi kudanitsa anthu. Amafetsa kuwawirana mtima ndi udani.

Khristu amafuna kuyanjanitsa ndi kugwirizanitsa anthu. Iye amafetsa mtendere ndi chikondi. Anthu nthawi

zonse adzakhala ndi maganizo olekana ndi makangano. Ngati zimenezi tingozilekerera osaziperera njira

yokonza, zimakwaniritsa zolinga za Satana. Maganizo a Yesu angathe kuthetsa kulekana kwa maganizo pakati

pa anthu ndi kugwetsa malinga olekanitsa mabanja, mipingo, achinansi, kuntchito kapena maubale ena

osiyanasiyana. Yesu watipatsa mfundo zomwe zingathe kuchiza ndi kubwezeretsa ubale woonongeka. Tiyeni

tione komwe makangano amachokera ndi chomwe tingachite pa nkhani imeneyi.

1. Muzu weniweni wa kulimbana ndi kulakwirana pakati pa anthu ndi kunyada ndi kudzikonda – Mateyu

18:1-5.

A. Bvuto: Tonse timafuna kudziwa kuti “Kodi wamkulu ndani?” (wopambana, mpondamatiki, wokhoza,

wodzisamala, wosiririka, wokondedwa, wa ulamuliro woposa ndi zina zotero). Ngati nthawi zonse

ndi mangoganizira za ine ndekha, ndiye kuti kulimbana ndi enawo kuyenera kuyambika nthawi ina

iriyonse.

B. Kuthetsa kwake: Kukhala wakufa kuthupi” – Agalatiya 2:20.

Page 10: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 10

1) Mateyu 18:3,4 – Mudzione ngati kamwana kakang’ono podzifanizira ndi ena.

2) Afilipi 2:5-8 – Kutaya ulemu ndi ufulu wanu mwakufuna kwanu.

3) Aefeso 5:21 – Kumverana chifukwa choopa ndi kulemekeza Khristu.

4) Afilipi 2:3,4 – Muwatenge ena onse monga ofunikira koposa inu.

5) Yohane 13:3-17 – Sambitsanani mapazi anu.

2. Sitingathe kubwezeretsa ubale womwe taononga – Mateyu 18:6.

A. Malipiro kwa olakwayo:

1) “Kuli bwino amizidwe m’nyanja yakuya.”

2) Mulungu sadzamva pemphero lake – Mateyu 5:23,24; Ahebri 12:14.

B. Mtengo kwa ena onse okhudzidwa.

1) Abale apabanja – kuwawidwa

2) Mpingo – kupatukana

3) Osakhulupirira - kukanidwa – Yohane 17:20,21; Afilipi 2:14-16.

C. Musalole kukhala woyambitsa udani kapena kukana kuthetsa zolimbana – Aroma 12:18.

1) Konzani msanga tolakwika ting’ono-ting’ono pa ubale wanu madzi asanafike mkhosi.

2) Pezani njira zothandiza kuti mukonze ubale molumikizana.

3) Limbikirani kuonetsa chikondi. Bwezerani chabwino ku choipa – Aroma 12:17,21.

4) Musaumirire pa ufulu wanu – mungadzaupezenso.

5) Mudzadalitsidwa – Mateyu 5:9.

3. Muyenera kuganizira ndi kuthana ndi zonse zoyambitsa maudani ndi kukhumudwitsa – Mateyu 18:7-14.

A. Kuganizira gwero la zolakwirana: Kodi inu muli ndi gawo lanji pa kulimbanako? Mateyu 7:1-5.

1) Ndi milandu yochepa yomwe wolakwa amakhala mmodzi.

2) Yang’anani bwino mopanda kukondera chomwe chakhumudwitsa mnzanu, mwana, kholo,

mbale, ndi mlongo wanu.

3) Kodi zochita zanga pankhaniyi zimaonjeza bwanji moto wa nkhani?

a. Mwina zolakwa zamnzangayo sizachilendo kwenikweni, koma momwe ndazitengera

ndi momwe muli moonjezera mafuta pa moto.

b. Mwina ndimaganizira kwambiri za ufulu wanga.

c. Ena sadzasiya kuchimwa. Kuthetsa kwake kuyenera kukhala malingana ndi momwe

ndiitengera nkhaniyo.

Page 11: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 11

d. Ichi ndicho chinsinsi cha ufulu ndi mtendere.

B. Kuchotsa zoyambitsa kulakwirana:

1) Kuyankhula (dula dzanja lako, kolowola diso) kumasonyeza changu chochotsera zoyambitsa

uchimo ndi kulakwirana. Mizimu ikutayika.

2) Kudzitamandira ndi kudzikonda kwanga sikuli koyenera.

3) Chikondi ndicho chidzalipira mtengo wa mtendere ndi kuyanjananso.

a. Yesu analipira msonkho womwe sanayenera – Mateyu 17:24-27.

b. “Bwanji osangololera kuti inu mukhale onyengedwayo” – 1 Akorinto 6:1-8.

c. Abrahamu anangompatsa Loti mwayi woti iye asankhe malo okhalako poyambirira

popewa kulimbana – Genesis 13:8-11.

4) Muthane nazo zolakwiranazo tsopano – musalorele kuti kudzitamandira kwanu ndi

kudzikonda kwanu kuononge mwana wa Mulungu – Aroma 14:13,15,19,21.

4. Tsatirani ndondomeko ya Mulungu yothetsera zolakwirana – Mateyu 18:15-20; 5:23-26.

A. Pitani kwa yemwe wakulakwiraniyo ndi kumuuza iyeyo osati ena ayi.

1) Timangofuna kuuza wina aliyense chifukwa cha mkwiyo wathu.

2) Anthu ambiri amathamangira kuuza akulu a mpingo asanaonane ndi wowalakwirayo.

B. Pitani modzichepetsa ndi modekha – Agalatiya 6:1. Mkwiyo umapangitsa kuti munthu winayo

ayambe kudziteteza ndipo amayamba kudzikonzera njira zodzitchinjiriza nazo.

C. Chitani zimenezi mwachangu, mkanganowo usanakule, usanakhudze ena, ndipo mitima isanafike

polimba.

1) Timalandira chilango chowawa pokana nzeru ya malemba.

2) Kulimbana kumakhala zaka zambiri mwinanso mpaka moyo wawo wonse chifukwa cha

kunyada.

3) Koma ngati pali chikondi chokwanira ndi kukhudzidwa pa moyo wabwino wa pa banja pake,

mpingo, kuntchito, anthu atha kupeza njira.

5. Khululukani monganso Mulungu anakukhululukirani. – Mateyu 18:21-35.

A. Kukhululuka kulibenso china chofaniziridwa nacho, ngati tifuna kupulumutsidwa – Mateyu

6:12,14,15.

1) Kusakhululuka ndilo “tchimo losakhululukidwa” lomwe tingalichite.

2) Nchifukwa chiyani tidzayembekezera kuti Mulungu atichitire ife zomwe sitingachitire enawo?

3) Kubwezera kuli kwa Mulungu – Aroma 12:19.

B. Kukhululuka ndi “mchitidwe wokhala ndi cholinga” osati wongomverera m’thupi ayi.

1) Monganso chikondi, ndi lamulo lachikhalire.

Page 12: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 12

2) Titha kuganizira zosankha kuchita mchitidwe wokhululuka. Kenako tidzayamba kumva m’thupi.

C. Kusakhululuka kumangolekerera ubale ukumangosweka.

1) Kuwawirana mtima pakati pa mwamuna ndi mkazi komwe kumangokhala osapezeredwa njira

yothetsedwa kumasakaza banja. (Ngakhale kuwawirana mtima kwa kholo, mbale, mlongo ngakhale wina aliyense).

2) Mkwiyo ndi kuwawirana mtima kwathu kumapatsa Satana mwayi m’miyoyo yathu – Yakobo

1:20; Aefeso 4:26,27.

D. Kukhululukirana kumabwezeretsa ndi kuchiza maubale owonongeka.

1) Ngati wina apempha chikhululukiro, tiyenera kutero nthawi yomweyo kuchokera pansi pa

mtima, popeza nafenso ndi ochimwa.

2) Mzimu wokhululukira umakhala wofunikira munthu winayo asanalape.

a. Khristu anapempherera iwo omupachika – Luka 23:34.

b. Mzimu wokhululukira sufulumiza kuchita choipa – 1 Petro 4:8; 1 Akorinto 13:6,7.

c. Pamene munthu mmodzi ali nawo mzimu wokhululukira ndipo abwera poyera,

zimapangitsa kuti winayonso abwere poyera.

Mawu otsiriza: Pamene tikuchita ndi zolakwirana, tikupemphedwa kuti “tithetse zoipa ndi zabwino.” – Aroma

12:20,21. Chabwino chomwe muchita chidzasungunula mtima wa yemwe munali kulimbana nayeyo – 1

Samueli 24:26.

Umodzi Pakati pa Ogwira Ntchito Gawo Lachiwiri: Pamene Ogwira Ntchito Mumpingo Alekana Maganizo.

Kodi bvuto lalikulu mumpingo ndiliti? Pa za utumiki? Akulu ambiri amaganiza kuti bvuto lalikulu ndi la

maubale a pakati pa atsogoleri. Mipingo yambiri yaonongeka chifukwa chakulimbana pakati pa akulu ampingo

koposa mabvuto ena monga ankhuli yachiwerewere kapena zanyanga ndi ufiti.

1. Ogwira ntchito mumpingo ayenera kuphunzira kusamalira ubwino wa ntchito ya Khristu asanaganizire za

zofuna zawo, ndiponso ayenera kudziwa ndi kuphunzira bwino magwero a zolimbana ndi kuthana nazo

zisanafike powasokoneza mwa uzimu, kusokoneza ntchito yawo, kukhumudwitsa ntchito ya mpingo

kumudzi ndi kumayiko akutali, ndi kulepheretsa kupulumutsidwa kwa miyoyo.

Sitingathe kulipira mtengo wa kulakwitsa komwe kungabwere kwa ife ngati tilephera kuchita zimenezi –

Luka 17:1-2; Yakobo 3:1.

2. Akulu ampingo ayenera kuzindikira gawo la moyo wodzikonda poyambitsa zolimbana. Akulu ampingo

nawonso ali nalo bvuto limeneli monganso wina aliyense. Amishonale kapena ogwira ntchito ampingo

nthawi zonse ayenera kumagwira ntchito m'magulu. Tingathe kumanena kuti tikulimbana chifukwa

“chofuna kutsata mfundo zokhazikika,” “zotumikira za mudongosolo”, kapena “nkhani zauzimu,”

pamene nkhani yeniyeni iri, “kodi wamkulu ndani?” “kodi akulamulira ndani?” pakadakhala palibe

kudzitukumula, nkhani zinazo bwenzi zitathetsedwa.

Mukaika atambala awiri mukhola lankhuku ndiye kuti mukhala nkhondo yafumbi mpaka adziwike mwini

weniweni wolamulira kholalo. Ndi kuganiza kuti palibe kusiyana pankhani ya nkhukuyi. Ku thupi ifenso

ogwira ntchito mumpingo tiri chomwecho pachilengedwe. Koma izi zisakhale chomwecho kuuzimu. Ndi

mfundo za Khristui ndi kukhwima mu uzimu kwa Mkhristu kokha komwe kungathe kuthetsa mabvuto a

ubale wa ogwira ntchito mumpingo. Ine kusagwirizana kudzakhalapobe koma zisafike poti mpaka

kuononga kapena kufooketsa ntchito ya Mulungu.

Page 13: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 13

3. Ngakhalenso ophunzira anali kukumana ndi nthawi zina zomwe panali mabvuto osiyana maganizo pakati

pawo. Paulo ndi Barnaba anafika poti aliyense amayenda m'njira yake yake, komabe anapitirira kusunga

ndi kusamala ubale wawo monga abale – Machitidwe 15:36-40 (sikukadakhala

kotheka kuti athe kufalitsa uthenga wabwino modalilika ngati akadalephera kuyanjana wina ndi

mnzake). Pamene Petro analakwitsa, Paulo analimbana naye kwambiri – Agalatiya 2:11-14. Koma anthu awiriwa anaconda ndi kulemekezana kwambiri – 2 Petro 3:15.

4. Anthu odzikhulupirira okha ndi kudzitukumula, omva za iwo okha, omwe amati akakumana ndi

maganizo olekana ndi awo, nkumaona ngati ali pa chiopsezo, asamasankhidwe pa udindo uliwonse mu

mpingo.

Malembo amati “woyang’anira asakhale womva za iye yekha.” (Tito 1:7). Koma akhala “wodzadzidwa

ndi Mzimu Woyera.” (Machitidwe 6:3) mphunzitsi sangathe kutumikira ena ngati iye alibe chipatso cha

Mzimu Woyera. Umodzi “ndi wa Mzimu” – Aefeso 4:1-3. Posankha a mishonale kapena akulu ampingo,

sikokwanira kwa munthu kukhala wodziwa kuyankhula bwino, kukonza zinthu mwadongosolo,

utsogoleri, ndi kukhala wodalira kwambiri pa ziphunzitso kokha ayi. Zinthu zonsezi zimakhala

zosafunikira ngati wosankhidwayo alibe mzimu wa Khristu – 1 Akorinto 13; Aroma 8:9. Pamene

mukuganizira za munthu woti akutsogolereni, tadzifunsani nokha kuti “kodi munthu ameneyi amachita

bwanji ndi anthu ena pa nkhani za ntchito za kumpingo? Nanga ku banja kwake?

5. Pakati pa Akhristu ndi pakati pa atsogoleri, Yesu watiphunzitsa momwe tingathetsere kusiyana kwathu

kwa maganizo. Ogwira ntchito ampingo ndi atsogoleri ayenera kumazindikira zakuopsa komwe

kumakhalapo chifukwa chakusagwirizana pakati pawo popeza kumakhudza ntchito ya uthenga wabwino.

Kuopsa kochotsedwa, kutaika kwa nthawi ndi mphamvu, kulephereka kwa mapemphero (Mateyu

5:23,24; Ahebri 12:14); Kupunthwitsa omwe akadakhala Akhristu ndinso Akhristu aang’ono ndi ofooka

– Yohane 17:21; Afilipi 2:14,15; Luka17:1,2.

6. Ogwira ntchito ampingo ayenera kumanga mfundo yoti sadzalola kusiyana maganizo kwawo kuti

kuononge ntchito ya Mulungu.

7. Atsogoleri ndi antchito ampingo ayenera kumatsata mfundo za malemba pokonza maubale osweka.

Konzani ubale womwe wangoyamba kuonetsa zizindikiro zoonongeka zisanafike woipitsitsa. - Mateyu

18:15-17; Agalatiya 6:1; Mateyu 5:21-26; Aefeso 4:26-27; Yakobo 1:19,20; Mateyu 7:2-5.

8. Pewani chirichonse chomwe chimakulakwitsani ndi kuyambitsa zolimbana – Aroma 14:13,19,19,21;

Mateyu 18:8,9.

9. Pewani kudzitukumula – Aroma 12:16; Afilipi 2:3..

10. Musakakamire pa ufulu wanu, Yesu sanachite choncho ayi – Afilipi 2:5-11; 1 Petro 2:21-25; Aroma

15:1-3. Paulonso sanatero ayi – 1 Akorinto 4:10-13; 9:19-23; 2 Akorinto 12:15. Tonse timatha

kumverana wina ndi mnzake ndipo timaphunzitsidwa kutero – Aefeso 5:21.

11. Pewani “kuyerekeza zinthu moipa” – kuyerekeza mongoganizira mopanda umboni weniweni – 1

Timoteo 6:4; Yohane 7:24.

12. Chikondi chimakwirira machimo ochuruka ndi zolakwika za unyinji – 1 Petro 4:8; 1 Akorinto 13:4-7.

13. Khululukiranani wina ndi mnzake – Aefeso 4;31,32; Mateyu 18:21-35.

14. Sungani chidzalo cha chipatso cha mzimu woyera – Agalatiya 5:22,23; Luka 11:13.

15. Sankhani antchito omwe ndi obvomerezeka mogwirizana ndi maganizo a choonadi ndi mfundo za

mpingo pa ntchito zake. Ngati pali kusamvana mu nkhani zina, kambiranani zimenezi m'kanyumba

komatu popanda abale ena onse.

16. Ngati nkhani zake ziri zazikulu mutha kuitana akulu ena odalirika kuti ayese kukuthandizani kukonza

Page 14: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 14

zobvutazo. Nthawi zina mutha musiyitsa njira yanji, koma chofunikira kwambiri ndi choti anthu awiri

olakwiranawo athetse nkhani yawoyo mwa uzimu ndipo akhaliranenso mwa mtendere pakati pawo koma

ngati apitirirabe kusungirana mkwiyo m’mitima mwawo, chisomo cha Mulungu chiyenera kuchotsedwa

kwa iwo pa ntchito yawo ya mtsogolo.

Takambirana za zosautsa, koma paliponse pamene mzimu wa Khristu uli mwa ogwira ntchito, zosautsa zonse zimathetsedwa zisanafike poipitsitsa. Mautumiki ena omwe amagwiridwa mogwirizana amathekanso, monga

anamchitira Paulo ndi anzake ogwira naye ntchito – Afilipi 3:16-17.

Umodzi Pakati pa Ogwira Ntchito Gawo Lachitatu: Kumanga Ubale Wabwino Pakati pa Atsogoleri Ampingo

Mawu oyamba: Mpingo utha kumayenda bwino, koma kenako ntchito imayamba kusokonekera chifukwa cha

kukangana wina ndi mnzake pakati pa atsogoleri. Ntchito zambiri za pa mpingo zimalowa pansi ndi kuzilala

chifukwa cha kukokana komwe kumayambika chifukwa cha ziphunzitso zonyenga. Ife atsogoleri kupyolera mu

kufooka kwathu, chonde, tisaononge kachisi wa Mulungu. 1 Akorinto 3:16,17.

1. Maganizo osiyanasiyana okhudza ubale pakati pa atsogoleri onse a mpingo (woyang’anira ndi

woyang’anira mnzake, woyang’anira ndi mlaliki, woyang’anira ndi mtumiki, ndi ena). Zambiri za

mfundo zimenezi, zimathandizanso pa ubale apakati pa Akhristu onse.

A. Chitani zonse mosakondera kapena kuyang’ana nkhope – 1 Timoteo 5:21. Aliyense ali nawo

anthu omwe amakondwera nawo, komatu izi zisakhudze momwe muchitira ndi anthu enawo.

B. Musamuyankhulire munthu mawu omwe simunayenera kumuyankhulira. Ndipo musayankhule

chirichonse chokhumudwitsa chomwe chiri chosathandiza.

C. Ganizirani ndi kusinkhasinkha zonse zomwe mwakonza ndi mawu omwe mwakonza kuti kodi

enawo akamva siziwapweteka m’maganizo?

D. Musakhale odzitamandira nokha ndi kumva za inu nokha monga opambana – Aroma 12:3,16.

E. Muzindikire zomwe zingautse, komanso zofooka za anthu ena pamodzi ndi zomwe amakonda

maganizo awo onse. Yesetsani kusamalira zimenezi ngati nkotheka.

F. Muzilolera zofooka za anzanu monga momwe mungafunirenso kuloleredwa pa zofooka zanu ndi

anzanu – Mateyu 6:14,15; Aroma 15:7.

G. Zindikirani kufunika kwa mphatso iriyonse ndi luso m’thupi la Khristu – Aroma 12:3-8.

Musayembekezere kuti munthu aliyense azingochita bwino nthawi zonse. Yamikirani mphatso

ya munthu aliyense pa yekha koposa kumukana kapena kumunyoza chifukwa chakulephera

kwake.

H. Nthawi zonse perekani ulemu kwa iwo omwe ayenera kuulandira panthawi yake – Aroma 13:7.

Khalani achangu potulukira zabwino zomwe ziri mwa anthu ena monganso momwe

mungachitire ndi zoipa mwayiwo. Mulibe ufulu wodzudzula zolephera, koma muyambe

mwabweza mangawa oyamikira ndi kulemekeza khalidwe labwino.

I. Phunzirani ndi kuzindikira chifukwa chomwe munaonetsera khalidwe la mtundu umenewo kwa

anzanu, ndipo muchotseretu moyo woipawo ku mbali yanu. Ichi chidzadalitsa moyo wanu wonse

kuchokera pa nthawi yomwe mwa phunzira izi.

J. Pa mkangano uliwonse, poyamba, inde movutikira, taonani ndi kufufuza mokhulupirika mbali

yomwe inu mwachititsa kuti mkanganowu ufike pamenepa, chomwe mumachita, ndipo kenako

yambani mwadzikonza inu eni ake – Mateyu 7:1-5.

K. Fulumirani kukonza ubale ndi kubwezeretsa mgwirizano pamene kusamvana kungoyamba

Page 15: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 15

kumene, pamene anthu sanataye mafuno abwino kapena chikhulupiriro mwa wina ndi mnzake.

Kukonza kumeneku kukhala chinthu choyamba kuganiziridwa. Ubale umasokonezeka chifukwa

ife timalolera kuti zitero. Anthu amakhala ogwirizana pamodzi chifukwa amatsimikira kutero

mokondweretsa Yesu. Ayenera kutero.

L. Ngati pali kusaganizirana bwino pakati panu ndi mnzanu pa nkhani ina, musayembekezere kuti

mnzanuyo ayambe kubwera kwa inu kudzapepesa. Yesu akuwauza olakwiridwa onse kuti iwo

apite – Mateyu 18:15-17. Akumuuza wolakwirayo kuti apite – Mateyu 5:23-25. Palibe

“weniweni woti akhale woyamba kupita”. Koma pitani ndi kudzichepetsa konse poopa kuti

mungaonjezere mabvutowo – Agalatiya 6:1. (Atsogoleri nawonso ayenera kudzichepetsa, lamulo

limeneli lodzichepetsa silichotsera atsogoleri ayi). Muyenera kuuza mnzanu kuti “timangoononga

ntchito ya Mulungu ndi Kupunthwitsa ena ngati tipitirira kusungirana udani. Ine ndifuna kuti

tiyambe kukhalirana bwino iwe ndi ine. Kodi titani pamenepa?

M. Khululukirani moonadi iwo omwe akulakwirani – Mateyu 18:21-35. Mulungu

sangakukhululukireni ngati inu simukhululukira. Zindikirani kuti kukhululuka sichinthu

chongomveka m’thupi ndi m’maganizo mwanu chabe koma ndi chinthu chomwe munthu

amachita kusankha kuti achite.

N. Lumikizanani ngakhale mnzanuyo sakutero. Khalani okonzekera kulandira mnzanuyo, siyani

chitseko chikhale chotsekula nthawi zonse.

O. Chitani zabwino ndipo mukhale achifundo ngakhale mnzanuyo akuchitireni zoipa zotani.

Musabwezere choipa ndi choipa chinzake, koma ndi chabwino gonjetsani choipacho – Aroma

12:17-21.

P. Mudzitha kukhala tcheru pofulumira kuona nthawi zomwe ena akumva kuwawa, kaya

kulimbana, ndiponso pamene akukumana ndi nyengo zowawa, ndipo muonetse mtima

wachifundo. Musangokhala omangiririka ku zinthu zanu zokha zokondweretsa inu nokha

mpakana kuchita kuiwala osatha kuona mabvuto a ena.

Q. Ganizirani njira zoonetsera chikondi ndi kuganizira ena. Chikhale cholinga chanu kuti nthawi

zonse mukhale monga wolimbikitsa ndi wochangamutsa munjira yomwe muyankhulira ndi

kuchitira.

R. Muzikhala ndi maphunziro a Baibulo olongosoka ndinso mapemphero pamodzi ndi atsogoleri ena onse. Izi zidzakuikani inu kufupi ndi Mulungu ndiponso pakati pa wina ndi mnzake.

S. Khalani ndi nthawi zapadera zomachezerana, kubindikira pamodzi ndinso kusangalala ndi

atsogoleri ena (monga mwa chitsanzo, mabanja awiri kuyenderana kumapeto a sabata). Izi

zimalimbikitsa ubale.

T. Zindikirani kuti anthu ena ndi obvuta kumvetsa zinthu. Anthu ena samalola kuti chisomo

chiwasinthe kwatunthu mumtima mwawo. Zindikirani kuti muyenera kukhala ndi moyo

wodziletsa ndi wolimba kuti musaonetse kupsa mtima kwanu kwa anthu oterewa ndi cholinga

chofuna kuwaonetsa chitsanzo chanu chabwino ndi kutinso ntchito ya Khristu isasautsike.

Yesetsani kutchinjiriza moyo wanu ndi kuusunga bwino poyambirira pomwe musanapse mtima –

Izi zimakhala zosabvutirapo

U. Ngati mukukaikira, nthawi zonse tsatirani lamulo labwino ndi loyenera kusungidwa iri:

“muzonse, chitirani ena zomwe mungakondwere iwo atakuchitirani.” – Mateyu 7:12;

tawerengani ndi kufaniziranso ndi Mateyu 22:39.

2. Maganizo ena oti mlaliki achite nawo pankhani ya ubale wake ndi oyang’anira/abusa.

A. Alemekezeni abusa ndi mawu ambiri. Ngati mungathe kuwalola kuti akuyang’anireni pa ntchito

Page 16: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 16

yomwe mukugwira, teroni. Mutha kuyankhula nawo molimbikira mfundo yanu, koma nthawi

zonse munjira yaulemu. Ngati muli nawo bvuto, yankhula nawoni abusawo kapena mmodzi wa

iwo osati kuyamba kumanena za iwo ndi anthu ena.

B. Musataye nthawi pomachita zionetsa kukondweretsedwa ndi mmodzi kapena ena a iwo. Izi

zingathe kuononga ntchito yanu ndi abusawo. Inde malinga ndi chikhalidwe cha munthu, mutha kuzolowerana ndi abusa ena mosiyana ndi ena, komabe muyenera kupereka ulemu mofanana

kwa onsewo. Onanani ndi abusa osiyanasiyana mu nthawi zosiyanasiyana pa nkhani zomwe

sizisowa abusa onsewo pamodzi.

C. Musanyengere abusawo kapena kuwachititsa kuti akukondeni munjira ya dziko kapena mwa

ndale, koma yesetsani kukhala mbale wachilungamo ndi choonadi kwa onsewo.

D. Musawapeputse abusa ngati inu munaphunzira bwino Baibulo kuposa iwo. Koma mugawane

nawo zinthu zabwino mwa Ambuye pamene mungathe kutero, ndi kuwalimbikitsa kukula mu

uzimu. Zinthu zomwe mungagawane nawo zitha kukhala mabukhu, maganizo, makaseti a mawu

a Mulungu, ma autilaini, madongosolo, anthu ndi zina zotere.

E. Mlaliki asataye nthawi ndi kulimbana ndi abusa chifukwa cha ulamuliro kaya kukondedwa.

Ngati anthu amenewa, abusa ndi mlaliki ali wokhwima mu uzimu wa Khristu, iri silimakhala

bvuto kwa iwo. Mwina ngati bvutoli liripo, aliyense wokhudzidwa achite ndi mzimu wake ku

mbali yake.

F. Ziri kwa abusa kuitana alaliki ku misonkhano yawo kapena ayi. Koma sayenera kuitana mlaliki

ku msonkhano womwe nkhani yake iri kuyang’ana mlalikiyo. Komabe pamene pali ubale

wabwino, abusa ambiri amasangalala poitana mlaliki chifukwa chakumvetsa kwake ndi udindo

wake pa mpingopo. Izi zimakhala zoona pamene abusa ake akuwetadi nkhosa mwa uzimu osati

omangochita misonkhano yongofuna kumanga mfundo wamba. Onsewo ndi ogwira ntchito a

mpingo, ndipo mlaliki monga wodziwa bwino za nkhosa zapampingopo, angathe kukhala

thandizo la mtengo wapatali kwa abusawo popanda kusokoneza dera la udindo wawo.

G. Alaliki omwe angosankhidwa kumene ayenera azibweretsa pang’onopang’ono maganizo awo

akusintha kwa ntchito zina za mpingo. Perekani nthawi yokwanira musanayambe zina, poonetsa

ulemu.

H. Ngati mpingo umapereka chithandizo kwa mlaliki, mlalikiyo ayenera adzigwiradi ntchitoyo.

Popeza nthawi zambiri amagwira popanda woyang’anira, ayenera aziyambitsa yekha ntchito zambiri. Ayenera kumagwira ntchito nthawi yake yonse ngati alandira chithandizo pa zosowa

zake zonse. Mlaliki asamajombe pa ntchito ya mpingo chifukwa cha ntchito zake zathupi kaya

bizinesi yake. Nthawi yomweyonso, abusa ayenera kuzindikira kuti kufunika kwa mlaliki

kumasinthasintha malingana ndi nthawi, choncho sangathe kusunga dongosolo lokhazikika

(ngakhale kuli koyenera kuti azisunga dongosolo labwino). Ngati mlaliki ali wodzipereka nthawi

zonse, abusa asamuimbe mlandu ngati nthawi zina agwira ntchito zapakhomo pake munthawi in

yatsiku lomwe kulibe ntchito zazikulu. Ayenera kukumbukira kuti amagwira ntchito munthawi

zambiri zausiku posawerengera masana ndi zina zotero. Koma izi zisachitike mopitirira.

I. Mlaliki ayenera kuchita dongosolo lomadziwitsa abusa pa kusintha kwa madongosolo a ntchito

zake monga maulendo opita kwina, maulaliki a nyumba ndi nyumba, ndi zina zotero, ngakhale

ngati maulendowo anali obvomerezeka. Izi zimathandiza kupewa kusamvetsetsana.

J. Ayeneranso kupereka dongosolo lokambirana ndi abusa mfundo ziri zonse zazikulu zomwe

afuna kuchita, zomwe ziri zoyenera kukambidwa pakati pawo.

K. Mlaliki ayenera aphunzire kusunga chisomo pamene mfundo zomwe anakonza zakanidwa ndi

abusa. Abusa angathe kumva zinthu mosiyana ndi momwe iye akumvera, komabe munjira

iriyonse, palibe yemwe adzingokhalira kuchita zake zokha nthawi zonse. Mlaliki asakhale

wowinya ngati mfundo zake sizinamveredwe.

Page 17: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 17

L. Ngati mbusa mmodzi kapena abusa angapo nthawi zonse angotsutsa kapena kulimbana ndi

mfundo zonse zomwe mlaliki apereka, pamenepa mlaliki angolimbikira pa mfundo zomwe iwo

agwirizana nazozo kuti poteropo ayambe kubwererana pafupi ndi kumvetsana

pang’onopang’ono. Kuganizirana zina ndi zina kungathe kuzima ngati mlaliki atsatira njira

zobweretsa chiyanjano nayesa mwa choonadi kukondweretsa enawo. “Gonjetsani choipa ndi

chabwino” – Aroma 12. Musalole maganizo owawa akhazikike mkati mwanu poganizira mbusa kapena abusa, chifukwa izi zidzalepheretsa kuti mugwire nawo bwino ntchito.

M. Mlaliki ayenera kuyesetsa kumvera zomwe abusa afuna momwe angathere, ndipo ndi mtima

wofunadi. Koma ngati ali ndi bvuto lachikumbumtima ndipo sangathe kuchita zomwe iwo afuna,

ayenera wachifundo koma moona mtima kufotokoza bwino kwa iwo ndi kupempha kuti ayese

kumukomera mtima. Ngati apempha mwa mzimu wabwino, iwonso adzamumvera ndi

kulemekeza pempho lakelo. Chirichonse chingatheke kukonzedwa pokambirana munjira

yabwino popanda kukhumudwitsana.

N. Ngati pali bvuto lalikulu pakati pa mlaliki ndi mpingo kapena abusa loti kusiya ntchito yake

kungakhale ngati njira yabwino, ayenera kukambirana moona ndimosasuka ndi abusa ndipo iwo

onse pamodzi ayesere njira zonse zoti ziwathandize kukonza ndi kuthetsa bvuto lawolo.

Chimodzi modzinso ngati bawo abusa ali ndi bvuto longa lomweli ndi alaliki.

O. Nthawi zina njira yothandiza imakhala yosiya ntchito – Machitidwe 15:36-41. Ngati mlaliki

waona kuti nkwabwino kupuma ntchito, ayenera kutero popanda kuyambitsa maganizo achabe

kapena kugawanitsa mpingo. Pa nthawi yobvuta imeneyi, zambiri zidzadalira momwe iye

asungira lirime lake. Ndipo ngakhale kuti abusa ndi mlaliki agwira ntchito zolekana kuyambira

pamenepa, iwo ayenerabe ngati nkutheka kusunga ubale weniweni. Ayenera kukhazikitsa ubale

ndi Chiyanjano asanalekane.

P. Pamene mlaliki ndi mpingo alekana, pasapezeke m’modzi wonenanena zambiri kwa akunja ndi

onse omwe siziwakhudza mosayenera kapena kusiya mbiri yachabe.

Q. Mlaliki ayenera apereke nthawi yokwanira kuti mpingo uthe kupeza wantchito wina, ndipo

mpingo uyenera kumpatsa mlaliki nthawi yoti akonze madongosolo atsopano.

R. Alaliki ndi abusa ayenera kukhala ndi zolembera za mapangano awo pa zomwe wina

angayembekezere kwa wina pofuna kupewa zosagwirizana zina ndi zina.

3. Maganizo ena oti abusa achite nawo pankhani ya ubale wawo ndi alaliki.

A. Yesetsani kumvetsa ndi kulemekeza maganizo a mlaliki, ngakhale pamene simubvomerezana

nawo nthawi zonse.

1) Nthawi zonse mlaliki amakhala kuti anaphunzitsidwa kuyesetsa kugwiritsa ntchito

malemba mobvomerezeka pofunafuna ndi kukulitsa mizimu yambiri. Nchachidziwikire

kuti abusa sangamvere maganizo onse omwe mlaliki angapereke, koma pomangotsutsa

nthawi zonse ndi kumangonena-nena za maganizowa, abusa amakhumudwitsa ndi

kugwetsa mphwayi antchito achinyamata abwino ndipo nthawi zambiri kupangitsa kuti

asiye ndi kuchoka m’chiyanjano chathu kapena kusiyananso utumiki kwathu. Abusa

ayenera kupewa msampha wodziona ngati atetezi a zochitika kokha. Abusa nawonso ndi

atsogoleri ndipo monga achitira mlaliki ayeneranso kumafunafuna njira zoberekera

zipatso.

2) Abusa ayenera kubvomereza kuti ndi momwe zimakhalira monga mwa chilengedwe kuti

mlaliki amakhala ndi maganizo amphamvu, atsopano. Ena. Ena amakhala abwino, ena

ayi. Abusa ayeneranso kukumbukira kuti kumatheka kuti mbusa akhale ndi maganizo

akale otopa, kukhala wozolowera zomwe zomwezo, kuopa kugwira ntchito mwa

mphamvu, kapena kuwalola kuchepetsa kapena kusiya kumene kulamulira magawo ena

antchito yake. Abusa ayenera kukhala ndi maganizo sinthika pa nkhani zimenezi ndi

Page 18: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 18

zizolowezi zimenezi. Atatero ndiye kuti zidzamuthandiza kugwirizana bwino ndi mlaliki

ndipo zidzamthandiza kubvomereza pamene alaliki akana kulandira maganizo ake.

B. Abusa ayenera kulemekeza maphunziro ndi zonse zomwe mlaliki adziwe, mphatso ndi maluso

osiyanasiyana a mlaliki. Ngakhale sangathe kubvomera zonse, ayenera adzikhala ndi chidwi

chomvera moona maganizo akewo. Nati afuna kukonza bwino kapena kukana kumene maganizo amlaliki, ayenera kutero m'njira yoti sikhumudwitsa mlaliki. Kudekha ndi kudzichepetsa ndi

zofunika kwa abusa monga ziriri kwa Akhristu ena onse.

C. Abusa ayenera kuganizira za zosowa za mlaliki pachuma ndi nthawi ndi banja lake. Ayenera

kumlimbikitsa kuti aziwauza za zosowa zake momasuka ndi moona. Utumiki wake

umamutengera nthawi yake yokhala ndi banja lake, ndipo abusa ayenera kumamvetsa pamene

mlaliki asowa kuchitako zina za kubanja kwake. Abusa ayenera kukonza dongosolo la masiku

omwe mlaliki ayenera kupuma ndi nthawi yoti ayendere malo ena monga kupumula.

D. Abusa ayenera kukonza dongosolo loti amve maganizo a mlaliki pa za alaliki ena omwe

angaitanidwe ku misonkhano ndi zokambirana zina. Mlaliki angathe kudziwa zomwe abusa

asoweka kuti adziwe pa za kufunika kwa mlaliki woitanidwayo pa ntchito ya pampingopo.

E. Ngati mlaliki akulakwitsa, abusa ayenera kumuthandiza modekha koma mwa chimvekere kuti

athe kuona zomwe akuchitazo. Ayenera kugwiritsa ntchito njira yomwe ingamulimbikitse, osati

njira yomwe ingamuvulaze m’maganizo.

4. Maganizo ena othandiza abusa pamodzi ndi alaliki.

A. Ayenera kumalowa ndi kuchita maphunziro pamodzi, kupemphera pamodzi ndi kulowa

m’bindikiro pamodzi kuti athe kuphunzira ndi kufunafuna cholinga cha Mulungu kuti athe

kulunzanitsa maganizo ndi mitima yawo ku zolinga ndi njira zofanana.

B. Abusa ndi alaliki ayenera kumazidziwa okha, akhale omvetsa zokhumba zawo zomwe

zingaonetse kudzikonda, ndipo azindikire zonse zomwe zingawafooketse kapena zofooka zawo

zimene, zamkati mwawo zomwe zingawapangitse kuti akhale odzimva mopitirira kapena kufuna

ulamuliro mopitirira. Ayenera moganiza bwino ndi mwachangu kuthana ndi zizolowezi zimenezi

kuti mwina izi zingaononge ntchito ya Yesu ndi kusokoneza mizimu. – 1 Akorinto 3:16,17.

C. Umodzi pakati pa abusa ndi alaliki uyenera ukhale woti mpingo wonse uchitire umboni monga

chitsanzo chabwino. Ngati pabuka kusamvana pankhani zina, chonde, zimenezi zisadziwike ndi ena onse koma zikhale monga chinsinsi pakati pa atsogoleri kufikira njira yothetsera itapezeka.

Abusa ayenera kuthandizira mlaliki monga momwe angathere pamaso pa mpingo monganso

momwe mlaliki naye angachitire.

5. Maganizo ena othandiza pakati pa mlaliki ndi alaliki enawo.

A. Ngati alaliki awiri agwirira ntchito pamodzi, nchachidziwikire kuti zikhala ngati zija za atambala

awiri mkhola limodzi. Amalimbana mpaka mmodzi aoneke wamwamuna. Moyo umenewu

womwe ndi wathupi, wokonda kulimbana, ulibe malo ndi nthawi pakati pa antchito a Yesu ndipo

uyenera kuthetsedweratu mwa kulapa ndi mzimu woyera. – Agalatiya 5:19-26.

B. Mlaliki ayenera kutaya khalidwe lonse la nsanje ndi kaduka pa mlaliki mnzake yemwe ali ndi

nzeru ndi maganizo oposa mnzakeyo. Iye ayenera kukondwera chifukwa mlaliki mnzakeyo

akutha kutumikira Mulungu mwangwiro. Dziwani kuti tonse tiri m’gulu limodzi.

C. Mlaliki asataye nthawi yake pomabvutika mumtima chifukwa mlaliki wina akuthandizidwa

kapena akulemekezedwa bwino, kapena akuchitidwa bwino munjira iriyonse. Mtumiki wa

Mulungu akhale wokhutitsidwa pololera kuti Mulungu akhale wokonza ndi Kulongosola za

ulemu ndi thandizo lomwe iye angalandire, ndi bwino kungoganizira kwambiri za ntchito yake

yotengera chipulumutso cha Yesu kwa anthu. Tiyenera kutaya ufulu ndi ulemu wathu monganso

Page 19: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 19

adachitira Yesu – Afilipi 2:5-11; Yohane 3:26-30.

D. Mlaliki yemwe ndi mlendo pa malopo ayenera kutsogoleredwa m’njira iriyonse yofunikira ndi

mlaliki wa pamalopo, iye ndi yemwe angalondolere kwa anthu omwe ayenera kuyenderedwa, ndi

zina zotumikira za uzimu pa mpingopo, ndi zina zotero. Mlaliki wodzachezayo, ngati ali ndi

mzimu wabwino, amabwera kudzatumikira, ndipo adzabvomera maganizo amlaliki wa pamaloyo.

Mawu otsiriza: Nkutheka kuti kudzera mu ubale wapakati pa anthu kuposa m’njira iri yonse, atsogoleri ndiwo

ali ndi mwayi woonetsa dziko zoonadi ndi kukoma kwake kwenikweni kwa ziphunzitso za Ambuye wathu

Yesu Khristu.

Umodzi Pakati pa Ogwira Ntchito Gawo Lachinayi: Zomwe Tingachite ndi Zolimbana.

Yesu nthawi zonse ankachenjeza ophunzira ake za mabvuto, zotsutsa ndi za mayesero omwe atumiki ake anali

kudzakomana nawo. Sanayesere ndi pang’ono pomwe kungowaika m'masamba kuti iwo aganize kuti iwo

adzakhala akupambana mosabvuta ndi mwa chisangalalo – Mateyu 10:16-42; Luka 9:57-62. Koma iye

anawalonjeza za chisomo ndi thandizo loti adzathe kuchita bwino, ndipo anawaonetsa kuti adziwe kuti

ntchitoyo pamodzi ndi mphoto yakeyo ndi zoyenera kubvutikiridwa. Nkhondo ya uzimu ifanana ndi nkhondo

zina zonse. Pamakhala kulimbana, zobvuta ndi zoopsa zomwe. Komabe iyenera kukhalapo basi ndipo

koyenera. Msirikali aliyense amakhala ndi zolinga ziwiri pa nkhondo yake, choyamba chimakhala chofuna

kugonjetsa mdani, ndipo chachiwiri kudziteteza kuti asagonjetsedwe.

1. Momwe tingachitire ndi zotsutsana.

A. Tiyenera kukonzekera kukomana ndi zolimbana – 2 Timoteo 3:12; Luka 6:22-26; Mateyu

10:16,34-36; Machitidwe 20:23; 1 Akorinto 16:8,9; Marko 10:29,30; Aefeso 6:10-12; 2 Timoteo

2:3; Yohane 3:19; Yohane 15:20.

B. Kutsutsana kulipo kwa mitundu ndi mphamvu zosiyanasiyana.

1) Kwina ndi komwe mumachita ku kuyamba nokha chifukwa cha kupusa kwanu, kufooka

kwanu kapena kuchimwa kwanu.

2) Kwina ndi komwe kumachokera kwa abale ofooka komabe olimbikira omangiririka ku

ziphunztso ndi zizolowezi za anthu, kusakhwima kapena kukhala ndi mtima wokhulupirira

kwambiri zinthu zadziko. Tawerengani Mateyu 16:21-23; ndipo mufanizire.

3) Kwina ndi komwe kumayamba pamene muputa anthu omwe ndi omangiririka ku

zolimbana, zofuna zawo ndi osakasaka chisangalalo ndi ulemerero.

4) Kwina ndi komwe kumayambitsidwa ndi choipa chomwe chimakhazikika kwa anthu koma

ndi kumaoneka ngati ndi chauzimu.

C. Dongosolo lothandiza pochita ndi kugonjetsera zotsutsana pa utumiki wanu wa Yesu.

1) Nthawi zonse muyambe ndi kupempha nzeru kwa Mulungu, ndi kukhulupirira Iye

adzaperekadi – Yakobo 1:5-8 (kutsutsa kumatithandiza potipangitsa kuti tidalire Mulungu).

2) Yeretsani moyo wanu ndi mtima wanu kuti mukhale okhulupiriradi za Chiyanjano chanu

ndi Yesu ndinso chithandizo chake. “musasiye malo ena alionse, ngakhale kufooka kwina

kuli konse kwa mzimu.” – Aefeso 6:10-18; Yohane 14:30.

3) Chotsani mwa inu chirichonse cholakwika chomwe chingathe kumayambitsa kapena

kuthandizira pa zotsutsana – Machitidwe 24:16; 1 Akorinto 10:31-33; 11:1.

Page 20: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 20

a. Mwapemphero, moona, fufuzani moyo wanu ndi womwe mumafikira enawo – 2

Akorinto 13:5; Mateyu 7:5. Kodi mumangochita zinthu potsatira zomwe thupi ndi

maganizo anu afuna mosalingalira bwino, kodi mumachita zinthu mopupuluma, kodi

mukusowa moyo wa chisomo pa makhalidwe anu, kodi mukusowa kudzichepetsa

ndi kuupeza mtima, kusagwirizana ndi zina, kukondera, kukhulupirira ndi kumva

zanu zokha? Kutsutsidwa kumatithandiza kuti tikhale ndi mwayi wokonzanso moyo ndi khalidwe lathu.

b. Ngakhale pamene mnzathuyo watilakwira, tiyeni tidzifulumiza kupeza njira

yothetsera bvutolo ife tokha. Kumakhala kobvuta kuti tiwasinthe ena mwa msanga

nthawi zonse, koma mungathe kudzisintha nokha, kusintha momwe muchitira ndi

ena akakulakwirani ndinso machitidwe anu pa nthawi yotsutsidwa.

4) Khalani msirikali wodalira nkhondo – Aefeso 6:18; Akolose 4:12. Pemphero la

wolungama lingathe kuchotsa mapiri a zolimbana – Marko 11:20-25. Pamene muli ndi

bvuto lalikulu, chitani nalo mwa kusala kudya ndi pemphero (komatu mukhale oupeza

mtima ndi okhazikika m’maganizo pa kusala kwanuko – chifukwa njirayi iribe tsenga liri

lonse.) Mulungu amakonda mapemphero a iwo amene amakonda mpingo ndi mizimu ya

otayika ndi ofooka.

5) “Pita kwa mbale wako” – Mateyu 18:15-17; 5:25; Aefeso 4:26-27. Musanene kwa ena

zambiri za yemwe akukutsutsaniyo – yankhula nayeni. Konzani zolimbana zanu

mwachangu zisanafike poopsa, makamaka pamene mwangoyamba kumene kudabwa,

musanayambe kukayikirana koti zinthu zifike pobereka uchimo waukulu. Konzani msanga

ming’alu ya ubale wanu isanasanduke mipata yaikulu ndi kugwetsa khoma lonse. Koma

pitani ndi kudekha konse – Agalatiya 6:1. Mapitidwe amenewa amafunika kudzichepetsa.

Ngati mutatsatira njira imeneyi yolumikizana ndi mbale wanuyo, kuphatikizana ndi

kupepesa kwanu, ndiye kuti mbale wanuyo adzakhala ndi mwayi waukulu womvetsa

momwe inu mumamukondera. Ngati muchita ndi zolimbana zanu mwathupi osati mwa

malemba, ndiye kuti zimangokhala ngati mwapereka mwayi wothira mafuta anyali pa moto

wa mumtima mwa yemwe mukutsutsana nayeyo. Pewani kutsutsana ndi kulimbana poyera,

koma ngati zingatheke zosakhudza mpingo ndi ubale wanu.

6) Musalimbane kapena kuchita makani – Mateyu 12:18-21; 2 Timoteo 2:24-26. Gwiritsani

ntchito kudandaulira mwachikondi ndi choonadi choperekedwa mwa chifatso.

Musatengeke mtima ndi kuyamba kuonetsa khalidwe lofanana ndi yemwe akukutsutsaniyo

lomwe ndi loipa. Musabwezere choipa ndi choipa – Aroma 12:17-20. Musachiyese chosangalatsa ngati mugonjetsa mnzanu molimbana.

7) Funani Mzimu Woyera kuti uthandize inu ndi anzanu, chifukwa umodzi ndi wa Mzimu –

Aefeso 4:3; Agalatiya 5:22,23; 2 Akorinto 13:14; Luka 11:13.

8) “Gonjetsani choipa ndi chabwino” – aroma 12:21. Pemphererani adani anu. Kumbukirani

chitsanzo chomwe Ambuye Yesu anaonetsa pamene anazunzidwa ndi kunyozedwa – 1

Petro 2:21-25. Perekani ka Mulungu zolinga zanu zonse, nthawi zonse chitani zabwino

ndipo wongolerani bwino mzimu wanu. Palibe chifukwa chokubvomerani kuchita zoipa

chifukwa choti winanso akuchita zoipazo. Kuchitidwa zoipa chifukwa choti muli ndi

mzimu monga wa Ambuye Yesu ndi phunziro lalikulu lomwe mudzayenera kuchita.

9) Phunzirani kunena zoona zokhazokha momveka bwino ndi mwachikondi. Aefeso 4:15.

Mungathe kuyankhula muli monse mungafunire ngati muyankhula mokhoza ndi

mwabwino. Yankho loperekedwa modekha limatha kuthetsa kulimbana – Miyambo 15:1.

Mzimu amatithandiza kuyankhulana ndi kumvana bwino mothandiza ndi moombolana.

10) Zoyambitsa kulimbana zina ndi zoti mutha kungozinyalanyaza ndi kuziiwala ngati

mwayesa yesa njira zinazo – Nehemiya 6:1-13.

Page 21: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 21

11) Ngati abale ali otsamira ndi kukhulupirira kwambiri pa miyambo ya makolo komabe

kwinaku ali nacho chikondi cha pa Mulungu, ziripo njira zina zomwe inunso mungachite

popanda kuwalakwira, kapena palinso njira ndi nzeru zina zomwe mungathe kukwaniritsa

zabwino pamene mukudikira ifike nthawi yoti njira itsekuke. Mudziganizira za

chikumbumtima cha abale monga momwe mungathere (Ngakhale kuti izi zichitike

molingana ndi udindo wanu pamaso pa Mulungu kuti mukathe kufikira otayikawo munjira ya uzimu.)

12) Samalirani pa zomwe mumayankhula kwa anthu pokhuza za omwe amakutsutsani. Ngati

simusamala mungathe kufesa mbewu zamnyozo chifukwa anthutu amamva zinthu

mwachangu. Mudziwenso kuti zomwe muyankhulazo tsiku lina zidzapeza yemwe

mukumunenayo.

13) Muzolowerane ndi osadziwa ndi ofooka powaphunzitsa modekha ndi mofatsatsirira bwino,

kuwadyetsa ndi kuwaonetsera chitsanzo chabwino. Pamene ofookawo ayesera kuchitako

bwino, ayamikireni.

14) Dandaulirani mfundo zomwe inu ndi okutsutsaniwo mungathe kugwirizana ndipo

mulimbike kugwira ntchito mu mfundo zimenezi ndi mtima wonse.

15) Taphunzirani ndi kuona momwe Yesu ndi ophunzira ake anamchitira ndi nthawi zobvuta

zomwe anali kutsutsidwa. Kodi ndi nthawi ziti zomwe anali kukana kugonja? Ndipo ndi

nthawi ziti zomwe anali kulolera kufooka kwa anthu?

16) Samalirani mwakuopa Mulungu momwe muweruzira okutsutsani, makamaka pa zokhudza

maganizo awo – Yohane 7:24; Mateyu 7:1-5; Yakobo 2:12,13. samalirani kuti

musafulumize kukhulupirira zomwe mumva za miseche yochokera kwa olimbana nanuwo.

Fufuzani kokwanira musanagwiritse ntchito zokumvazo.

17) Chenjerani kuti pasayambike magulu kapena timabungwe pakati pa abale ndi alongo

chifukwa chokhala ndi maganizo osiyana pakulimbana. Musakolezere moto pakutsutsana

ndi kulekana kwa anthu.

18) Pezani malangizo kwa oyera mtima odalilika ndi atsogoleri a akulu.

19) Musapangitse banja lanu kuti likhale ndi mkwiyo wa pa omwe mutsutsana nawowo kapena

mpingo chifukwa kayankhulidwe kanu. Phunzirani kupempherera ndi kufunira adani anu zabwino pamodzi ndi banja lanu lonse (pali nkhani zina zoti zimuyenera kukambirana ndi

ana anu aang’ono ndiponso zina ngakhale aakulu amene).

20) Potsiriza, pamene mwa ona kuti kutsutsako kukuchokera mkati weniweni mwa choipa,

ndipo mfundo zofunikira kapena mtendere wa ntchito za mpingo ungathe kusokonezeka,

iripo tsopano nthawi pamene zonse zalephereka yochotsera choipacho ndi kufotokozera

momveka bwino, posiya matsutso agwere komwe ayenera kugwera – Mateyu 23;

Machitidwe 13:6-12; Agalatiya 2:11-13.

a. Muyenera mutsikize kuti mukulondola ndi kuti mfundo za mpingo zikuopsezeka.

b. Tengani maganizo a anthu a mtima wolondola.

c. Mukhale okonzekera kulandira zotsatira zake.

d. Yesetsani kupanga zoti zisasokoneze kwambiri mpingo (mwa chitsanzo, ngati musiya

utumiki wanu, ndi chanzeru kuchoka ndi kumakasonkhana ku malo ena ampingo

womwewo wa Yesu koposa kukhala chida chothandiza kugawa anthu).

e. Yesetsani kuti ubale wanu wonse ukhale wosaonongeka kuti ubale wanunso ndi

Mulungu usaonongeke

Page 22: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 22

21) Perekani moyo wanu ndi zolinga zanu kwa Mulungu – 1 Yohane 4:4; 1 Petro 2:23;

Masalmo 23:5.

22) Lolerani kulakwiridwa kapena kulakwira chifukwa cha Mulungu ndi cholinga chake, koma

osati chifukwa chofuna kukwaniritsa zolinga zanu. Muzidziwa kusiyana kwake!

Mu utumiki, zambiri ndi zosautsa ndi zokhumudwitsa. Komabe zimenezi sizingafanizidwe ndi chisomo cha

Khristu Yesu chomwe chaperekedwa kuti chitithandize ngakhale ndi chisangalalo chomwe utumiki

wopambana umabweretsa ku mizimu ya anthu.

Phunziro 5: Umodzi mu Mpingo wa Pamalo Gawo 1: Mzimu wa Utumiki wa Khristu

Chinthu chapamwamba chopusa zonse pa mpingo womwe ndi wogwirizana kapena pa banja ndi moyo

wotumikira wa Khristu. Mabvuto ambiri m’mipingo ndi m’mabanja amabadwa kukuchokera ku uchimo,

kudzikuza, ndi kudzikonda. Akhristu ali nayo njira yamphamvu yothetsera zimenezi kudzera m'moyo wa Yesu womwe uyenera kumabadwa m’miyoyo yathu. Palibe njira zopezekeratu “za mayankho ododometsa” ku

mabvuto am’mipingo ndi m’mabanja ndiponso palibe lonjezo lirilonse lomwe lingabweretse kusintha kwa

zinthu popanda kudzipereka kwa Ambuye kuti atilamule. Koma pokhala pansi pa iye monga Ambuye wathu

ndikutsatira chitsanzo chake, mipingo yathu ndi mabanja athu angathe kukhala ogwirizana monga momwe

Mulungu anakonzera! Mu phunziro loyambali tidzayang’ana za maziko a umodzi, moyo wotumikira wa Yesu.

1. Khristu anali nawo ufulu monga Mulungu wokhala kumwamba – Afilipi 2:5-7.; Yohane 1:1,2,14; 17:5.

2. Khristu anasiya padera ulemerero wake mwakufuna kwake ndi cholinga chofuna kuti atithandize –

Afilipi 2:5-8. “Iye anadzikhuthula yekha

A. Iye anabvomera pa chiyambi pomwe ndi Mulungu kuti adzachita zimenezi - Ahebri 10:4-7;

tawerengani Aroma 15:3; 2 Akorinto 8:9; ndipo mufanizire.

B. Izi zimafuna mphamvu zambiri koposa kuumirira ufulu wathu.

C. Pamene tiri kuphunzira chikondi chosadziganizira wekhachi, cha Khristu, moyo umenewu

wotumikirau, tidzatha kukhala ndi khalidwe lomwe mwa njira zina sitikanatha ndi kulikwanitsa

m’mabanja mwathumo.

3. Khristu anakhala wotumikira (kapolo) – Afilipi 2:5-8.

A. Pobadwa monga munthu – Yohane 1:14; Mateyu 1:23.

B. Ponyamula zolemetsa ndi zosowa za anthu ena – Mateyu 8:1-4; Luka 7:11-15; Yohane 8:2-11;

Marko 6:31-34; Mateyu 15:32; Luka 13:10-17; Yohane 5:1-15; Yohane 4:1-38; Luka 22:24-26;

Yohane 13:3-17; Luka 23:39-43.

4. Yesu anadzichepetsa yekha ndipo anamvera mpaka imfa ya pamtanda – Afilipi 2:8.

A. Uku kunali kudzikhuthula kwake kwa Yesu m’moyo wake kwachiwiri.

B. Imfa yake inali yodzipereka yekha, kutisenzera zolakwa zathu pamene ife tinali olephera –

Yesaya 53:3-6.

5. Popeza anataya ulemerero wake wonse kuti apulumutse ena, Mulungu anamukweza iye kopambana ndi

kumubwezera zonse mochuruka. – Afilipi 2:9-11. Ngakhale pakali pano akutisenzerabe zolakwa zathu

ndi kutipempherera – Ahebri 7:25; 1 Petro 5:7.

6. Yesu akutiimiranso ife kumoyo womwewo wodzikhuthula, wotumikira ndi cholinga chofuna

kupulumutsa.

Page 23: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 23

A. Kuti tinyamule zolakwa za ofooka ndi kuti tisadzikondweretse tokha – Aroma 15:1-3;

tawerengani Machitidwe 20:35; 2 Akorinto 12:15.

B. Kuti tikonde ena monganso Khristu anaconda ife – Yohane 13:34; tawerengani 1 Akorinto 13;

Yohane 15:13; 10:11.

C. Kuti tidzikhuthule ndi kunyamula mtanda wa Khalidwe lofuna kuombola ena – Mateyu

16:24,25.

1) Njira yekhayo yotsatira nayo Khristu.

2) Dzikhuthuleni, osangoti machimo okha – Mateyu 16:24; Aroma 6:6; Agalatiya 2:20.

3) Kunyamula mtanda tsiku ndi tsiku – Luka 9:23

4) Ngati titaya moyo wathu chifukwa cha Yesu ndi cha ena onse, timaupezanso.

Mau otsiriza: Kodi ndingathe bwanji kukhala wopulumutsa monga anamchitira Yesu?

1. Mthane ndi zoyambitsa kupunthwa ndi kuchimwa m’moyo wanu – Mateyu 18:6-9.

2. Lapani ndi kusiya moyo wodziganizira nokha ndi kumaukonza nthawi iriyonse pamene muona kuti ufuna

kuyambiranso.

3. Yang’anani kwa Yesu ndi uthenga wake ndipo pemphani thandizo la Mzimu wake – 2 Akorinto 3:18;

Luka 11:13.

Kusinthika kwanu kudzathandiza kuti banja lanu lonse lipulumutsidwe ndi kukonzeka. Nthawi zambiri banja

limasinthika chifukwa cha kusinthika kwa munthu mmodzi wapabanjapo.

Gawo lachiwiri: Utsogoleri Wotumikira.

Mawu oyamba: Yesu anaphunzitsa kuti utsogoleri wa mu ufumu wake ndi wosiyana ndi utsogoleri wa dziko

lapansi.

Ndipo kunakula kutsutsana mwa iwo, ndani wa iwo ayesedwe wamkulu. Ndipo anati kwa iwo, mafumu a anthu

amitundu awachitira ufumu; ndipo iwo amene awachitira ulamuliro anenedwa, ochitira zabwino. Koma

sipadzatero ndi inu; komatu iye ali wamkulu mwa inu akhale ngati wamng’ono; ndi iye ali woyamba, akhale ngati wotumikira. Pakuti wamkuru ndani, iye wakuseyama pachakudya kapena wakutumikirapo? Sindiye

wakuseyama pachakudya kodi? Koma ine ndiri pakati pa inu monga ngati wotumikira. – Luka 22:24-27.

Koma amene aliyense akafuna kukhala wamkulu mwa inu, adzakhala mtumiki wanu; ndipo amene aliyense

akafuna kukhala woyamba mwa inu, adzakhala kapolo wanu; monga mwana wa munthu sanadza

kutumikiridwa koma kutumikira ndi kupereka moyo wake dipo la anthu ambiri. – Mateyu 20:26-28.

Wetani gulu la Mulungu liri mwa inu, ndi kuliyang’anira, osati mokakamiza, koma mwa ufulu, kwa Mulungu;

osatsata phindu lonyansa, koma mwachangu; osati monga ochita ufumu pa iwo a udindo wanu, koma okhala

zitsanzo za gululo. – 1 Petro 5:2,3.

1 Yesu ndiye chitsanzo chathu cha utsogoleri wotumikira – Afilipi 2:5-11; Mateyu 20:28; Aroma 15:1-3.

A. Momwe amachitira ndi unyinji.

B. Anasunga nthawi yoganizira anthu osowa ndipo nthawi zonse ankakhudzidwa kwambiri chifukwa ena

koposa momwe ankadziganizirira yekha.

C. Ankasamalira osauka, osawerengedwa, akunja ndipo ankapeza nthawi yokhala nawo pamodzi.

Page 24: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 24

D. Sanadzikweza yekha kapena kutenga maulemu adziko lapansi.

E. Ngati anakwiya, chinali chifukwa cha Mulungu, osati chake ayi.

F. Kudzichepetsa kwake sikutanthauza kuti anali wofooka ayi. Iye anali mwamuna wolimba koposa

ndinso mphunzitsi wamphamvu yemwe sanaonekepo ndikale lonse. Nthawi zina ankakalipa, koma zinali zoonekeratu kuti zinkachitika m’chikondi, osati chifukwa cha iye mwini ayi.

G. Pamene anakomana ndi mtanda, anatumikira zosowa zathu koposa zofuna zake za iye mwini. Tonse

tikuitanidwa ku moyo woterewu, wokonda ndi kutumikira modzikhuthula – Afilipi 2:5-11; Aroma

15:1-3; Mateyu 16:24,25; Yohane 13:1-17,34.

2. Akhristu sadzaphunzira utumiki pokhapokhapo atsogoleri awo atawaonetsera utumikiwo monga momwe

Yesu anamchitira – Yohane 17:19.

3. Utsogoleri wotumikira sungatheke ku moyo wathu wauchimo wathupi. Ungatheke potsatira moyo

watsopano wofanana ndi Khristu womwe umaperekedwa ndi Mzimu Woyera:

A. Moyo wathu wathupi wa uchimowo umalamulidwa ndi kudzikonda, ndi kunyada – Agalatiya 5:19-

21. Aliyense amafuna kukhala wotsogola, kuti enawo azingotsatira zomwe ife tifuna basi. – Mateyu

18:1-4.

B. Mzimu woyera amabwereka mwa ife chipatso chatsopano cha moyo wofanana ndi Yesu – Agalatiya

2:20.

4. Kodi atsogoleri otumikira amaganiza ndi kuchita motani?

A. Utsogoleri wotumikira sudzikondweretsa okha koma umafunafuna ulemerero wa Mulungu ndi

kuonetsetsa kuti ena apeze bwino – 1 Akorinto 4:8a; Aroma 15:1-3; Yohane 3:26-30.

B. Umalakalaka ndi kukonzekera kutumikira anthu ndi Mulungu – Ahebri 13:17; 1 Petro 5:4; Yakobo

3:7; 1 Timoteo 3:1-7; Tito 1:5-9; 1 Samueli 12:1-3. Mtsogoleri saopa kutumikirana ngati ali

woyeneradi, wosankhidwa munjira yoyenera ndi yobvomerezeka. Mtsogoleri wotumikira saopa

kupereka malipoti okwanira a chuma cha mpingo kumpingowo. Iye amafunsa anthu kuti apereke

maganizo awo kwa iye pa za ntchito ya pampingopo. Mtsogoleri wofana ndi Yesu amabvomera

kudzudzulidwa kothandiza komwe kungathandize utsogoleri wake. Utsogoleri wamtundu umenewu

umabweretsa umodzi mumpingo, pamene utsogoleri wofanana ndi wadziko lapansi umabweretsa kugawikana mumpingo.

C. Utsogoleri wotumikira umapulumutsa.

1) Kutumikira mwachikondi, ndi mopanda kudzikonda kumachita bwino, kumawala bwino m’dziko

lodzitumikira lokha. Kudzikonda ndi kunyada ndi chizindikiro cha moyo wathupi wa uchimo.

2) Anthu analondola Yesu chifukwa anamva mumtima mwawo kuti iwo ofunikira kwa iye. Iye anali

wokhudzidwa kwambiri pa za moyo wawo, osati pa za moyo wake.

3) Anthu amakopeka ndi kukokeredwa ku moyo wokonda, wosadzikonda ndipo amafuna atakhala

ndi khalidwe lotere.

4) Chikondi chotumikira chimasintha anthu pamene palibe china chirichonse chomwe chingathe

kuwasintha – Yohane 12:32; 1 Yohane 4:19; 2 Akorinto 5:14; 1 Petro 3:1-6.

D. Umathana ndi zolimbana mwa chiombolo.(Satana amagwiritsa ntchito kutsutsana moononga, koma

Akhristu odzala ndi chisomo amatenga kutsutsana ngati mwayi wowathandiza kuti aphunzire ndi

kukula.)

Page 25: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 25

1) Sutenga kutsutsana mwa iwo okha. Mtsogoleri wotumikira anadzikhuthula. Nthawi zina Yesu

ankakwiya mwa chifuniro cha Mulungu, koma simunamuona akukwiya mwa chifuniro cha iye

mwini. Mtsogoleri wotumikira amaphunzira kuchokera mukudzudzulidwa pa za Madera omwe

iye ayenera kukonza – Mateyu 7:3-5, ndiponso amaphunzira kungosiya kudzudzula kopanda

phindu kupite, chifukwa anali ndi zinthu zambiri zofunika kuti achite poyamba koposa kudzitcha

wachilungamo. Iye amadziwa kuti onse otsutsana naye si adani ake; Satana, zofooka za munthu, kusadziwa ndiwo ali adani ake.

2) Umalumikiza koposa kusiya monga munthu wathupi wa zamdziko angachitire. Mtsogoleri

wotumikira sayembekezera kuti munthu winayo ndiye ayambe.

3) Pochita ndi wotsutsa, suchita monga mwa nkhondo kuchititsa kuti winayo akane kukambirana

ndi cholinga chodziteteza. Umafikira mwa chilungamo koma modekha poika njira za chimvano –

Agalatiya 6:1,2; 2 Timoteo 2:24-26.

4) Pokonza zoonongeka umagwiritsa ntchito dongosolo lomwe Yesu anatipatsa lothetsera

makangano mwachangu asanakule ndi kuononga kwakukuru. Cholinga choyambirira sichofuna

kuweruza ndi kudzudzula ayi koma kuthetsa kusiyana kwa maganizo kuti asachitinso monga

mwa chifuniro cha Satana – Mateyu 18:15-17; 5:23,24; Aefeso 4:26-27.

E. Mtsogoleri wotumikira amafikirika. Mtsogoleri sachepsa maganizo a ena kapena kukana Mafunso

awo koma amamvetsera ndi kuyankha modekha ndi kudzisunga konse – Yakobo 1:19,20; 3:17;

Aefeso 4:29; 2 Timoteo 2:24-26; 1 Petro 3:15; Afilipi 2:3; Akolose 4:6. Tingathe kulimbikitsa

dongosolo la Mulungu popanda kukhala oweruza aukali.

F. Utsogoleri wotumikira umalemekeza ndi kulolera maganizo osiyana ndi ake a ena pa nkhani zina

zomwe chifukwa cha umunthu wathu wolephera, sitingathe kuzimvetsa ndi kuzimasulira bwino,

zomwe siziri zofunika kwenikweni ku chikhulupiriro chathu. Nkofunika ndipo nkoyenera kuti

Mkhristu aliyense wokhulupirika ndi wodalilika aone zinthu zimenezi mosiyana. Mtsogoleri

wotumikira amadziwa kuti iye wangokhala munthu mmodzi m’gulu la anthu otumikira mofanana,

okhulupirira olemekezeka, ndipo sadzakakamiza anzakewo kuti akhulupirire ndi kukhala ndi

maganizo onga akewo pa zinthu zomwe zioneka monga zochepera mphamvu, kapena kuti akhale ndi

maganizo ofanana ndi ake pa momwe iye amvera Baibulo.

G. Utsogoleri wotumikira sulamulira ena kuti atsatire njira yake. Koma mtsogoleri amamvera ndipo

amakamba poyera, pofotokozera chifukwa chomwe iye amaganizira munjira yakutiyakuti. Amadziwa

kuti sichikhala chinthu wamtengo wapatali ngati angomvera mongomukondweretsa koma amvere mochokera pansi pa mtima wawo. – 2 Akorinto 3:17. Anthu omwe amatsutsana naye mwa

chilungamo amalandirabe ulemu wake.

H. Umakonda kukopa ndi kudandaulira momwe ungathere koposa kulamula – 2 Akorinto 13:10.

Utsogoleri weniweni suchita kupemphedwa m'njira iyiyonse. Umapezeka polandira ulemu wa iwo

omwe tiwatsogolera.

I. Umakhala ndi chidwi chogawana ntchito yotsogolera ndi kulekera nsakali kwa m’badwo wobwerawo

– 2 Timoteo 2:2.

1) Mipingo yambiri ikufa chifukwa asogoleri ake onse akula ndipo ayamba njira zawo zawo ndipo

akukanika kupereka mwayi kuti anthu aang’ono ndi maganizo a anthu ang’ono abwere

mumpingo.

2) Atsogoleri otumikira nthawi zambiri, ndi cholinga, amaphunzitsa atsogoleri aang’ono ndi

kumagawana nawo ntchito ndi maudindo kuphatikizapo ufulu woti athandizepo kukonza

dongosolo la tsogolo la mpingo (atsogoleri omwe lero akulawa, nawonso ankafuna ufulu

womwewo pamene anali kuyamba kumene).

Mawu otsiriza: Maganizo ndi njira za Mulungu ndi zosiyana ndi zathu – Yesaya 55:8,9. Utsogoleri womwe

cholinga chake ndi kutumikira ndi wamphamvu kuposa utsogoleri wina wamtundu uliwonse womwe

Page 26: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 26

mungaudziwe. Unamthandiza Yesu kusiya chitsanzo chosaiwalika mpaka kalekale padziko lapansi, ndipo

udzatithandiza kutsogolera mpingo mwa mphamvu ndi mofuna kubweretsa anthu kuchiombolo, kuti tithe

kupyola ku zopunthwitsa zomwe sitikanatha kuzidutsa mu njira iriyonse, ndi kuwakopa anthu kuti akhale ndi

chidwi cholondola ndikutsatira. Kumvetsa zinthu zimenezi nkwamtengo wapatali koposa dongosolo lina liri

lonse.

Gawo lachitatu: Kupasirana Nsakali: Kumwetulirana Kapena Kuponyerana Nkhondo? (Kupewa Kulimbana kwa Pakati pa Atsopano ndi Akale.)

Sauli anamponyera nkondo Davide, chifukwa sanakondwere poganiza kuti Davide adzalowa ufumu wake tsiku

lina. Herodei anapha unyinji wa makanda a ku Betlehemu pamodzi ndi akubanja kwake komwe posakondwera

ndi kubvomera ganizo loti iye sadzakhala wolamulira mpaka kale kale, ena adzayeneranso kudzatenga malo

ake.

Kumbali inayi, tiona Eli wansembe wamkulu, mosiyana ndi omwe tamvawa, akudzipereka yekha pophunzitsa

Samueli mnyamata kuti adzakhale mtsogoleri wamawa. Eliya adaphunzitsa Elisa kuti adzatenge malo ake ndi

kupitiriza ntchito yake mtsogolo. Nawonso Elisa ndi Samueli anaphunzitsa pa sukulu yokonzekera aneneri

amtsogolo. Mtumwi Paulo analimbikitsa gulu la alaliki ang’onoang’ono ndi aphunzitsi omwe oti adzapitirize

kufalitsa uthenga wabwino pamene Paulo amwalira. Anali wokondwera chifukwa cha iwo. Ndipo anali

kumawapempherera. Kwa Timoteo monga wophunzira wake wopambana, anamlembera kuti, “zonse zomwe

wandimva ndikulankhula pamaso pa mboni zambiri uikize kwa anthu okhulupirika amene adzakhoza

kuphunzitsanso ena.”

1. Ife omwe tagwira ntchitoyi kwa nthawi yaitali tikadakonda tikupitirizabe kugwira ntchitoyi.

Sitikondweretsedwa kumva kapena kuganizira zakufooka kwathu. Koma tsopano taonani tisanazindikire za

kuzilala kwa mphamvu zathuku, timafika mundime yoti mphamvu zathu zimayambabe kulowa pansi.

Mphamvu zathu zimayamba kulephera. Timayamba kumangobwereza zomwezo zakale m’malo

moganizirabe njira zina zatsopano. Timayamba kusowa mphamvu za achinyamata kuti ayeserere ndi

kuganizira ndi kumanga. Timangoyamba kumayang’ana za m’mbuyo m’malo moyang’ana zamtsogolo. Sitithanso kumvetsa za makono zomwe ndi zofunikira. Timatopa msanga.

Choncho tiyenera kusiyira ntchitoyi ku m’badwo winawu. Koma tiri nawo mwayi wosankha njira yake

yochitira zimenezi. Tingathe kusiyira nsakali ya ntchitoyi mwa chisomo ndi mwanzeru kapena tingathe

kumakana zimenezi ndi kumangokhalira kulimbana ndi achinyamata, kumawatenga ngati adani. Pamene

tisankha njira imeneyi mpingo umabvutika ndipo umalipira dipo loopsa kwambiri.

2. Mulungu safuna kuti mpingo ugawikane pakati pa mibadwo mibadwo. Monga momwe uthenga wabwino

uyanjanitsa ndi kulumikizira mitundu ya anthu yosiyanasiyana, amuna ndi akazi, anthu azikhalidwe

zosiyana, umalumikiza ndi kuyanjanitsanso aakulu ndi achinyamata m’chikondi cha kwa aliyense ndi

cholinga. Ngati kukula msinkhu kuli nazo zofooka zake, kuli nachonso chuma chamtengo wapatali, ndicho

nzeru. Achinyamata ayenera kumvera mwa ulemu malangizo a achikulire. Nawonso achikulire ayenera

kulemekeza zolakalaka ndi zofuna za achinyamata. Akulu ndi achinyamata si adani; onsewo ali m’gulu

limodzi. Mphamvu zawo ndi zofanana.

A. Uwu ndi mutu wobvuta ndi wotenga mtima. Komabe ndikhulupirira ndiri nawo ufulu woti ndinene

ndithu pankhani imeneyi popeza nanenso ndi kuyandikira nthawi yoti ndipume, ndakhala woyang’anira

kwa nthawi yaitali ndipo ndaukonda mpingo. Ndakhala ndi kupemphera kuti ndilandire nzeru

yolankhula mosasonkhezera moto woyambitsa makangano koma kuti ndithandize ife atsogoleri

achikulire kuti tidziunike tokha ndi kukonza malingaliro athu ndipo potero tilandire udindo wathu

wauzimu wa kuti tithe kusintha mwa chisomo, ntchito ya Mulungu pakati pa mibadwo ndi misinkhu

yosiyana.

B. Umenewu ndi udindo wathu chifukwa 1) Ndife okhwima, olimba omwe tiyenera kunyamula zofooka

za ochepa mphamvu; ndipo 2) Ndife omwe tikutsogolera ndipo tiri ndi mwayi wosankha momwe

ntchito ipitire patsogolo.

C M’mipingo ina atsogoleri akupatsirana bwino nsakali ya utsogoleriyi ndipo anthu aakulu ndi

Page 27: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 27

achinyamata akugwirira ntchito pamodzi. Koma m’mipingoyo yambiri zafika posukusa ngati

sikuonongeka kumene. Pamene kugawikana pakati pa akulu ndi achinyamata ndinso kulimbana

kubuka, achinyamata a amakambirana ndi achinyamata anzawo za achikulire ndipo achikulire nawonso

amakambirana ndi achikulire anzawo za achinyamata, ndipo palibe gulu lomwe limayankhula gulu

linzakelo. Nthawi zambiri amayankhana monga athupi amachitira, molimbana, mopanda moyo

wololerana wa chikondi monga momwe Akhristu otsogoleredwa ndi Mzimu amachitira.

Ndi kumbukira nthawi ina yomwe ndinali kukambirana ndi atsogoleri achikulire ku tauni ina yake,

pamene ndinali kuwalimbikitsa kuti asamafulumize kukhulupirira miseche yopanda umboni yonena

ogwira ntchito mu mpingo achinyamata, koma alumikizane nawo modekha poopa kuti mwina

achinyamatawo angayambe kusafuna kukhala pafupi ndi iwo. Ngati ife achikulire tipitiriza kukakamira

udindo, ngati tikaniza achinyamata mwayi woti athandize kutsogolera mpingo, ndiye kuti tidzathawitsa

achinyamata abwino pamodzi ndi nzeru zawo zomwe zikanadzathandiza mpingo mtsogolo.

3. Nchifukwa chiyani zimakubvutani kusiyira nsakali ya utsogoleri kuti muthandizane kutsogolera?

Choipitsitsa kwambiri ndi choti mwina kumangokhala kulimbanira ndi kukanirira udindo, zosasiyana ndi

zomwe Sauli kapena Herodi anaganiza zija. Tonsefe tili nako kufooka koganiza monga mwa thupi. Ngati

tizindikira moyo umenewu mwatokha, nkoyenera ndi kofunikira kwambiri kulapa, kudzichepetsa,

kufewetsa mitima yathu ndi kusintha mthandizidwa ndi Mulungu! Komabe nditha kuganiza kuti ambiri a

atsogoleri athu amakhala ndi cholinga kapena zolinga zabwino zowapangitsa kuti asachite zinthu

mofulumiza. Zina za zolingazo ndi izi:

A. Kukayikira kutuma ena. Mbali ina yakhalidwe limeneli ndi kudzitamandira (“ndine ndekha wodziwa

bwino”), komanso mbali ina ndi maganizo ongofuna kuti ntchitoyo igwiridwe bwino. Tiyenera

kudziwa kuti atsogoleri achinyamata sadzakhwima ndi kulimba ngati sapatsidwa mwayi weniweni woti

aphunzire kutsogolera. Tiyenera kuwapatsa mwayi woti okha aone chochita molakwitsa monganso

tinkachitira ife munthawi zathu zoyamba zija. Nthawi zina tidzadzidzimuka Poona mphatso ndi nzeru

zomwe sitimayembekezera kuti ali nazo.

B. Kukhudzidwa ndi tsogolo la mpingo. Kwa ambiri a ife atsogoleri ampingo achikulire, mpingo wakhala

monga moyo wathu. Tidzalolera kutaya moyo wathu chifukwa cha mpingo. Achinyamata amaonetsa

zikhulupiriro zina zomwe sitikondwera nazo. Timaiwala kuti nafenso pamene tinali kukula kumene

mumpingo tinkachita zomwezo, ndipo zinkatero ndi mibadwo yonse yakumbuyoku.

Masiku ano kusintha kukuchitika mowirikiza. Koma m’badwo uliwonse unaziganizira wokha

mamvedwe ake a zomwe Baibulo liphunzitsa. Timayesetsa kuphunzitsa ana athu kuti adziopa ndi

kulemekeza Mulungu kuti akonze okha chikhulupiriro chawo. Timakhumbira atakwera m’mapewa athu ndikudziwa zambiri koposa ife eni, koma taonani akateronso timayambanso kuganiza zina ndi

kusowa nawo mtendere. Kodi nanga, ngati Mulungu munjira zina, athandiza ana athuwa kutulukira

nzeru zina zomwe ife sitinadziwa? Kodi nanga monga Paulo wa ku Tariso titsutsa, ndi kusowetsa

mtendere pa ntchito yomwe Mulungu waikonza? Kodi nthawi zina timaponya mivi kwa anthu omwe

Mulungu wawasankha?

Kukhudzidwa kwathu pa nkhani ya mpingo kumakhala kolimba ngati tidzipereka ndi kukumbukira kuti

tiri nacho choonadi chonse ndipo maganizo ena onse abwera pamwamba pa chimenechi ndi monga

nkhamba nkamwa chabe (zakumva). Titha kumalepherabe kumvetsa kwenikweni za zomwe Baibulo

liphunzitsa za chisomo ndi zomwe Mulungu atilamulira pa kulemekezana ngakhale pamakhala

kusiyana maganizo “pa mfundo zina zazing’ono.” (Aroma 14,15). Nthawi zambiri takhala tikubvutika

polimbana ndi nkhani zazing’ono zoti titha kungozisiya, zomwe sitiyenera kuzitenga monga

zoyambirira kuganiziridwa, ngati ndi zofunikira kwambiri pa chikhulupiriro chathu. Inde ndiyenera

kumvera chikumbumtima changa, koma lemba liti ndidzatha kupulumutsidwa ngakhale ndalakwitsa pa

mfundo zina zomwe zagawanitsa okhulupirira. “Mubvomerezane wina ndi mnzake, inde, monganso

Yesu anakulandirani inu….” Izi zingapangitse kuti kukhale kosabvuta kukhalirana pamodzi ndi

achinyamata omwe ayenera kupatsidwa udindo wotsogolera. Komanso sitiyenera kumangololera

maganizo awo alionse; kuwamvera kwathu sikutanthauza kukhuthula maganizo athu onse ayi; pali zina

zoti tidzimusiyira Mulungu.

Page 28: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 28

C. Kusokoneza pakati pa tanthauzo lenileni la mpingo logwirizana ndi Baibulo, ndi momwe titanthauzira

mpingo mogwirizana ndi chikhalidwe chathu cha makolo. Pamene Mulungu wamanga zinthu zina kuti

tisazisinthe, palinso njira zina zambiri zomwe watipatsa mwayi wosankha njira yotikondweretsa

malingana ndi nthawi ndi zinthu zotizungulira. Dongosolo la zambiri zomwe mpingo umachita lagona

m'gawo limeneli. Pankhani ya ufulu wosankhawu, m’badwo uliwonse umasintha mpingowo kuti uthe

kugwirizana ndi kuchita bwino mogwirizana ndi zofunikira za nyengo. Ife omwe takula tiyenera kubvomera kuti momwe chikhalidwe chathu chigwirizanira ndi kumvera tanthauzo la mpingo

chidzatha monganso momwe zakhala zikuchitira ndi mibadwo mibadwo yapitayo. Koma kufunikira

kwa mpingo monga mwa malembo kudzapitirirabe ndipo kudzalimbalimbane; zipata za akufa

sizidzaulaka. Ine ndatengeka ndi kusanalatsidwa ndi chikhulupiriro chopambana ndi kudzipereka

komwe kuli mwa m’badwo wa achinyamata.

4. Kodi tingasiyirane bwanji nsakaliyi mwa chimwemwe ndi kuchepetsa kulimbana pakati pa achinyamata

ndi achikulire?

A. Titha kumaonjezera atosogoleri ena atsopano mumpingo. Atsogoleri anzeru sadikira mpakana zinthu

zifike pofuna kuonongeka chifukwa cha mabvuto autsogoleri. M’malo mwake amalimbikitsa nthawi

isanafike, kugwirira ntchito pamodzi ndi achinyamata nthawi zambiri. Choncho kukonzekeratu

utsogoleri mwa choonadi kumaimirira mpingo wonse ndiponso maganizo a achinyamata amakhala ndi

gawo pa zamtsogolo la mpingo.

Podziwa kuti atsogoleri sakhwima tsiku limodzi, choncho pamafunika kukhala ndi cholinga chofetsa

mbewu ya atsogoleri amtsogolo ndi akazi awo nthawi isanafike. Ichinso chitanthauza kuti gawo la

utsogoleri lomwe liperekedwe kwa achinyamatawo liyenera kukhala leni-leni. Ngati mtsogoleri kapena

atsogoleri akale angodziikirabe okha mphamvu zina, atsogoleri atsopanowo sachedwa kutulukira

bvutoli. (choona ndi chakuti, gulu la atsogoleri lakhala ndi mibadwo yosiyana-siyana, ndi nthawi

zochepa mwinanso osachitika kumene kuti pakhale kugawanikana pakati pa misinkhu yosiyana.)

B. Ife omwe tiri achikulire pa zaka tiyenera kumamvera mwa ulemu maganizo a achinyamata ndi

kumaganizira maganizo awo ngakhale tikulekana ndi maganizo awo. Tinayenera, ndi nthawi yaitali

yomwe takhala padzikoyi, kukhala titadziwa momwe tingachitire modekha ndi moganizira bwino.

Koma ngati nthawi zomwe timangowaikira maganizo athu ndi kumangowakhumudwitsa,

timangowatalikitsa nafe ndipo m’badwo wawo kukhalanso pafupi nafe. Ndipo ngati achinyamata

amveredwa popanda kubvutikira, ndiye kuti kukhala kosabvuta kuti amvere nzeru za achikulire.

C. Titha kumabweretsa pang’ono pang’ono kusintha kwa muyezo woyenera mwa pafupipafupi. Apatu ndi

kutanthauza kusintha kwake kobvomerezeka, kofunikira, kusintha kukhala molingana ndi chikonzero cha Mulungu komwe mpingo wakhala akuchita kuyambira mibadwo yoyambayo mpaka tsopano ndi

cholinga choti mpingo ukhale wolimba ndi kutha kufikira otayikawo. Ngati sitikonza dongosolo

lomasintha mpingo pang’onopang’ono munjira yoti mpingo uthe kumvetsa, timafika pa ndime yobvuta

yoti achinyamata amafuna kusintha kochuluka kwa nthawi yomweyo ndipo mwa msanga koposa

momwe achikulire angathe kukonza. Nkhondo za pakati pa mibadwo zimauka, Akhristu amachoka

ndipo timaononga mphamvu ya mpingo yoti ukanachita kanthu. Atsogoleri anzeru amakonzeratu

zamtsogolo, osati ongochita modzidzimukira.

D. Ife atsogoleri aakulu misinkhu titha kulimbikitsa mizimu yathu ndi maganizo athu ndi mapemphero

pamodzi ndi maphunziro nthawi zonse. Kulimbana kungathe kuyamba nthawi iriyonse pamene anthu

achinyamata aposa achikulire pakamvetsedwe ka malemba ndi ubale kwa Mulungu. Ngati ena a

atsogoleri achinyamata ali ndi mfundo zoopseza, ambiri a iwo amakhala ndi mtima wolimbika zedi za

Mulungu ndi mawu ake. Ife atsogoleri akale nthawi zambiri timangotsamira pa “mfundo zochepa”

zomwe tinaphunzira kale m’masiku oyambirira aja, ndipo timangoona ngati basi, potero takwana,

palibenso china chomwe tikusowanso monga atsogoleri achikhulupiriro ndi okhulupirika. Ziphunzitso

zoyambirira, inde, ngakhale ndi zofunikira, si zilowa m’malo otifikitsa ku moyo wokhwima mwa Yesu.

Nthawi zina abusa amaonetsa kulephera ndi kusadziwa malemba. Ndipo mfundo za dzanja, ngakhale

zikhale zabwino chotani, si zokhazo zomwe ife atsogoleri tiyenera kudziwa. Kuti tithe kulemekeza

misinkhu yonse mumpingo, tiyenera kumvera lamulo la Yesu ndi mtumwi Paulo loti “tiyenera

Page 29: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 29

kumvetsa za nthawi yomwe tiri.” Kodi ndiye kuti ndifedi atsogoleri oona ngati tikulephera monga

atsogoleri, kuphunzira ndi kupempherera zobvuta za makono zisanafike poopseza nkhosa zathu.

Ine monga munthu ndimakhuzidwa ndi momwe zakale zimabvutira atsogoleri achinyamata. Komatu zomwe

tibvutika nazo lero ndi zomwe tikubvutika nazo kale. Ngati ena akubvutika ndi zochitika zimenezi, ife akale

ndi omwe timathandiza kukhazikitsa zimenezi. Zomwe tiwasiyira achinyamata sikuti ndi zoipa kwenikweni. Ayenera kumakumbukira kuti tidawaphunzitsa kukonda Mulungu ndi mawu ake. Koma pamene tikuwasiyira

nsakali imeneyi, tikhale ndi chidwi chotani choonetsetsa kuti tipewe zomwe zimapangitsa kuti achinyamata ndi

ongophunzira kumene apunthwe! Tikhale osamala bwanji kuti tipewe mafano akale omwe ankathawitsa

achinyamata: kukhulupirira zinthu zosachitika, magawano osafunika ndi osatsatira malemba, kulimbikira pa

zinthu zazing’ono, kusokoneza pakati pa maganizo athu ndi malemba, kuchititsa kuti ziphunzitso ndi

zikhulupiriro zikhale amphamvu ndi zofunika kuposa Mulungu mwini.

Chitsanzo chopambana ndi chamtengo wapatali chochokera m’Baibulo cha kusiyirana muuni kwabwino ndi

cha Yohane Mbatizi. Pamene khamu linayamba kusintha ndikuyamba kutsata Yesu, Yohane anakondwera ndi

zimene Mulungu anali kuchita ndipo anati, “Munthu amalandira zokhazo zomwe iye walandira kuchokera kwa

Mulungu … Iye ayenera akule; ine ndikhale wamng’ono.”

Ndinamva ulaliki wina wosasunthika, wochirimika, wodzipereka ndi chikhulupiriro chonse, akulankhula pa

maphunziro zaka zapitazo. Moyo wake ndi chitsanzo chomwe Mulungu amafuna kuchokera kwa atsogoleri

aakulu ndi akale. Kwa ogwira ntchito achinyamata ananena mawu otere: “Ifetu tsopano kuno nkukula. Tiyenera

kuyang’ana kwa inu kuti mupitirize ntchito. Tilandireni udindowu. Tumikirani Mulungu mokhulupirika.

Maganizo anu ena atha kutibvuta ife omwe tiri akale. Komabe musaope kuchita zomwe mukukhulupirira kuti

Mulungu ndiye afuna kuti inu muchite kuti mubale zipatso. Iye adzakhala nanu monganso wakhala ndi ife.”

1. Kulandirira Muuniwo

Ngati nsakali ya utsogoleri ikapatsidwe kapena kusiyiridwa kuchokera ku mibadwo umodzi kupita ku

m’badwo winawo payenera pakhale wolandira wofunadi ndinso wopereka wofunadi. Zimadabwitsa kuti

m’mipingo mwina mulibe anthu ofunadi kulandira katundu wodzipereka wa utsogleri. Kodi zinthu ziri

chonchi chifukwa chiyani? Ndi chifukwa choti makolol asiya kuphunzitsa ana awo kulakalaka utsogoleri

wa Chikhristu kapena kuiona ntchito imeneyi ngati ganizo losiririka labwino? Kapena ndi chifukwa choti

sitiphunzitsa ndi kusula atsogoleri ndi cholinga cha mawa? Kapena ndi chifukwa choti anthu athu

atanganidwa ndi ntchito zawo zina zapadera? Kapena ndi chifukwa cha zobvuta zosiyanasiyana zomwe

asogoleri amakumana nazo masiku ano? Kapena ndi chifukwa choti timasasulira zoyeneretsa za

m’malemba munjira yomwe Mzimu Woyera sabvomereza?

A. Yambani kukonzekera tsopano lomwe. Mtsogoleri amakula pang’ono pang’ono monga mtengo

wamlambe kuchokera m'chiyambi chaching’ono kwambiri: Makolo omwe moyo wawo wonse

umadalira Mulungu ndi kumagawana malemba, mapemphero ndi utumiki pamodzi ndi ana awo

kuchokera adakali ang’ono. Makolo omwe nthawi zonse sangokhalira kutsutsa alaliki ndi abusa koma

amaonetsa kuthokoza pa ntchito zawo ndi kupangita ana awo kuti aganize kuti kukhala mlaliki kapena

mbusa ndi chinthu cha ulemu. Atsogoleri omwe analimbikitsa achinyamata kuti akule ndi kuphunzira.

Makolo achinyamata omwe amaphunzira ndi cholinga choti akule mwayiwo okha. Sukulu za Baibulo

zingakonze maphunziro a masiku ochepa a atsogoleri ozungulira dziko lino ndinso ena omwe afuna

kudzakhala atsogoleri. Abusa angathenso kutumiza achinyamata omwe akuonetsa kuti ali ndi tsogolo

labwino ku uzimu kumaphunziro “a maluso ena.” Ndi kuwalola kuti aphunzirebe pomakhala nawo pa

misonkhano ya abusa ndi kumatsagana ndi abusawo ku ntchito zoyendera nkhosa. Oyang’anira wa

angathe kutuma ophunzirawa ntchito zina.

B. Utsogoleritu siwa wina aliyense. Munthu yemwe akhumbira utsogoleri ayenera kuzindikira ndi

kudziwiratu za kudzipereka nsembe ndi udindo womwe umayenerana ndi utsogoleri. Pamene munthu

wina anafuna kutsata Yesu, Yesu anamchenjeza kuti, “nkhandwe ziri napo pogona pawo ndiponso

mbalame ziri nazo zisa zawo, koma mwana wa munthu alibe poikapo mutu wake.” Woyang’anira

yemwe amayang’aniradi adzasiya nthawi yochita zinthu zake yambiri kuti akonze dongosolo la ntchito

ya Mulungu ndi kutumikira anthu pa zosowa zawo. Adzasamala pochepetsa ufulu wake kuti

asapunthwitse ofooka. Yakobo akutichenjeza, “Musafune kukhala aphunzitsi ambiri a inu, abale anga,

Page 30: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 30

chifukwa mudziwa kuti ife amene tiphunzitsa tidzaweruzidwa moposa enawo.” Atsogoleri ndiwo ali

ndi udindo ndipo ndiwo adzayankhe kwa Mulungu pa nkhosa zomwe iwo ayang’anira. – Ahebri 13:17.

C. Koma Mulungu ndiye amayang’anira iwo omwe alakalaka komanso ali ndi mphatso zamtsogoleri. Iye

amachita izi poyankha mapemphero athu a ogwira ntchito kuti tikolole zipatso. Iye amachita zimenezi

D. pamene anthu payekha payekha apemphera kuti Mulungu awagwiritse ntchito monga mwa mphatso

zawo.

E. Ndi chinthu chofunika kuti okalaka ntchito ya utsogoleri adzichepetse pansi pa ulamuliro wa Mulungu.

Ngati oyang’anira ndi atumiki “oyambira kuphunzitsa” anthu omwe akuoneka kuti ali ndi mphatso,

tiyenera kumvetsa bwino pamenepa kuti dongosolo limeneli silitanthauza kuti amenewa ndiye

angolowa ndi kukhala atsogoleri. Zotsatira zake ziyenera kusiyidwa m’manja mwa Mulungu. Ndipo

ngati mpingo ufunsidwa kutchula maina a atumiki ndi oyang’anira kuti aonjezedwe ku mpingo, iwo

omwe alandira mavoti ochepa, ayenera akukonzekeratu zisanachitike izi kubvomereza zomwe mpingo

wachita popanda kuwawidwa mtima. Mzimu Woyera ndi amene amapanga abusa mumpingo

(Machitidwe 20:28) ndipo imodzi ya njira zomwe amachitira zimenezi ndi yoyankhula kudzera

kusankha komwe mpingo umachita.

Pamene Mulungu aitana anthu ena kuti akhale atsogoleri, izi zimatsimikizika ku mpingo pamene ayesa

moyo ndi khalidwe la iwo omwe aitanidwawo. Ngati wina sanasankhidwe padakali pano, mwina

zingatanthauze kuti Mulungu akufuna nthawi yokwanira yoti amukonze munthuyo. Kapena zitha

kutanthauza kuti Mulungu anampatsa munthuyo mphatso yoti atumikire m’njira zina. Tidziwe kuti

simtumiki aliyense amakhala woyang’anira wa mawa. Inde tikudziwa kuti ntchito zonse ziwirizi

zimakhudzana ndi nzeru za utsogoleri ndi moyo wa chitsanzo, udindo wa woyang’anira ndi wa paokha.

Pali atumiki ena abwino omwe sangathe kutumikira bwino ngati akhala oyang’anira, ndiponso pali

abusa ena omwe sakanakhoza kukhala atumiki abwino.

Popeza zimatenga nthawi yaitali kuti pakhale mtumiki, mlaliki, mphunzitsi ngakhale mbusa, tiyenera

tidzikonzekera ndi kuchitiratu dongosolo lero lomwe lino ngati tikufuna kuti tikhale ndi atsogoleri okwanira ku

mibadwo yakutsogoloyo.

Gawo Lachinayi: Momwe Tingachitire ndi Kasinthidwe ka Zinthu.

Mawu oyamba: Nkhani ya kusintha kwa zinthu ndi nkhani imodzi yobvuta kwambiri mumpingo ndi ntchito

zake, chifukwa kusintha, kaya kwabwino ndi kololedwa komanso kofunika, ndi kobvuta malingana ndi

chizolowezi ndi chilengedwe cha munthu. Chikhalidwe chathu ndi miyambo yathu ikusintha mofulumira

kwambiri moti sizinachitikenso m’mbiri yadziko ndipo zimenezi zikubweretsa mabvuto mumpingo. Mipingo

yambiri konsekonse ikusauka ndi makangano. Anthu ena mumpingo amafuna ufulu wosintha kuti mpingo uthe

kugwirizana ndi kufikira m’maganizo a anthu amakono. Ena amaopa kutaya mpingo ndi choonadi cha

m’Baibulo chifukwa chakusintha kumeneku, ndipo amalimbalimba ndi kukana kusinthika. Alipo ambiri

okhulupirika omwe ndi okonda Mulungu ndi mawu ake ku mbali zonse zakulimbana kumeneku. Komanso

kumakhalanso ena odzikonda, akhungu ndi aukali ku mbali zonse zakukanganako. Tiyeni tiyese kuona

modekha pa cholinga cha nkhani ya kusintha zinthu mumpingo.

1. Kusintha ndi nkhani yamphamvu: ndi nkhani yoopseza ndi yosowetsa mtendere.

2. Kusintha kungathe kukhala kwabwino kapena koipa.

A. Kusintha kungathe kukhala koononga ngati kuli kusintha kochoka pa zabwino kupita pa zachabe,

kapena kusintha ndi zolinga zofuna kudzikondweretsa, kapena kungosintha pofuna kutsatira nkhosa.

Ngakhalenso kusintha kwabwino kumaononga nthawi zonse ngati mpingo ungokakamizidwa popanda

kupatsidwa nthawi yoti umvetse bwino.

B. Komanso kusintha ndi kofunika kwambiri. Ndi mbali ya moyo wathu. Popanda kusintha palibe yemwe

angathe kukula ku uzimu kapena kuthupi. Palibe munthu kapena gulu lomwe lingachize bwino kapena

kuthandiza kwambiri. Palibe yemwe akanatha ngakhale kulapa kumene kapena kufika pafupi ndi

Page 31: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 31

Mulungu ndi cholinga chake. Ndipo mpingo sungathe kufikira anthu a makono osinthika ngati susintha

njira zake zofikira anthuwo.

C. Ziripo mfundo zina zoona zenizeni za mpingo zomwe siziyenera kusinthidwa; ndi zomwe zimachititsa

mpingo kuti ukhale monga momwe ulirimo. Ziripo ziphunzitso zina zofunikira kwambiri, zobweretsa

umodzi zomwe sizisowanso kukambirana kwa mtundu uliwonse – Aefeso 4:4-6; 1 Akorinto 15:1-4. Mpingo nthawi zonse uyenera kukhala woyera, wokhala ndi makhalidwe a Yesu. Nthawi zonse

udzakhala pansi pa ntchito yaikulu yopanga ndi kutuma ophunzira. Udzakhala ndi mangawa

opembedza Mulungu ndi kutumikira anthu osowa.

D. Koma Mulungu wapereka ufulu wambiri ku mpingo kuti usinthike pamene nthawi ziri kusinthanso,

potilola kuti tigwiritse ntchito njira iriyonse, zochitika, ndi mwambo uliwonse. Munthawi zimenezi

mumpingo wakhala ukusintha kuchokera ku m’badwo uwu kupita ku m’badwo wina ndipo kuchokera

ku zaka mazana mazana kufikira zaka mazana ena. Titati tibwerere kumpingo woyamba ija, tingathe

kudabwa poona kusiyana maganizo komwe kunali pakati pawo, chimodzimodzinso ndi iwowo

angadabwe Poona kusiyana maganizo kwa pakati pathu lero.

E. Choncho mu zinthu zina kusintha kungaononge cholinga cha Mulungu. Mu zinthu zinanso Mulungu

amayembekezera kuti zisinthike kuti ziyende bwino, choncho kusasintha kungaononge cholinga ndi

chifuniro cha Mulungu.

3. Miyambo ya makolo ingathe kukhala yabwino kapena yoipa.

A. Miyambo yagawika pawiri:

1) Matanthauzidwe ndi magwiritsidwe ntchito a malemba omwe mibadwo yopitayo inasiira anthu

kuchokera kwa atsogoleri olemekezeka, ndinso

2) Miyambo ndi “njira zabwino” zochitira zinthu zomwe tinasiyiridwa ndi makolonso.

B. Miyambo ndi ya umunthu, osati uzimu. Iribe ulamuliro ndi mphamvu mofanana ndi mawu a Mulungu

ayi. Koma chodabwitsa ndi choti timailemekeza pafupifupi ngati mawu a Mulungu amene, mwinanso

kuipatsa ulamuliro ndi mphamvu ndi kumaisokoneza ndi mawu a Mulungu. Kotero kuti wina akayesera

kusinthako miyambo yanuyo, zimachitika ngati wachita kusintha malamulo a Mulungu.

C. Miyambonso ndi yofunikira mu njira zambiri. Mpingo uliwonse uli nayo. Imathandiza kusunga nzeru

zakale. Imatithandiza kudziwa momwe tingapitirizire mtsogolo ntchito ya Mulungu. Imatipatsa moyo wozindikira mtundu wathu ndi chitetezo. Imapereka dongosolo labwino lakagwiridwe ka ntchito.

D. Miyambo imafika poononga pamene ifika pa ndime yooneka ngati yofunikira kwambiri ndi kumaona

ngati ndi kosayenera kuisintha ndi kuikonza pophunzitsa zomwe Baibulo linena, ndipo ndi kumaganiza

kuti sikwabwino kuisiya pamodzi ndi njira zina zomwe tazolowera ngakhale malinga ndi nthawi

sizikuthandizanso.

E. Ngati miyambo ya anthu iyamba kulepheretsa chiphunzitso cha m’Baibulo kapena utumiki wabwino

ndinso mafikiridwe a anthu ena, iyenera kusiyidwa (ngatitu tifuna kuti tikhale omvera Mulungu ndi

kuika chifuniro chake patsogolo). Tidziwe kuti tidzayankha kwa Mulungu ngati tikonda kwambiri

miyambo ya makolo athu koposa osochera omwe tiyenera kukawafikira. Yesu anamdzudzula atsogoleri

aChiyuda aja chifukwa chonyalanyaza mawu a Mulungu ndi cholinga choti alemekezebe miyambo

yomwe makolo awo anawasiyira – Mateyu 15:1-9.

4. Mfundo zothandiza pa kagwiritsidwe ntchito ka kusintha zinthu kobvomerezeka ndi Mulungu.

A. Mfundo yofunikira kwambiri yomasula nayo kumangiririka ku miyambo ya makolo ndi kuthandiza

Akhristu kuti akule m’chikondi cha pa osochera. Pamene tikukhwima m’Chikhristu, tikuphunzira kuti

kupulumutsa mizimu ndi kofunikira kwambiri koposa mtendere wathu, koposa kudzikondweretsa

tokha. Timaphunzira kuti njira yeniyeni ya Khristu ndi chikondi, kudzipereka ndi cholinga chofuna

Page 32: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 32

kupulumutsa – 1 Akorinto 9:19-23; Aroma 15:1-3; Mateyu 16:24,25. Pamene mpingo ulimbikira

kufikira osochera ndi kupanga ophunzira, pameneponso mpingo udzalimbikira kufuna kusiyiratu

miyambo ndi zizolowezi zomwe zingalepheretse ntchito imeneyi ndi zolinga zimenezi.

B. Pezani nthawi yoti muphunzitse mpingo za kusiyana kwa miyambo ya anthu ndi malemba. Nthawi

zambiri timalimbana chifukwa miyambo imasokonezedwa ndi chiphunzitso cha Mulungu. Upezeni

C. mtima ndi kobvuta kuti anthu amvetse bwino zimenezi.

D. Chitani mosamala ndi modekha monga momwe mungathere. Ine ngakhale ndi kusintha komwe

Mulungu amakondwera nako, anthu ambiri ali ndi muyezo wawo wachilengedwe womwe angathe

panthawi yakuti yakuti. Mulungu amaonetsa kudekha mtima akamachita ndi anthu motere:

1) M’malo mosintha zinthu zambiri nthawi imodzi, amayamba pa zofunikira kwambiri.

2) Amabweretsa kusintha m’magawo oyenera. Mwa chitsanzo, kuphunzitsa nyimbo imodzi yokha

yatsopano pa mwambo ndi nyengo yoperekedwayo.

3) Kupitirira kuonjezera atsogoleri ku gulu la atsogoleri ena ndi cholinga, kuchokera kwa

achinyamata kuti utsogoleri wampingo ukhale woimiriridwa ndi mibadwo yonse ndi kutinso

utsogoleri usakhale monga chinthu chakale chongokhazikika.

E. Thandizani mpingo kukhala wozindikira chifukwa chomwe kusinthika kuyenera kukhalapo.

F. Musalole kuti mpingo ukhale womangiririka kumaganizo ofooka kwambiri, mokakamizika malingana

ndi pamalopo. Kumatheka kuti abale 98 apa malopo abvomereza kuti pakhale kusintha kuti anthu

ambiri akafikiridwe koma awiri aona kuti sikwabwino. Monga mwachizolowezi timangosiya chifukwa

cha awiriwa chifukwa malembo ati musakhumudwitse mbale. Tiyenera kukhala ndi mtima wodekha

ndipo mwa mapemphero kuyesetsa kubweretsa umodzi. Koma ponena zoona Paulo zingatanthauze kuti

maganizo ochepa mphamvu ndi ofookawo, akalamulire ntchito za mpingo.

Pa kuphunzitsa za kusiyana kwa maganizo, Paulo ananena molimbika kuti sibwino kwa iwo omwe

akhulupirira pa chinthu china kuti aweruze ena monganso anauzira iwo omwe alibe bvuto ndi chinthu

china kuti asalakwitse enawo. M’mbuyo monsemu sitinaganizire ndi kuzindikira mfundo imeneyi.

Paulo anatiphunzitsa kuti tidzisiya kuweruza kwina kuti kukhale m’manja mwa Mulungu ndi kupitiriza

pamodzi ntchito ya Mulungu. Pa zinthu zina zazing’ono ndi bwino kugonja pa zomwe

zikanakhumudwitsa winayo. Koma pamene tikuona kuti ntchito ya malemba ingaonongeke yomwe ikadakhoza kupulumutsa miyoyo 50, ndipo ife tingoganiza chifukwa cha miyoyo iwiri, kodi pamenepa

ndiye kuti tawakondadi anthu makumi asanu aja moyenera? Posaganizira za kudekha ndi kukonda

komwe atsogoleri ali nako, nthawi imafika pamene utsogoleri umayenera kungochita chimene

akudziwa kuti ndi chomwe ntchito ya Mulungu ifuna.

G. Sizimachitika kawirikawiri kubweretsa kusintha kwa padera mumpingo wakale, wokhulupirira

miyambo. Kuti zitero ndiye kuti mwina pafupifupi mpingowo ungagawike kapena ena ambiri

adzachoka. Ndi bwino kukonza dongosolo mpingo watsopano womwe udzalemekeza zolinga za

uthenga koposa miyambo ya makolo koma mwa mtendere.

Mawu otsiriza: Kusintha zinthu mofunikira ndi chinthu chobvuta, koma tingathe kupirira ndipo kenako

kukwanitsa kusinthako ngati atsogoleri ndi Akhristu onse ali odzazidwa ndi moyo wa Khristu.

Gawo Lachisanu: Kuchita Mwanzeru Pamene Talekana Maganizo.

Mawu oyamba: Werengani 1 Akorinto 3:1-17. Ngakhalenso mipingo yolimba iri nazo “zowawa zake

zanthawi zonse.” Nthawi zimene tikumana ndi zolimbana ingakhale monga mwayi wotithandiza kuti tikule

mwa uzimu chifukwa timakakamizika kuphunzira ndi kuzidziwa tokha. Kulekana maganizo mumpingo

kungatithandize kuona zambiri; kumva chinthu mosiyana kumathandiza kukonza, kufananiza, kapena

kuonjezerana nzeru wina ndi mnzake.

Page 33: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 33

1. Kodi zina za zoyambitsa akulimbana ndi kukokana mumpingo wathu ndi ziti?

A. Zochitika “zachilendo” kapena “zatsopano” zimayamba kugwiritsidwa ntchito mumpingo ndi iwo

amene amafuna zomwe iwo amati kusintha zinthu mwa phindu. Zinthu zatsopano zimenezi zisakhale

zosiyana ndi malemba ndi cholinga choyambitsa kutsutsana. Monganso momwe zinthu zosiyana ndi

zomwe tinazolowera kuchita, zoyambitsidwa mochuluka ndi mwa msangamsanga, zingachitire.

B. Kusintha kwa utsogoleri ku guwa nthawi zonse kumayambitsa maganizo abwino ndi oyipa.

C. Takhala tikusiyira “nsakali ya utsogoleri” kwa achinyamata, pophunzira kugawana nawo utsogoleri.

1) M’badwo uliwonse uyenera kuchita zimenezi.

2) Iwo omwe ali achichepere adzaona zina za zinthu mosiyana ndi momwe m’badwo winawo

umaonera, monganso momwe ife akalefe tinali nawo maganizo athu pamene tinali achichepere.

3) Ngati akalefe sitinapitirire kuphunzira kuti tikule mwa uzimu ndi m’maganizo anzeru, ndiye kuti

kulekana pakumvetsa kwathu kudzakhala kwakukulu ndiponso kulimbana ndi kutsutsana

kudzakhala ku kukulirabe.

4) Talera ndi kuphunzitsa achinyamata athu kuchita zinthu zoposa kungolimbana ndi zoganizira

zina ndi zina. Tawaphunzitsa iwo kufuna zakuya zauzimu mwa kutsata zolemba. Nthawi zina

sizimakhala bwino pamene achita. Komabe timafuna kuti ana athu aimebe pa mapewa athu ndi

kukula kulabe mu choonadi koposa ife.

D. Mipingo ya Khristu yonse pamodzi yafika munthawi zomwe sitikuzindikira kuti kodi ndife yani? Kodi

tiri nacho choonadi chonse, kapena ziripobe zinthu zina zoti tiphunzire?

E. Pamalo pomwepo mumpingo pangathe kupezeka anthu amitundu yonse iwiri omwe atsamira pa

miyambo ya makolo ndi osasunthika, ndi enanso omwe ndi omasuka ndi okonzekera kusintha nthawi

zonse ndi cholinga chofuna kuti zinthu zikhale bwino.

[ ZOFUNIKA KUONA: Mu mphunziroli, pamene tikunena za “kusintha” tikunena za miyambo ya

makolo ndi zina zachilendo zomwe Mulungu watipatsa mpata woti tokha tichitepo chisankho. Komatu

tiribe ufulu wosintha chirichonse chomwe Mulungu wachikhazikitsa m’malemba.]

1) Anthu amaganizo onsewa nthawi zina amaononga. Anthu amaganizo osasunthika aja amati, “uwutu ndiye simpingo. Anthuwa akuusintha. Ukutayika.” Nawo omasuka posintha zinthu aja

amati, “ziripobe zambiri zoti tichite kuti mpingo ufikepo penipeni pa mpingo wa malemba.

Bwanji nanga tipitirirebe mtsogolo?”

2) Anthu amaganizo onsewa ndi okhulupirika ndipo amamkonda Mulungu.

3) Titha kumangwiriza maganizo ndi zomwe malemba atiphunzitsa komabe ndi kumasiyanabe pa

zinthu zina zazing’ono zoti tiri nawo ufulu wosankha pa kachitidwe kake.

Taonani zitsanzo za momwe mipingo imasiyanirana mu machitidwe ake:

a. Amaona maimbidwe ndi Amaona maimbidwe ndi machitidwe

machitidwe a nyimbo monga a nyimbo monga kupereka

chinthu chongopangidwa chopereka chamtengo wapatali

kapena kuonetsedwa” kwa Mulungu.

Amakondwera kuti anthu Ntethemya za kaimbidwe zimaonetsanso

Kudzipereka kwa mitima mtima wa munthu. Nyimbo monga ulaliki

Yathu, osati za ukatswiri zimamangirira. Nyimbo zoyimbidwa

womwe timauika m’mayi- mwa uthetemya ziri chimodzimodzi ndi

Page 34: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 34

mbidwe athu.” Ulaliki wokonzedwa bwino.

b. Amakondwera kuti anthu Amakondwera kuti okhawo

ambiri agwire ntchito akukhosi kwabwino atsogolere

yotsogolera nyimbo nyimbo lamulungu lija.

lamulungu lija. ”Mulungu sayang’ana zakuja, “Timaika alaliki odziwa ntchito

kaya sikome chotani, guwa la Mulungu lija, chonchonso

m'mayimbidwe athu. Kutsogolera nyimbo, monga gawo

lina la kupembedza, sizinasiyane.

c. Kuomba m’manja sikuloledwa kuomba m’manja ndi kofunikira

ndipo sikuli kofunikira ndipo kumaloledwa m’nthawi

m’nthawi zopembedza. Zopembedza.

”Kuomba m’manja kusonyeza Kuomba m’manja kwa sinthika

Kugonjetsera kapena kuyambira matanthauzo lake pa chikhalidwe

kuti ena aone, koma tiri ku chathu chamakono. Ku kusonyeza

mpingo kuti tipembedze Mulungu kukondwa kapena kuthokoza

osati kuti tionetse anthu monga momwe zinalili m’Chipangano

kapena tiimbire anthu” chakale panthawi yopembedza

(nthawi imeneyo Mulungu analamulira

kuti anthu aziomba m’manja ndipo iye

sanakuone ngati chinthu chosayenera)

Ndipo ndikoyenera “kupereka ulemu

kwa iye womuyenera” ngati iye

salowerera ndi kulandira ulemu wa

Mulungu mwini.

d. Panthawi za chipembedzo Magulu ena apadera amaloledwa

tiyimbe nyimbo za m'bukhu munthawi zina zapadera.

lodziwika zokha basi. Anthu ena anadalitsidwa ndi

Nyimbo zapadera “zimakhala mphatso yokopa ndi kulimbikitsa

monga zoyimbiridwa ena. M’mayimbidwe monga momwe

Tonse tikulamulidwa kuti alaliki achitira pa guwa. Nyimbo

tiziyimba pamodzi. imakhala yoimbira wina (Aefeso 5:19; Akolose 3:16) pokhapokhapo ngati maganizo ake

ali oterowo. Mumpingo woyamba

“aliyense anali ndi nyimbo

mawu ……” (1 Akorinto 14:26).

Zikuoneka nati iyeyu ankaimbira

ku mpingo monga anali nawo”

e. Amaona kuwerenga malembo Amaona kuwerenga malembo

pa gulu lonse monga chinthu pamodzi pagulu lonse monga

chosavomerezeka, zochitidwa chimodzi mmodzi ndi kuimba

ndi mipatuko. Nyimbo pamodzi mofanana ndi

kusangalala komwe mpingo

woyamba uja unkaimbira.

f. Amaona ngati kukweza Amaona ngati kukweza manja

manja m'mwamba ndi njira m’mwamba ndi kusefukira kwa

imodzi yoyamba kuchita kuyamikira ndi kukweza Mulungu,

ngati anthu opembedza maganizo m’Chipangano Chats-

mofuula ampatuko. pano (1 Timoteo 2:8).

g. “Amakonda nyimbo zauthenga Amakonda nyimbo zoyimbidwa

Page 35: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 35

zakale.” Mwaluso,” zoikiriridwa ukatswiri

pozikonza,” kapena amakonda

“nyimbo zomwe zikuyimbidwa

makono.”

”Nyimbo zosazolowereka “Tiyenera kupereka kwa Mulungu sizikondweretsa anthu ndipo zinthu zabwino zomwe tingathe;

nyimbo zina zimangowadutsa maimbidwe akhale odzala ndi

anthu osamva bwino zomwe chauzimu chopambana momwe

ziri m’menemo.” Tingathere. Nyimbo zikhale

zotha kukulumikizidwa bwino

ku maganizo a anthu amakono.

h. Amafuna mapembezedwe Amafuna ufulu wokwanira kuti

olondolezeka bwino, olongosoka athe kuonetsa chisangalalo ndi

ndi odziwika. kuyanjana.

”Chipembedzo chichitike “Kupembedza kuzichokera mumtima

molongosoka ndi moyenera. - osati zooneka zokha ayi. Kumasuka

sikutanthauza chisokonezo.”

Zonsezi ndi zizolowezi ndi miyambo yoti tikhoza kusankha kuichita kapena kuisiya. Munkhani

zonsezi mbali iri yonse imakhala nacho choonadi chake. Zimenezi ziribe umboni weniweni wa

malemba. Koma anthu amabvutika ndi kukhuzidwa ndi nkhani zimenezi koposa nkhani zomwe

ziri zofunikira kwambiri malinga ndi malemba.

4) Kodi nafenso tiri nako kusiyana maganizo pa zinthu zazing’ono ngati izi mofanana ndi momwe

mpingo woyamba uja unaliri? Ena amasungabe maphwando apadera ndi masiku monga Sabata,

koma ena ayi. Ena ankadya nyama ena ayi – Aroma 14.

2 Kodi timachita bwanji pamene tasiyana maganizo?

A. Osati:

1) Kunyoza omwe ali ndi maganizo osiyana nawo kapena kuwatsutsa ndi zolinga zoipa.

2) Kunenanena za zovuta zathu ndi wina aliyense osakhala omwe tinayenera kunena nawo, motero

timangoonjezera ndi kukulitsa kulimbana kwathu.

3) Kukana kuganizira ndi kubvomereza maganizo ena.

4) Ndale, mphamvu, kulamulira, kunyozetsa, kunenana zoipa ndi okutsutsani, kupatsana maina

achabe (wachilamulo, waufulu, wauzimu, wampatuko)

B. Koma mwa:

1) Kumvetsa mfundo zina:

a. Nthawi zonse padzakhala kusiyana maganizo pa mpingo uliwonse

womwe

ukukula. Padzakhala kulolerana ndi kugwirizana munkhani zina

zazing’ono, apo ayi, mpingo udzagawika ndi kukhala m’magulu. Paulo

amatiphunzitsa kuti tidzikhala ololerana munkhani zina zazing’ono –

Aroma 14,15.

Page 36: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 36

b. Pamene tikukula kusintha kwina kumakhala kofunika. Tiribe ufulu

wosintha zomwe zinamangirika ndi malemba, koma pa nkhani

zakumasuka tiyenera kusintha kuti tithe kufikira bwino ku khalide

losinthikali (ngati tikufuna kutsatira chitsanzo cha Paulo ndi kufikira

mizimu yochuruka – (1 Akorinto 9:19-23). Kusinthika pakokha sikuli

koipa kapena kwabwino.

c. Kusintha nthawi zonse kumatisautsa. “zakale zomwe zija zinali bwino.”

d. Nthawi zina anthu amaukirana wina ndi mnzake chifukwa chosamvetsa

zomwe mpingo ndi mapembedzedwe ake uliri malingana ndi malemba.

e. Kulimbana kwathu m’mipingo nthawi zambri kuli pa momwe timvera

malembo osati pa chiphunzitso chenicheni cha malemba.

f. Kulimbana kotigawa kumayambika ndi “mbali zonse” zokakamiza kuti

zisinthe ndi kulimbana pokana kusintha. Cholakwika chimodzi chachikulu

chomwe tingachite ndi chodzudzula mbali imodzi yokha ya vutoli.

Mu Aroma 14 ndi 15 timaphunzira kuti anthu okhala ku mbali zonse

zankhaniyi ayenera kufewetsa zofuna zawo ndi maganizo awo kuti athe

kusamalirana ndi kukhala amodzi. Uwu ndiwo moyo wa mtanda – Aroma

15:1-3. Mpingotu sungathe kukula ndi kuyendera pamodzi popanda

chimenechi.

2) Pomvetsa ndi kubvomereza kuti tiri ndi umunthu wochimwa ndi wodzitamandira.

a. Nditha kumafuna kudzikondweretsa ndekha koposa kukondweretsa

zofunikira za mpingo.

b. Nditha kukhala wopanda chidwi chosenza zofooka ndi zosowa za ena.

c. Nthawi zina nkhawa zanga za kunyumba kwanga kapena zina zodziwa ine

ndekha kapena kuntchito kwanga ndimazipitiriza ndi kuzilowetsanso

kumpingo.

d. Zolimbana zambiri mumpingo ndi m’mabanja nkhani za “mphamvu” osati

zimene zimaonekerazo.

3) Pochita zinthu zosagwirizana ndi umunthu m’malo mochita za umunthu pamene titsutsana ndi

ena.

a. Umunthu wathu umatikakamiza kusakomanso ndi anthu omwe

sitigwirizana nawo. Choncho anthu olekanawo amangopitirirabe

kulekana.

b. Onetsani kupepesa kwanu chifukwa cha umunthu wanu wa uchimo

pochita zomwe anthu sangaziyembekezere:

1. Khalani ndi nthawi yoyanjana ndi omwe simugwirizana mu zambiri.

2. Yesetsani kuyamikira ndi kumvetsa maganizo a enawo mosakondera ngakhale

simugwirizana nawo.

3. Onetsani zolinga zabwino kwa okutsutsaniwo – 1 Akorinto 13:4-7.

4) Yambani mwaganiza bwino kwambiri musanayankhule kapena kuchita.

Page 37: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 37

a. Tidzayankha mlandu pa mawu onse opanda pake omwe tidzayankhula – Mateyu 12:36-37.

b. Mulungu amadana ndi anthu omwe amafetsa mbewu zodanitsa abale – Miyambo 6:19.

c. Yesu amapempherera kuti tikhale amodzi kuti dziko likhulupirire kuti Mulungu ndi amene

anamtuma – Yohane 17:20-21.

d. Kukanakhala bwino kuti munthu amizidwe m’nyanja yakuya koposa kuchimwitsa mmodzi

wa aang’ono – Luka 17:1,2.

e. Ngati tiononga kachisi wa Ambuye pogawanikana, nayenso adzationonga – 1 Akorinto

3:16,17.

f. Tiyenera kumadziunika tokha koposa enawo – Mateyu 7:1-5. Mwina chifukwa cha

kusadziwa, nditha kutsutsa zomwe Mulungu afuna. Nditha kumalimbikitsa zomwe Mulungu

safuna. Polimbikira kusunga miyambo ndi zizolowezi nditha kumangofuna maonekedwe

osati zenizeni zofunikira. Pofunafuna kusintha kwa zinthu nditha kumangofuna kuti ndione

momwe zikhalira m’malo moti zikhale molingana ndikufuna kwa Mulungu kapena kumvera

kwathu kwa tsiku ndi tsiku. Ngati ndikana kusintha chifukwa cha chiphunzitso chomveka

bwino cha malemba, Iye adzandipatsa mphoto. Ngati ndikana kusintha chifukwa chakufuna

kungokondweretsa maganizo anga ndi zofuna zanga, Mulungu adzandilanga chifukwa

ndalepheretsa ntchito yabwino yobereka zipatso ya mpingo. Nditha kuchita zinthu

kumpingo zomwe sindinachitepo.

4) Pouza zotisautsa zathu kwa wotilakwirayo, ndipo kenako ngati nkofunikira kwa

atsogoleri a mpingo – Mateyu 18:15f.

a. Popereka kwa enawo chilolezo chomwe ifenso tikadakonda atatipatsa.

a. Popita ku tchalitchi ngakhale kuti pali poti dongosolo lomwe

likukonzedwalo sitikondwera nalo patokha.

b Poganizira kuti nditha kuupeza mtima ndi kudzibweza ngakhale wina

atachita china chomwe ine sindichibvomereza monga cholondola.

c Pokhala ndi mtima wodekha mwachikondi kwa omwe sagwirizana ndi

maganizo anga osintha zinthu.

6) Atsogoleri athu pomvetsera mosamala ku maganizo ndi zofunikira zonse mumpingo ndi

kusankha njira yodekha yomwe idzakhoza kukwaniritsa zosowa za mbali zonse monga momwe

kungathekere. Mpingo suyenera kukhala ndi maganizo a anthu a mbali imodzi yokha.

Abusa oyenera azikhala owonetsetsa ndi odziwa zonse zochitika pa mpingo, akonze ndi

kugwiritsa ntchito mfundo yodekha yosinthira miyambo ndi zizolowezi, kulemekeza zonse

zokhazikitsidwa mwa malemba, kuphunzitsa mpingo kuti uonjezere chidziwitso chake, ndi kuika

chitsanzo chabwino cha kulolerana pakati pa atsogoleri okha. Ayenera kumadziwitsiratu mpingo

kusintha kuli konse kusanachitike.

Mawu otsiriza: Palibe chinthu china chomwe mdierekeze angachikonde chopusa kucheptsa ndi kunyoza

ntchito yabwino yomwe ikuchitika m’mipingo. Iye amafuna kuti ife tidziika maganizo athu kwambiri pa zinthu

zazing’ono, ndi kutichotsera moyo wodalira Yesu ngati Ambuye wathu, ndinso kutichotsera moyo wofuna

kukafikira ndi kukachiritsa mizimu. Tiyenera kupereka ulemu wathu wonse kwa Khristu pochita ndi kulekana

maganizo kwathu munjira yoti siting’amba thupi lake, mpingo. Tiyenera kulemekeza atsogoleri athu ampingo

pamene akuyesetsa kutitsogolera mu umodzi. Ndipo tiyenera kupempherera atsogoleri athu pamodzi ndi

mpingo wa Khristu.

Page 38: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 38

Mutu 6: Umodzi ndi Malekano Mumpingo wa Khristu -

Yesu anapempherera omtsatira ake kuti akhale amodzi kuti dziko lapansi likamkhulupirire Iye – Yohane 17:20-

21. Ntchito yopititsa mtsogolo ufumu wa Mulungu yokhala ikusokonezedwa kwambiri ndi kugawanika pakati

pa Akhristu koposa zifukwa zinazo. Ndipo ufumu wa Satana wapindula kwambiri potengera mwayi

kugawanika kumeneku. Ngati tiri ndi mtima wonga wa Khristu, tidzalakalaka umodzi wapakati pathu ndi anthu ena okhulupirira ndipo tidzachita china chirichonse, poyesa yesa kuti pakhale umodzi. M’masiku ano, pamene

mipatuko ikuchepera ndipo pali njala yomwe ikukulira yofuna kubwerera ku zoona zokhazokha, nkhani

yotsatira itithandize kuganizira mozama.

1. Kodi onse okhulupirira Yesu angathe bwanji kukhala amodzi? M'zaka za m’ma 1800 ku Britain ndi ku

America, kunapezeka aphunzitsi ambiri ochokera m’ziphunzitso zosiyanasiyana za mpingo omwe

anasautsidwa m’mitima yawo chifukwa cha malekano ndi kulimbana pakati pa okhulupirira, omwe anafuna

kuyanjanitsa okhulupirira onse pobwerera ku ulamuliro umodzi wa malembo achikhulupiriro ndi zochitika

za mpingo. Padali Abner Jones ndi John Wright a gulu la a Baptist; James O’kelley a gulu la a Methodist;

ndi Barton W. Stone, Walter Scott, Thomas Campbell ndi mwana wake Alexander Campbell a gulu la a

Presbitale. Aliyense wa amenewa payekha payekha anakhumudwa ndi kulimbana ndi kupatukana komwe

kunalipo pakati pa otsatira Khristu chifukwa cha ziphunzitso. Ndipo aliyense anaona kuti njira yabwino

yoyanjanitsira okhulupirirawa inali yekhayo yobwerera ku ulamuliro wa malembo. Thomas Campbell

anayesetsa kugwira ntchito yoyanjanitsa Akhristu a m'gulu la a Presibiteriani omwe anali kulimbana ku

mpingo wa ku Ayalandi (Irelandi).

2. Thomas Campbell, Alexander Campbell ndi Barton W. Stone anali atsogoleri opambana omwe anadziwika

nthawi imeneyo pa ntchito yoyesetsa kubwezeretsa chikhulupiriro cha pa malemba ndi kuchita komwe. A

Thomas Campbell anapita ku America kuchokera ku Scotland. Iye anali pasitala wa mpingo wa a

Presibitare, ndipo kudziko la chilendo iye analandiridwa napatsidwa ulamuliro ku mipingo ina yakomweko

komwe iye ankayendera. Campbell anabvutikanso m’maganizo pamene anapeza kuti ku America nakonso

kunali magawano ndi magulu omwe anawasiya kwawo ku Scotlandi kuja. Omwe anali a gulu limodzi

samalola kuyanjana pamodzi ndi a gulu lina lija ngakhale kuti onse anali a Pulesibitare okhaokha. Ndipo

m'matauni monse munali magulu odzipatsa maina osiyanasiyana namataya nthawi yawo ndi mphamvu

zawo kulimbana wina ndi mnzake, mphamvu zoti anayenera kudzigwirira ntchito yopulumutsira osochera

ngati mipingo ikanakhala yogwirizana.

3. Pamene Campbell anafuna kuyanjana ndi gulu lina lija mwa mgonero, iye anatsutsidwa ndi akulu a

mpingo. Kenako iye anangoganiza zosiya kugwiritsa ntchito dzina loti “Pulesibitare” nayamba

kumangotumikira Mulungu wake monga Mkhristu basi popanda kuonjezeranso dzina lina la padera la chipembedzo. Anayamba kuzindikira kuti maina opangidwa ndi anthu ndi zikhulupiriro zake zomwe,

zimangolimbikitsa zipupa zamalekano pakati pa magulu otsatira Khristu. Iye anatsimikizika kuti ntchito

yake yonse ikangotsamira pa mphamvu za malemba basi, ndipo anayamba kudandaulira ena onse omwe

anali m’mipingo kuti asiye kulimbana pakati pawo chifukwa cha miyambo ndi zikhulupiriro zoikidwa ndi

anthu ndikuti agwirizane pomangoyang’ana pa malembo kuti adziwe komwe akupita ndi choyenera

kuchita. Iye analibe cholinga chofuna kuyambitsa mpingo watsopano. Iye anangofuna kuti mipingo

isinthike posiya miyambo ndi zizolowezi zomwe inadzipangira ndi kudziunjikira ndipo m’malo mwake

agwirizane ndi kuyanjana pansi pa chiphunzitso ndi machitidwe a atumwi.

4. Pamene Thomas anapita ku America, Alexander, mwana wake, anatsala ku Scotland kwa kanthawi

pamodzi ndi mayi wake ndi ana ena onse. Panthawi imeneyi Alexander anali kuphunzira pa univesite ina.

Nayenso, monga bambo wake, anatulukira kuti panali kulekana kwa maganizo mumpingo pa zifukwa

zazing’ono, ndipo kuti anthu a gulu linalo sanali kulola kuyanjana pa mgonero ndi anthu a gulu linali

ngakhale onse anali a Pulesibitare okhaokha. Iye anaonanso kuti makonzedwe ndi dongosolo la zochitika

za mumpingo wa a Pulesibitalewu zinali zosiyana kwambiri ndi zomwe iye anaona m’malemba. Pasanapite

nthawi Alexander pamodzi ndi ena onse a pa banja lawo anapita kukhala pamodzi ndi Thomasi ku Amerika

kuja. Ali ku Amerikako Alexander anayamba kuthandiza bambo ake mu ntchito yodandaulira kuti pakhale

umodzi wosadalira zoikika ndi maganizo a anthu koma zotsamira pa malembo.

5. Thomas Campbell analemba bukhu labwino lofotokoza za umodzi pakati pa Akhristu ndi zoyambitsa

Page 39: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 39

kupatukana. Linatchulidwa “Kunena poyera ndinso kuyankhulira” (Declaration and Address), (onani gawo

lake ku zoonjezera). Thomas ndi Alexander anaona kuti Baibulo linali chimodzimodzi ku mipingo yonse,

koma ziphunzitso ndi zikhulupiriro ndizo zinasiyana. Mipatuko siichokera mu Baibulo limodzi ayi, koma

ichokera ku zikhulupiriro ndi ziphunzitso zolekanazo zomwe ndi zopangidwa ndi munthu. Mpingo

uliwonse unali wokonzekera kumvera unzakewo ngati unzakewo ukanasiya zikhulupiriro zake ndi

ziphunzitso zake ndi kubvomereza za winawo. Koma zonse sizinayenda bwino popeza mpingo uliwonse pawokha unakakamira kugwiritsa zikhulupiriro zake monga zoulamulira.

6. Thomas Campbell anayamba kupempha okhulupirira onse kuti ayambe kusiya zikhulupiriro ndi

ziphunzitso zonse zolembedwa ndi munthu ndi kubwerera ku malemba, omwe ali olandiridwa ndi onse,

monga maziko enieni owalamulira ndinso umodzi. Iyenso anapereka maganizo oti anthu asamachite

chirichonse mumpingo chifukwa choti atsogoleri awo akale ankachita motero, koma kuti tiwerengenso ndi

kuphunzira bwino malemba ndi kuchita chirichonse chomwe tichita chifukwa cha mphamvu ndi ulamuliro

wa malembo.

7. Ndipo pamene anapitirira kuphunzira mawu a Mulungu, Thomas ndi Alexander Campbell, mabanja awo,

ndi ena omwe ankaphunzira nawo pamodzi anabatizidwa mwa ubatizo weniweni womizidwa. Iwo

anazindikira kuti ubatizo wawo wa poyamba wa pamutu sunalingane ndi ubatizo wa mawu a Mulungu,

ndipo kuti ubatizo wa pa mutu unali wonga njira za chidule zopangidwa ndi munthu monga chizolowezi

chabe chomwe chinayamba kuchokera munthawi za atumwi. Anasiyanso kumayang’ana malo ena a dziko

kapena bungwe monga boma kapena likulu la mpingo, chifukwa anaona kuti m’mawu a Mulungu mpingo

uliwonse unali nawo atsogoleri ake osakhalanso pansi pawina aliyense koma pa ulamuliro wa Khristu basi.

Anasiya kudalitsa makanda ndi ana aang’ono chifukwa sanapeze ulamuliro kapena chitsanzo cha

mchitidwe umenewu m’mawu a Mulungu. Anayamba kumayanjana ponyema mgonero wa Ambuye sabata

iriyonse pokumbukira imfa ya Khristu tsiku loyamba la Sabata iriyonse chifukwa anaona ndi kuphunzira

kuti mpingo woyamba unkatero. Anapitiriza kuphunzirabe ndi kutsatirabe zambiri ziphunzitso ndi

machitidwe a mpingo wa Chipangano Chatsopano, ndi kutaya zikhulupiriro ndi ziphunzitso zomwe

anakhulupirira kuti zinangoonjezedwa ndi anthu m mibadwo yobwera nthawi ya atumwi itapita. Patapita

nthawi, Campbell ndi mwana wake anagwirizana ndi Walter Scott ndi Barton W. Stone omwenso nawo

anali kulakalaka ndi ntchito yobweretsa umodzi potsamira pa mawu a Mulungu.

8. Chiwerengero cha anthu omwe anakhulupirira mfundo zimenezi chinachulukira chulukira ndipo mipingo

inabadwa. Zinthu zonga zomwezi zinali kuchitikanso ku Britain. Ntchito yonseyi pamodzi inatchedwa

“Ntchito yobwezeretsa” (Restoration Movement). Komatu atsogoleri antchito imeneyi analibe maganizo

ndi zolinga zofuna kuyambitsa mpingo winanso ayi. Iwo anangofuna kuti magulu onse olekana aja akhale

amodzi monga thupi la Khristu motsamira pa malembo. Komabe ngakhale anthu ambiri anabvomereza

pempho limeneli, anthu ambiri m’mipingo yambiri anakana, ndipo “Osinthitsa zinthu aja” kapena “obwezeretsa zinthu aja” pamodzi ndi owatsatira awo anangopitiriza monga gulu chabe. Choncho konse ku

America ndi ku Britain anthu a m'gulu limeneli ankatchedwa “Akhristu”, ndipo mpingo wa pamalo

unkatchedwa “mpingo wa Khristu,” “mpingo wa Chikhristu,” kapena “Ophunzira a Khristu.” Koma ndi

maina amenewa sanatanthauze kuti iwo okha ndi amene anali anthu ake a Khristu. Sanali kuyeserera

kutenga malo a Mulungu ndi kuweruza zotsatira zake za okhulupirira enawo. Koma anangokhulupirira kuti

ngati mpingo uli wake wa Khristu, uyenera kumlemekeza pobvalanso dzina lake, monganso momwe

mkwatibwi amabvalira dzina la womkwatira wake. Sanafune dzina lomwe silinachokere m’mawu a

Mulungu, ndipo anakhulupirira kuti maina oikidwa ndi anthu osiyanasiyana amangolimbikitsa kusiyana

komwe kulipo pakati pathu.

9. Bungwe limeneli lobwezeretsa silinakwaniritse zomwe limayembekeza ndi zolinga zake monga momwe

zikanakhalira. Panabukanso kugalukirana kwakukulu mzaka za m ma 1900. Pankhani ya nyimbo

zoimbidwa pogwiritsira ntchito zida munthawi yachipembedzo ndi kukhazikitsa bungwe la a mishonare.

Kugawikanaku kunapitirirabe pamene mpingo tsopano unasowa ndi kutaya masomphenya a zolinga zake

zoyamba zija. Ena omwe anali kugulu lopanda ukali mubungwe limeneli anayamba kusalemekeza ndi

kukhulupirira mphamvu ndi ulamuliro wa malemba. Nawo oumirira za miyambo aja anasokonekeranso

kumbali inayo, nayamba timagulu tina tambirimbiri, namadzitcha kuti iwo okhawo ndiwo ali mpingo

weniweni wopulumutsidwa. Zolinga zenizeni zomwe zinatsogolera ntchito imeneyi zinali za kufunika kwa

mphamvu ndi ulamuliro wa malemba ndi kuipa kogawanikana chifukwa chosiyana maganizo ndi

kumvetsana pa nzeru zina ndi zikhulupiriro zina. Mipingo ya Khristu inapitiriza ganizo loyambalo koma

Page 40: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 40

unalephera kumvetsetsa ndi kukumbukira cholinga cha ganizo lachiwiriro. Tinalepherakusiyanitsazinthu

zenizeni zotumikira ndi maganizo chabe. Tinali monga gulu limodzi la palokha, logawika

m'timagulu tambiri mwa magulu a chipembedzo ku America, logawikana m’magulu opitirira 25. Gulu lathu

lotchedwa ‘mipatuko’ ndipo kenako tinawapitirira mu njira yolekanitsa, moyo wa mpatuko.

Monga momwe kusintha ndi kubwezeretsa kumafunikira nthawi zina, komanso kuli nako kuopsa kwake komwe kuli kwa mitundu iwiri: Pa momwe amatengera machitidwe a m’Chipangano Chatsopano, angathe

kunyalanyaza chiphunzitso cha m’Baibulo pazakusinthika mtima kwa mumtima (komwenso umodzi

umatsamira). Ndipo angayambe kukhala ndi moyo woyang’ana ndi kudalira malamulo, kukhulupiriro kuti

Mulungu amatilandira chifukwa cha kusunga malamulo kuposa chifukwa cha chisomo cha ulere cha

pamtanda wa Khristu. Ntchito yosintha ndi kubwezeretsa imeneyi nthawi zambiri yakhala ikugwera m

misampha yonse iwiri. Ngakhale panthawi yomwe ntchitoyi inali pa kaindeinde, sikunatheke kubwezeretsa

chiphunzitso cha m’Chipangano Chatsopano, machitidwe ndi moyo wabwino sizinatheke kufika pomwe

zinali kufunikirapo. Iyi ndi ntchito yoti imangopitirira.

Wolemba ameneyu akukhulupirirabe kuti “mfundo yobwezeretsa” ndi yofunikirabe yoyenera kupitirira,

makamaka kusiya miyambo ndi zizolowezi zopangidwa ndi anthu ndi kupitiriza kuyanjanitsa okhulupirira

onse mwa kutsamira pa mphamvu ndi ulamuliro wa mawu a Mulungu basi. Palibe yemwe angatsutse

mfundo imeneyi. Ngakhale mfundoyi yakhala ikulephera m’magawo ena, ntchito yobwezeretsayi yalalika

ndi kufalitsa uthenga wamtengo wapatali ndi wofunikira kwambiri wonena za kutsamira ndi kudalira pa

mphamvu ndi ulamuliro wa malembo, ndiponso waturutsa atumiki a Mulungu ambiri omwe agwira ntchito

yotamandika kwambiri. Ndipo sionse a atsogoleri a gulu limeneli omwe anakhala ndi mtima wampatuko.

Abambo anga a ine anakana kulowa m’gulu la mpatukolo ndipo zotsatira zake ndi zoti anazunzidwa

kwambiri. M’masiku atsopanowa, magulu ena omwe anachoka mogalukira analapa ndipo analandiridwa

m’chiyanjano chathu.

10. Mpingo uyenera kumayendetsedwa mwa ulamuliro ndi mphamvu za malemba okha m’chikhulupiriro ndi

m’machitidwe wokha basi, chifukwa:

A. Miyambo ndi ziphunzitso zongoonjezeredwa ndi anthu zimagawanitsa Akhristu – Aroma 16:17.

B. Akhristu ayenera kumvera mawu a Khristu Ambuye wawo ndipo ayenera kumachita chifuniro chawo

monga momwe chinaululidwa m’Baibulo. Iwo alibe mphamvu ndi ulamuliro wosintha chimene

chinalamulidwa ndi Ambuye kapena atumwi awo. Onse okonda Khristu ayenera kumalakalaka

kumukondweretsa pomvera ndikudzipereka ku mawu ake – Yohane 14:21,23; Luka 6:46.

C. Mulungu sakondwera ndi mapemp0hero athu pamene tilowetsa miyambo ndi zizolowezi zopangidwa ndi anthu m’malo mwa malamulo a Mulungu – Mateyu 15:3-9.

D. Sitingathe kupeza nzeru za mtundu woposa nzeru za Mzimu Woyera zomwe zifotokozedwa

m’malamulo a atumwi ndi zitsanzo za mumpingo woyamba.

11. Atsogoleri oyamba a gulu la kubwezeretsa aja, anali okhudzidwa kwambiri ndi nkhani ya umodzi pakati pa

Akhristu. Iyi ndi nkhani ya Baibulo. Mu Aefeso 4:4-6 Paulo akutiuza wapereka mndandanda wa

ziphunzitso zisanu ndi ziwiri (7) za zoonadi zake zomwe mipingo yonse pamodzi ndi Akhristu onse

ayenera kugwiritsa ndi kukhala nazo mofanana ngati afuna kukhala ndi “umodzi wa Mzimu Woyera” mwa

Khristu. Iye akutchula thupi limodzi, Mzimu mmodzi, chikhulupiriro chimodzi, Ambuye mmodzi, ubatizo

umodzi, ndi Mulungu mmodzi. Awa ndiwo maziko enieni a chiphunzitso cha umodzi.

Komabe kungomvana ndi kugwirizana pa chiphunzitso chokha sikungayanjanitse Akhristu. Koyambirira

kwa ndime yomweyo ya umodzi, pa Aefeso 4:1-3, Paulo akutiuza za mtima womwe Akhristu ayenera

kukhala nawo kuti asunge ndi kusamalira umodzi pakati pawo. Iye akutchula, kudzichepetsa konse,

chifatso, chipiriro ndi kulolerana mwachikondi. Malingana ndi Pauloyo, umodzi ndi chinthu cha Mzimu,

ndipo zoyeneretsa zomwe zasanjidwa pamenepazi ndizo chipatso cha Mzimu Woyera – Agalatiya 5:22,23.

Kulikonse komwe Paulo anapita, iye amaphunzitsa kuti Akhristu sayenera kuweruzana wina ndi mnzake

kapena kulekana chifukwa cha mfundo zazing’ono, zomwe angathe kukambirana ndi kusankha maganizo

omwe afuna ponena za m’Baibulo ndi ziphunzitso zake, koma ayenera kungosiyira nkhani zimenezi

Page 41: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 41

Mulungu pamene iwo apitiriza kugwira ntchito pamodzi. – Aroma 14:1-15:7. Kugawanikana pa zinthu

zimenezi pakokha ndiko kusamvera malemboko. Baibulo litiphunzita kuti ife timayanjanitsidwa ndi

kukhala amodzi chifukwa choonadi chenicheni cha chilungamo osati chifukwa choti tagwirizana ndi

kufanana maganizo pa mfundo zina zazing’ono. Ndipo kupatukana kwambiri sikumabwera chifukwa

chosamvana pa ziphunzitso koma chifukwa mtima wofuna kudziganizira wekha, ndinso makani chabe –

Agalatiya 5:19-21; Aroma 16:17,18. Nthawi zambiri nkhani za chiphunzitso ndi chikhulupiriro zimaperekako mwayi wa ulemu; zoterezi zikanatha kukonzedwa ngati pakanakhala mtima wabwino ndi

kulakalaka kwenikweni kwa umodzi. Titha kukhalabe okhulupirira ndi kudalira malemba pa chiphunzitso

ndi chikhulupiriro chathu ndi machitidwe athu, koma ndi kulekanabe maganizo ndi kumagawikanabe,

kumapitirirabe kupikisana kufikira mitima yathu itasinthika ndipo umulungu utabadwa mwa ife mwa

Mzimu Woyera ndi mawu. Nthawi zambiri kupatulana chifukwa cha zipembedzo, sichifukwa ayi, koma

kungofuna kulimbana kudzifunira kutchuka, kudziyeretsa pobvala mwinjiro wa chipembedzo. Ngakhale

ntchito yobwezeretsa inachita gawo lalikulu pobwerera ku kudalira ku maziko a chiphunzitso ndi

machitidwe a malemba, sunathe kupitiriza mpaka pa ndime yokonzanso za bvuto la kufunika kwa kusintha

kwenikweni kwa uzimu ndi kusinthika kwenikweni kwa mkati mwa mtima.

Choncho pofuna kukhala ndi umodzi wachipembedzo, chiphunzitso chathu chiyenera kupitirirabe kusinthika

pogwiritsa ntchito malemba, ndipo mitima yathu nayonso isinthike pogwiritsa ntchito Mzimu Woyera. Zonsezi

kuti zitheke pamafunika kudzichepetsa. Munthu wodzitukumula ndi wonyada sangathe kusiya ndi kuiwala

zikhulupiriro ndi zizolowezi zake za umunthu pamodzi ndi moyo wake wozolowera zolimbana ndi zotsutsana.

Ndipo kudzichepetsa kumeneku kumatheka pokhapokha pamene tibadwanso mkatikati mwa mtima wathu mwa

Mzimu Woyera ndi kupatsidwa umoyo watsopano wa Yesu Khristu. Tiyeni tidzipereke kumoyo womvera ndi

kukhulupirira malemba ndi Mzimu Woyera. Pakutero tidzakwaniritsa pemphero la Ambuye Yesu: “[Ine ndi

pemhera] kuti onsewa akakhale amodzi … kuti dziko lapansi likakhulupirire kuti inu munandituma ine” –

Yohane 17:20,21.

Mutu 7: Mpingo wa Khristu ndi Zipembedzo Zina za Chikhristu.

Ngati umodzi uli wofunikira kwambiri mu ntchito yofalitsa uthenga wabwino, ndi koyenerera kuti tionenso

bwino pa za momwe timaganizira magulu omwe analowa nawo mu gulu losintha sintha zija. Nkhani zina za

ziphunzitso zomwe zimatigawanitsa pakati pathu zimakhala zokulirapo. Komanso mwa chiyero, timayenera

kuyamikira ndi kuthokoza pa zinthu zomwe anthu achita bwino, poonjezera pakudzudzula ngati alakwitsa.

Ndiri wokondwa chifukwa ambiri pakati pa abale alibenso mtima wofuna kutenga udindo wa Mulungu

woweruza ena omwe ali mu “zipembedzo zina.” Tingathe kukhala okhulupirika m’malembo popanda kutero.

Ndimasanalatsidwa ndi mawu amphamvu omwe ena a abale m’mipingo ina amanena, “osati Akhristu okhawo,

koma Akhristu okha.” Yesu analangiza ophunzira ake kuti asaletse iwo omwe anali kutumikira m’dzina lake

ngakhale sanali nawo m’gulu limodzi. Paulo anali wokondwera chifukwa Yesu analalikidwa ngakhale ena a

olalikawo sanali ndi zolinga zowona.

1. Mipingo ya Khristu mzaka zatsopanozi, zaposachedwapa inayamba kudziwika mona yokhulupirira kuti ndi

yekhayo yodziwika kuti ndi yopulumutsidwa. Ndiri wokondwa chifukwa tsopano pali kusintha, chifukwa

izi si zomwe abale athu omwe amayamba ntchitoyi anakhulupirira. Abale omwe anayambitsa kuti Mulungu

anali nawo anthu ake omwe anali m'zipembedzo zosiyanasiyana. Anapempha Akhristu onse kuti asiye

ziphunzitso ndi zikhulupiriro ndi kugwirizana mwa kumangiririka pa malemba basi. Bambo wanga

anandiphunzitsa kuti munthu aliyense yemwe wabadwanso kawiri, nalandiridwa ndi Mulungu, ali gawo la

thupi la Khristu ngakhale mipingo yathu isamdziwe kaya imdziwe. Tikanakomana nako kuzunzidwa

mwadzidzidzi, maganizo athu onse akadasinthika tsiku limodzi pa umodzi wathu. Tikanayamikira

kwambiri aliyense yemwe alemekeza Yesu monga Ambuye ndi kuyeserera kumumvera.

2. Gulu lathu lachita ndi ziphunzitso zina zofunikira zomwe enawo amazifuna. Mwa chitsanzo, Alexander

Campbell anali mmodzi wa anthu omwe anayambirira kuona ndi kulalikira za kusiyana kwa pakati pa

mapangano akale ndi atsopano, ganizo iri tsopano likuvomerezedwa ndi kulandiridwa ndi zipembedzo zina

zomwe zimakana kusintha mwa chisawawa. Ndimakhulupirira kuti tiri nazo nzeru zofunikira pa za ubatizo

ndi utsogoleri mu mpingo.

3. Anthu adzatimvera ngati tiwalemekeza ndi kuwakonda. Kwa zaka zambiri, ndakhala ndi kuganizira kuti

ngati tifuna kuti anthu amvetse bwino zikhulupiriro zathu, kunali bwino tikanakhala nayo njira yabwino

yochitira zimenezi. Kudzichepetsa ndi chikondi kungatithandize kukalowa m’mitima yomwe kuuma moyo

Page 42: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 42

ndi chipongwe, ndi kupikisana sikungalowe (2 Timoteo 2:24-26). Mmodzi wa ophunzira anga, mkulu

wampingo, anandiuza kuti sanakhulupirira kuti mipatuko ingadzathetsedwe kufikira pamene anakhala ndi

kuphunzira mu maphunziro a SHBI ndi kuona anthu ochokera ku mipingo yosiyanasiyana mwa chidwi

akubvomereza chiphunzitso cha Baibulo. Mkulu wina anadabwanso Poona momwe anthu amenewa

anachita pokhalabe m’maphunziro ake omweo amfundo za kubwezeretsa omwe takhala tikuphunzitsa

nthawi zonse.

Tsiku lina madzulo ndinali kuphunzitsa pofotokozera chiphunzitso cha Calvinistic chomwe chimati

chirichonse chimatsogoleredwa ndi Mulungu ndipo palibe mwayi wopanga chisankho chifukwa Mulungu

ndiye amaoneratu zonse. Wina anathirira ndemanga yoti “zimenezi ndiye zitinso?” Ife timakhulupirira kuti

Mulungu amatipatsa mwayi wosankha chifuniro chathu.” Tsiku lina usiku ndinafotolozera za nkhani ya

Namani wakhate yemwe chikhulupiriro chake chinayesedwa polamulidwa kuti akasambe mu mtsinje wa

Yordano. Ndinafotokoza kuti nthawi zambiri Mulungu amafuna muyezo wina wake wa chikhulupiriro

monga njira yoonera chikhulupiriro chathu. Mkulu wina wopuma pa ntchito monga mphunzitsi wamkulu

yemwe anali ndi zaka 80, wampingo wa Baptist, wa nzeru zake ndithu, anafunsa kuti, kodi nawonso

ubatizo ungakhalenso njira yoyesera chikhulupiriro? Nthawi zonse ndimafotokoza kuti ubatizo ndi gawo

ndi nthawi yomwe chikhulupiriro chathu chimakumana ndi chisomo cha Mulungu ndi kubweretsa

chikhulupiriro. Ndi kukhulupirira kuti kupambana kwathu kungathe kufanizidwa bwino ndi kwa wina

aliyense pamene tifika pa ndime yolandira ulemu pa maganizo a chiphunzitso ndi chikhulupiriro chathu.

4. Ine ndimakhulupirira kwambiri monga ndakhala ndi kuchitira nthawi zonse pa za ubatizo, ngakhale

ndimaganizanso kuti pena pakenso sitinaganizire bwino ndipo tinasokoneza chiphunzitsochi chifukwa

chochita nacho mopitirira. Ngati mwana analandira ubatizo wa pamutu ali mwana, ndingamulimbikitse kuti

akwaniritse ndithu chiphunzitso cha Ambuye cha ubatizo ndipo achite zimenezi ndi chikhulupiriro

chakechake. Ngakhale kuti asanatulukire ndi kuona kufunika kwa zimenezi, sikuti ndikanakhala naye ndi

ubale wofanana ndi womwe ndingakhale ndi wina yemwe amakaniratu Yesu kukhala Ambuye wake.

5. Nimakhulupirira kuti kulakwitsa kumodzi kuopsa komwe kunachitika mu mbiri ya nthawi zosinthayi, pa

mbali yogawanitsa thupi la Khristu, kunali kukhulupirira kuti, “kuti ubatizo ukhale waphindu,

wobatizidwayo ayenera kumvetsa kuti ubatizowo umachotsa machimo. Maganizo amenewa amafalitsidwa

ndi mzaka za 1900 ndi Austin Mc Garry, yemwe anali mlembi woyamba wa bukhu lotchedwa “maziko

olimba” (Firm foundation). Chifukwa chenicheni cholembera bukhu limenelo chinali choti anthu aunikire

ndi kuona ngati kubatizidwa kawiri ndi kwabwino malingana ndi maganizo a David Lipscomb, mlembi wa

bukhu lotchedwa “kuyankhula mogwirizana ndi uthenga” (Gospel advocate) ku Tennessee ku America.

A. A Baptist ambiri akhala akuphunzitsa kuti chikhululukiro chimabwera panthawi yomwe munthu

akhala ndi chikhulupiriro mwa Khristu monga mpulumutsi, ndipo kuti ubatizo umangoonetsera kuyeretsedwa komwe kwa chitika kale. Mbale Lipscomb anali mmodzi wa atsogoleri omwe anagwira

ntchito pakati pa mipingo ya Khristu kumwera kwa America. Iye anakhulupirira monganso ambiri a ife

tichitira, kuti ubatizo ndi nthawi yomwe ife timalandira chikhululukiro cha machimo. Koma iye

anakhulupirira kuti sikwabwino kubatizanso kawiri mbaptist yemwe anafuna kulowa m’misonkhano

yathu. Iye anafotokoza kuti popeza anthu omwe anatembenuka mwa a Baptist amakhulupiriranso

mpulumutsi yemweyo amene ifenso timkhulupirira, anamva chisoni chifukwa cha machimo awo,

ndipo anafunitsa kukhululukira machimo ndi kubwera kwa Khristu monga mpulumutsi wawo ndi

Ambuye wawo, ndipo popeza ambiri a iwo ndi cholinga choti akadzichepetse ndikudzipereka ku

cholinga cha Mulungu, onse omwe anachita zimenezi analandira ubatizo woyenera ndi wolondola.

Lipscomb anakhulupirira kuti ngati panali chikhulupiriro chodzichepetsa mwa Mulungu, sikunalinso

kofunikira kwenikweni kuti munthu amvetse bwino machitidwe a nthawi yomwe iye anayeretsedwa,

kapena kutsatira mwatsatanetsatane lemba lirilonse lofotokozera za dongosolo la ubatizo. M’Njira ina,

amanena kuti, ife tomwe tinabatizidwa popanda kumvetsetsa bwino za mphatso ya Mzimu Woyera

tinayenera kubatizidwanso kawiri kuti tilandire Mzimu Woyera. Nkhani yonse iri mu bukhu

Lolembedwa ndi Jimmy Allen lothedwa “kubatizidwanso” (Rebaptism).

B. Alaliki athu oyambirira aja a m'gulu losintha zinthu aja sanabatiza kawiri a Baptist aja ayi koma

anangowatenga iwo ngati ziwalo za thupi la Khristu. Mipingo yambiri ya Khristu ya ku mmawa kwa

mtsinje wa Mississippi ku America anachitanso mogwirizana ndi maganizo a Lipscomb, ndipo pa

Page 43: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 43

mafika mzaka za m'ma 1980 iwo ochitira umboni uthenga anali kugwirizanabe ndi maganizo a

Lipscomb obatizanso kawiri. Mipingo yambiri ku Texas ku America, kumbali inayi, inakopedwa ndi

Mc Garry ndipo anayamba kuwatenga onse obatizidwa ndi a Baptist ngati osapulumutsidwa. Ine ndi

kukhulupirira kuti Lipscomb amalondola. Panalibenso njira ina yomwe tikanagwirizana kapena

kuganizira monga momwe taganizira kapena kugwirizanira pa ubatizo. Mwa chitsanzo, ngati malamulo

a boma lathu akanakhala kuti amafuna zonse, malumbiro a akwatiwo ndinso ………. Kuti apange ukwati weniweni wobvomerezeka, ndipo ngati akwatiwo adachita zonsezo koma ndi kuganiza iwo

analowa kale banja pochita malumbiro awo basi, ndani wa ife angathe kuwachititsa kuti abwererenso

nakayambenso ukwati wawo? Kodi sitikanakwanitsidwa popeza cholinga chawo chenicheni chinali

chofuna kulowa banja ndipo anachita zinthu zonse zofunikira? Ine ndi kuona njira ya Mc Garry

yobatizanso kawiri ngati gawo limodzi pa zochitika zoloza ku magawano ndi kulekana maganizo pa

malamulo, ndiponso losagwirizana ndi mtima kapena Mzimu wa uthenga. Ndipo ngati Lipscomb anali

wolondola ndi wokhoza, ndiye kuti tiri ndi abale ndi alongo ochuruka koposa momwe timaganizira.

6. Poonjezera pa kuononga komwe kumabwera chifukwa cha kugawanikana ku uthenga, munayamba

mwaganizira za momwe timachimwira pamene tikana abale ndi alongo omwe Mulungu anawalandira?

Kumbukirani wamkulu uja anamutcha mwana wolowerera uja kuti “mwana wanu uja” m’malo moti

“mbale wanga.” Kodi ife mwa kusadziwa kwathu sitinanenepo zinthu zina zonyoza anthu ena omwe ndi

odzadza ndi chikhulupiriro ndi odzipereka kwambiri kwa Khristu ndiponso ali a nzeru ndi odziwa malemba

monga ife tiriri? Mzaka zanga zoyamba ntchito yanga yotumikira ngati m’mishonare, ndinalemba nkhani

za ubatizo zomwe ndimaika kunja ana a Mulungu ambiri. Ndiri wodzadzidwa ndi manyazi ndipo ndi

kupempha chikhululukiro kwa Mulungu ndi kwa inu a mumpingo.

A. Ngati Mulungu amagwiritsa ntchito chizindikiro cha Mzimu Woyera monga chomdziwitsa za anthu

ake, kodi ife tingathe kunyalanyaza chipatso chobadwa chifukwa cha Mzimu Woyera wopezeka

m’miyoyo ya okhulupirira odziperekawa?

B. Kodi ife tokha tiri ndi choonadi chonse? Tiri ife kodi olungama, kapena tidalira pa chisomo? Ngati

tidalira chisomo, kodi ndiye kuti chisomocho chimangogwira ntchito pa kuperewera kwathu kokha,

kapenanso ngakhale zolakwika zosiyanasiyana ndi zofooka za anthu ena? Kodi tikudziwa ntchito

yaikulu yomwe chisomo chimagwira pamene anthu alemekeza Khristu monga Ambuye

mokhulupirika? Kodi tidayamba tapanga chisankho pakati pa chisomo ndi lamulo?

7. Tinasochera kuchoka pa kumvetsa bwino zomwe malemba anena za umodzi womwe unaphunzitsidwa ndi

omwe anayambitsa ntchito yobwezeretsa. Tiyenera kulapa ndi kupempha chikhululukiro cha Mulungu

chifukwa chokaniza ana ambiri a Mulungu powatcha akunja, osapulumutsidwa. Ntchito ya gulu lathuli

yakhala ikutsutsa ena chifukwa chogawikana ndi kulowa m'mpitatuko. Komanso pamene nafenso tiri ndi tchimo longa lomwelo. Mau oti “mpatuko” satanthauza “munthu yemwe amaphunzitsa kuti kudzilekanitsa

wekha podzitengera dzina la padera lakolako. Nakhale dzina loti mpingo wa Khristu ndi dzina labwino

ngati cholinga chathu chiri chongofuna kulemekeza Khristu, nkotheka kusagwiritsa ntchito dzinali

moyenera wampatuko ngati cholinga chathu ndi chodzilekanita ndi anzathu monga mpingo wokhawo

wokhulupirika woyenera kumasonkhana wokha. Baibulo limapereka maina ambiri ampingo, koma mipingo

yambiri yomwe tipembezako singalole kutchulidwa “mpingo wa Mulungu,” kapena “Banja la Mulungu,”

“ana a Mulungu.” Izi zikungoonetsa momwe ambiri a ife takhalira amipatuko pa za dzina loti “mpingo wa

Khristu.”

Tikukhala m’masiku oyipa ndipo kuipitsitsa kungabwerebe. Tiyenera kufikira ambiri a osochera monga

momwe tingathere. Ndi kovuta kukonza zofooka ndi zotchinjiriza zomwe zimasokoneza uthenga

zoyambitsidwa ndi malekano osafunika osabvomerezeka ndi Baibulo. Posachedwapa tidzaima pamaso pa

Mulungu. Tiyenera kuopa Mulungu koposa zinthu zomwe munthu sadzibvomereza. Tiyenera

kudzichepetsa ndikachita ndi pemphero la Ambuye lija la umodzi ndi chidwi chonse. Tiyenera kugwirana

dzanja ndi okhulupiria ena omwe anabadwanso mwatsopano kuzipembedzo zinazo, ndi anthu omwe mwa

iwo Mzimu Woyera akuchita nawo mwa chionekere. Kuti tichite izi sikuti tiyenera kutaya chimodzi cha

zikhulupiriro zathu za m’Baibulo. Pamene ubale pakati pathu ndi iwo ukukula, ndipo pamene akuona

Khristu mwa ife, adzayamba kulemekeza kwambiri Khristu pa china chirichonse chomwe Khristu

Page 44: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 44

adzawaphunzitsa kudzera mwa ife. Ndipo ngakhale atapitirira kulekana maganizo pa zina zazing’ono

m’malemba, izi siziwachititsa kuti akhale anthu osochera ayi. Anthu sapulumutsidwa chifukwa

kukhulupirira bwino za mphamvu za Mulungu pozifanizira ndi chifuniro chake cha munthu, kapena pa za

Baibulo lotanthauziridwa bwino, kapena pa za mphatso za Mzimu Woyera kapena pa za makhalidwe ake a

pakutha pa zaka chikwi. Chomwe chimafunikira kwambiri ndi ubale wathu ndi Khristu. Ngati ena a ife

adzapulumutsidwe, chidzakhala chifukwa cha mphatso ya mwazi wa Khristu, osati chifukwa choti tinali olondola ndi ochita bwino pankhani zonse za malemba ayi.

Malekano akufa pang’onopang’ono m’malo ambiri. Anthu tsopano akukhala ndi chidwi chofuna kuiwala

kusinjirirana za mipatuko ndikuyamba kungomvera chiphunzitso cha Baibulo chosavuta. Mipingo yambiri

m’dera la kwathu posachedwapa yasiya maina odzipatsa chifukwa cha kupatukana. Mipingo yambiri ya

ganiza zomatsogoleredwa ndi akulu a mpingo kaya kuti oyang’anira – Abusa. Anthu a m’zipembedzo

zambiri akuitanitsa ziphunzitso zotsamira ndi kudalira Baibulo. Anthu mazana anayi (400) ochokera ku

zipembedzo zosiyanasiyana m’dera la Houston amalembetsa kuti alowe m’maphunziro ochitika pa sukulu

ya Baibulo ya South Houston chaka chiri chonse. Ife timaphunzitsabe zomwe tikhulupirira za Baibulo,

ndipo popeza timawaphunzitsa anthuwa mwa ulemu ndi modekha mwa Mzimu ndi moyo wa Khristu, iwo

amakondweretsedwa kubwera ndi kudzaphunzira.

Ngakhale mu Chikatolika mulinso kubwerera kumachitidwe a mpingo woyamba; mpingo uliwonse womwe

ndi womangidwa m’masiku ano ku Houston udzakhala nalo damu lobatizira pobiza thupi lonse. Mkulu

wina wachinyamata wa mpingo wa Hispanic anabwera ku ofesi kwanga sabata yathayo ali wosangala ndi

wotengeka chifukwa anali wofuna kuyamba maphunziro. Iye amachokera ku mpingo womwe unasankha

kudzitcha kuti “mpingo wobwezeretsa”. Iye amafulumiza kuzindikira za malingaliro athu obwerera ku

Baibulo. Sikuchokera zaka mazana awiri (200) zapitazo pamene takhala ndi mwayi wothandiza anthu kuti

akhale amodzi mwa kudzichepetsa kwa malemba.

Zoonjezera: Zothandizira Zina pa Phunziro la Umodzi

Mafunso Othandizira Phunziro la Aroma 14:1-15:13

1. Kodi anthu onse a mumpingo amamva mofanana, kapena ali ndi chidziwitso cha chikhulupiriro

chofanana? 14:1.

2. Kodi “nkhani zazing’ono” ndi chiyani? (14:1). Kodi mawu amenewa a masuliridwa motani m’mabuku

enawo?

3. Kodi mfundo zonse za choonadi cha chipembedzo zimamveka mofanana m’malemba? Kodi mfundo zonse

ndi zofunikira monga maziko a chipulumutso?

4. Kodi alipo Mafunso ena okhudza za chipembedzo kapena makhalidwe a Chikhristu omwe kungatheke kuti Akhristu awiri okhulupirika angathe kusiyana maganizo?

5. Kodi ndi nkhani ziwiri ziti zazing’ono zomwe Paulo apereka mona zitsanzo mu Aroma 14:2-8? Kodi

muganiza kuti kusiyana maganizo kumeneku kunachokera m’maganizo ati?

6. Kodi chikhulupiriro chofooka (kapena chidziwitso cha choonadi cha chikhulupiriro) chidampangitsa

bwanji kukhala ndi moyo wolimbikira kukana zina?

7. Kodi ndi zinthu zinanso ziti zomwe timaonetsa kulekana kwathu (zazing’ono) zomwe ziriponso pakati pa

Akhristu lero?

8. Kodi Mkhristu wolimbayo (wosabvutika ndi chikumbumtima chodziletsa) anayesedwa pokhala ndi moyo

wotani kwa mbale wake wofookayo? Kodi mbale wofookayo anayesedwa ndi moyo wotani kwa mbale

wake wosamangikayo? 14:3,10.

9. Kodi Paulo anamlamulira chiyani mbale wolimbayo? Nanga wofookayo, womangikayo? 14:3,10.

Page 45: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 45

10. Kodi pamenepa ndiye kuti Paulo akunena kuti anthu angathe kukhala ndi zikhulupiriro zosiyana ndinso

machitidwe osiyana munkhani zimenezi komabe ndi kumakhalirana bwino mwa mtendere mumpingo

umodzi?

11. Kodi ziripo mfundo zina zofunikira ndinso choonadi chomwe tonse tiyenera Kudzibvomereza ndi

kuzilandira ngati tifuna kuti tikhale amodzi? Aefeso 4:1-6; 1 Akorinto 15:3-8; 1 Timoteo 3:16.

12. Nchifukwa chiyani payenera kukhala kulolerana ndi kugonjerana pokhudza nkhani zazing’ono ngati tifuna

tigwire ntchito ngati mpingo?

13. Nchifukwa chiyani kuli kobvuta kugwiritsa ntchito chiphunzitso ichi cha kulolerana ndi kugonjera pa

mfundo zokhudza kupembedza kwa gulu lonse osati pa mfundo zokhudza kungosintha chabe?

14. Kodi tilipire yani nkhani za zolimbana zazing’ono zing’onozi? 14:10-12.

15. Kodi abale omwe asiyana maganizo ayenera asachite chiyani? Ayenera alimbikire chiyani? 14:13.

16. Ngati munthu akayika ndi china kapena mfundo ina, kodi iye mwini ayenera kuchita chiyani? 14:14,23.

17. Ngati mbale wofookayo womangika m'chikumbumtima ali pomwepo kapena zimkhudza, kodi mbale

wolimbayo wosakaikayo asachite chiyani? 14:13-21.

18. Nanga naye mbale wofookayo, kumbali yake asachite chiyani? 14:3,13.

19. Kodi ndi kulakwa kuti mbale wofookayo odzudzula ufulu wa mbale wake wolimbayo monganso momwe

mbale wolimbayo kuchita zinthu zomwe zikhumudwitse mbale wofookayo? Kodi machitidwe awiri

onsewa amalimbikitsa kulakwirana ndi magawano pakati pa Akhristu?

20. Kodi tiyenera kuika umodzi ndi moyo wabwino ndinso kuchita bwino kwa mpingo patsogolo pa chiyani?

21. Kodi olimba ayenera kumachita chiyani? Nanga sayenera kumachita chiyani ngati atsata chitsanzo cha

Khristu? 15:1-3.

22. Nchifukwa chiyani kumakhala kosabvuta kuti mbale wolimba azindikire kuti nkhani iyi ndi yaing’ono

kusiyana ndi mbale wofooka? Kodi zingatheke kuti mfundo ina iwoneke ngati lamulo koma ndi kutheka

kuti ine ndizindikirebe kuti pali mpata woti ndi sagwirizane nazo mokhulupirika?

23. Tiyenera kumalolerana wina ndi mnzake m'njira yomweyo yonga ndani analandira ndani?15:7.

24. Kodi zimene zija zinangochitika chifukwa cha kuchita bwino kwathu, kapena chifukwa cha chisomo?

25. Ngati mbale wolimba uja ndi wofooka uja analibe chidwi chochita ndi kulekana maganizo kwawo

mogwirizana ndi maganizo a Paulo aja mundimeyi, koma kulimbikira pa kudzudzulana kapena

kunyozana, kapena kulakwirana mwadala kotero kuti kulekana kukanayambika, kodi mpingo

ukadatani nawo? 16:17,18.

26. Yemwe anachita motere sanatumikire Khristu kapena kukonda koma anali kutumikira chiyani?

27. Kodi 1 Akorinto 8:1-13 ndi 10:23-33 akulozera chiyani munkhani imeneyi?

28. Sititaya kwakukulu ngati titaya nyama ndi cholinga chofuna kupewa choyambitsa kupunthwa. Koma nanga

bwanji ngati palinso china chomwe mpingo ukanapindula nacho ndi kufikira mizimu yambiri, koma

chikhumudwitsa m’modzi kapena awiri mumpingo? Kodi nthawi zina timathawitsa abale kapena

kufooketsa abale ambiri ndi cholinga chofuna kupewa kukhumudwitsa ochepa? Kodi Paulo amatanthauza

zimenezi pa chiphunzitso chake cha m’misonkhano chija?

Page 46: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 46

Zothandiza Powerenga Aroma 14:1-15:7

Mu Aroma 14:1-15:13 Paulo akupitiriza kuphunzitsa za machitidwe akhalidwe ndi moyo wa Mkhristu

malingana ndi chifundo chomwe Mulungu wationetsera. Gawo limeneli likuona mwapadera momwe

tingakhalire ndi umodzi mumpingo ndinso monga abale ndi alongo mwa Khristu, ngakhale timakhala nako

kusiyana m’maganizo ndi zikhulupiriro pa nkhani zina “zazing’ono.” Iri ndi bvuto lomwe limakhalapo chifukwa cha umunthu wathu wauchimo kuchokera mu zifukwa zosiyansiyana ndi masiyanidwe a makulidwe

m'nzeru ndi kukhwima.

Zoyenera kuyang’ana mu Aroma 14:1-15:13

14:1: Yemwe chikhulupiriro chake chiri chofooka mumlandire. Yemwe ali womangika malinga ndi

chikumbumtima chake ndipo “amangosiya” zinthu zambiri zomwe Mulungu sanaletse; yemwe sanakhwime

m’chikhulupiriro ndi chidziwitso cha Khristu kokwanira kuti amvetse ufulu womwe tiri nawo mwa Khristu.

Popanda kuweruza pa zinthu zazing’ono [NASB: osati ndi chifukwa chofuna kuweruza malingana ndi

maganizo ake; RSV: koma osati chifukwa cholimba pa maganizo.]

Mawu a Mulungu anazindikira kuti chifukwa cha kufooka kwathu kwa umunthu, mfundo zonse zolondola

kapena zolakwika zimamveka bwino kwa ife, choncho zina ndi zoti titha “kulekana maganizo.” Komanso

m’malembo sananenemo zambiri za Mafunso ena koposa enanso. Mpata ulipo kwa anthu okhulupirika, oopa

Mulungu wosiyana maganizo munkhani ngati zimenezi.

Malembonso amazindikira kuti sinkhani zonse za chikhulupiriro cha Chikhristu chachikulu mofanana kapena

mofunikira – Mateyu 5:19; 23:23. Alipo malemba omwe ali ndi mndandanda wa ziphunzitso ndi zikhulupiriro

zazikulu – Aefeso 4:4=6; 1 Akorinto 15:3=4; Aroma 14:17; Mateyu 22:35-40. Ziphunzitso zazikulu zimenezi

zomwe ziri monga maziko zimaphunzitsidwa m’malemba kawirikawiri komanso mwadongosolo kuposa zina

zazing’ono zija. Palibe mwayi waukulu wololedwa kulimbana pa ziphunzitso zazikuluzi.

Mulungu amvetsa mwangwiro, koma amadziwa kuti ife sitiri choncho ayi. Gawo limeneli likuonetsa poyera

kuti titha kukhalirana pamodzi ndi kumagwira ntchito pamodzi mumpingo popanda kugwirizana pa mfundo

zina zazing’ono, zomwe pa umunthu wathu mwayi ulipo woti titha kutsutsana mokhulupirika. Palibe wina wa

ife yemwe amaona zinthu mwangwiro, kapena yemwe amamvera mwangwiro. Chisomo chiyenera kutchinjiriza

kusamvetsa kwathu monga momwe chimatchinjirizira kusachita mwangwiro kwathu. Ndipo tiyenera kuchitira

chifundo iwo omwe timalekana nawo maganizo monga momwe Mulungu amapatsiranso ife chisomo. Tiyenera

kukana yemwe akana chiphunzitso ndi chikhulupiriro chachikulu, chofunikira chenicheni cha Chikhristu – 2

Yohane 9-11. Koma tiyenera kulandira, osati kukana, yemwe tasiyana naye mu nkhani ndi mfundo

“zazing’ono.”

Kodi tingadziwe bwanji zomwe ziyenera kutengedwa ngati nkhani zazing’ono?

14:2-12: Kuchokera mu mpingo wa ku Roma, Paulo akupereka zitsanzo ziwiri za nkhani zazing’ono zomwe

Akhristu angathe kusiyana maganizo komabe ndi kumagwira ntchito pamodzi mwa Khristu. Chikhulupiriro cha

munthu wina chimlola kudya chirichonse (iye akudziwa kuti Yesu “anayeretsa zakudya zonse” – Marko 7:19 –

ndi kutinso “fano sirili kanthu” – 1 Akorinto 8:4) – Koma munthu wina, amene chikhulupiriro chake chiri

chofooka, adya masamba okha. Iye akhulupirira kuti ndi kuchimwa kapena kungakhale kuchimwa kudya

nyama. Omasulira ena amaganiza kuti yemwe akumangikabe ndi lamulo la Chipangano Chakale la zakudyali

ndi Myuda. Ena amaganiza kuti ndi wa amitundu yemwe wangotembenuka kumene kuchokera ku kupembedza

mafano yemwe tsopano ali wosamala kwambiri pa za chakudya chomwe chikuperekedwa ku mafano poyamba

ndipo kenako kugulitsidwa ku misika yakunja. Atha kuganiza kuti chakudyacho chaipitsidwa mwa uzimu

chifukwa chinaperekedwa kwa mafano m’mbuyomo. Myudanso angaganize mwa mtundu womwewo.

Chikhulupiriro cholimba chingamuthandize munthu ameneyu kuti aone kuti chakudya ndi chakudya ndiponso

kuti fano liribe uzimu weniweni. Fano ngakhale mdierekeze wokhala pambuyo pa fanolo alibe mphamvu ya pa

munthu wina aliyense kupatula munthu yekhayo amene aopa fanolo m’maganizo mwake. Koma ngati fanolo

alilumikiza m’maganizo ake mwa uzimu ndi chakudyacho pamenepo ndiye kuti chakudyacho chiri

chosayeretsedwa kwa iyeyo.

Page 47: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 47

Mwa chitsanzo china, mundime 5, munthu wina atenga tsiku lina monga loyera kuposa linzake; wina

angotenga masiku onsewo monga chimodzimodzi. Kusunga tsiku loyamba la Sabata monga “tsiku la Ambuye”

pokumbukira kuukanso kwa Khristu sinkhani yomwe iri mumtima ayi. Tsiku limeneli linalandiridwa ndi

Akhristu onse oyamba aja ngakhale anali ndi maganizo osiyanasiyana pa za masiku enawo. Pano Paulo

akunena za masiku achipembedzo a padera, a munthawi za Chipangano Chakale ndi malamulo ake aChiyuda:

masabata kapena masiku opumula Mulungu uliwonse, kulemekeza “kutuluka kwa mwezi uliwonse”, ndi miyambo yina yachipembedzo yochitika chaka ndi chaka mwa chitsanzo paska, Pentekoste, kumasulidwa ndi

zina zotero

Chikhulupiriro cha uthenga wabwino chidawamasula Akhristu, kaya Ayuda, kaya amitundu ku kudalira pa

zinthu zimenezi (Akolose 2:13-17), koma ngati china chinali cholinga cha Mulungu, nkobvuta kuti tichisiye

ndikuyamba choonadi chinanso chatsopano. Choncho tiri ndi Akhristu ena mumpingo wa ku Roma omwe

akudya nyama pamene ena sadya; ena akusungabe mwambo wakale cha Chiyuda wosunga ndi kulemekeza

masiku ena pamene ena satero ayi.

M’masiku ano tiribe bvuto limeneli kwenikweni mumpingo koma tiri ndi mabvuto ena olekana maganizo pa

nkhani zina “zazing’onozing’ono”. Pali nkhani za khalidwe labwino, lobvomerezeka: Kodi kubvala kwabwino

ndikuti? Kodi amuna ndi akazi asambe malo amodzi kunyanja? Kodi Mkhristu abvine dansi? Kodi ndi zithunzi

ziti zomwe Mkhristu sayenera kuona? Kodi nyimbo zonse za magatala ndi zachabe? Kodi Mkhristu achite ndi

fodya? Kodi kungolawa pang’ono ndi kwachabe, popeza munthu saledzera nako? Kodi pa nthawi yochezerana

mwamuna ndi mkazi, khalidwe lobvomerezeka ndi liti?

Palinso Mafunso ena a chipembezo ndi ntchito za mpingo, zomwe zina za izo zitsatidwa ndi kuchitidwa ndi

maganizo osiyana pakati pathu mobwerezabwereza: Kodi tikhale ndi mgonero wa Ambuye kangati? Kodi

tiyenera kukhala ndi kalasi mumpingo? Kodi tikhale ndi zikho zingati zomwera chipatso cha mpesa munthawi

ya mgonero? Kodi nyimbo zoimbira ndi zida ndi zobvomerezeka m'chipembedzo? Kodi mwamuna amene

analekana ndi mkazi wake mwa malemba angathe kukhala woyang’anira/mbusa? Kodi nchoyenera kuika

atumiki achikazi? Kodi mipingo ingathe kugwirizana kudzera mu utsogoleri wa mpingo womwe wayambitsa

ntchitoyo pa ntchito zina zazikulu? Kodi ndi chobvomerezeka kuomba m’manja mumpingo? Kodi zisudzo

zimaloledwa mumpingo? Komanso pali Mafunso ena a ziphunzitso ndi zikhulupiriro: Kodi Khristu adzabwera

patapita zaka chikwi kapena pasanapite zaka chikwi? Kodi mphatso za zozizwitsa zikuchitikabe mumpingo

lero? Kodi zimatheka kuti Mkhristu agwe kuchoka m’manja mwa Khristu ndi kutayika?

Pamene Akhristu asiyana maganizo “pankhani zazing’ono,” machimo awiri amayenera kufika: mbale wolimba

yemwe mwa chikhulupiriro chake amadya nyama anganyoze mbale wofooka yemwe chikumbumtima chake

chimletsa; ndipo mbale wofookayo angadzudzule mbale yemwe ali ndi ufulu uja. Paulo akuletsa zonsezi.

Munthu yemwe adya zonseyo asanyoze (NASB): tiganizirane mosanyozana; RSV: osanyoza) iye amene sadya;

ndipo munthu amene sadya chirichonse asadzudzule (NASB: asaweruze; RSV: asaike chiweruzo pa) munthu yemwe amadya. Chifukwa chiyani? Popeza Mulungu amulandira iye. Mulungu angalandire munthu yemwe

kwa ine aoneka monga wolakwa.

Munthu yemwe ali ndi chikumbumtima cha choonadi, yemwe adziwe zambiri za chikhulupiriro, nthawi zonse

amakhala pa mayeso odzitukumula podziona ngati wapamwamba kuposa wina yemwe sanadziwe kwambiri

uja, pomutenga ngati wosafunikira kwa Mulungu ndi mpingo. Chidziwitso chimatukumula, koma chikondi

chimamangirira. Munthu yemwe aganiza kuti adziwe zambiri alinakonso kuperewera kwina” – 1 Akorinto 8:1-

2. Kudzitukumula ndi dzenje la anthu omwe amaganiza kuti iwo ndiye odziwa kuposa ena onse. Munthu

womangidwa ndi chikumbumtima uja, ngakhale kuti kwenikweni zimachitika chifukwa cha kusakhwima mu

uzimu, nayenso amakhala pa mayeso oganiza kuti mbale wake wokhala ndi ufulu uja, ngati wosasamalira

malamulo a Mulungu ndi kumudzudzula. Kumakhala kobvuta kwa iye kuti azindikire “nkhani zazing’ono”

monga momwe ziriri ndi kusiyira zina zonsezo kuti Mulungu ndiye aweruze pamene iye apitiriza kutumikira

Mulungu.

Bvuto la maganizo a mbale wolimbayo lingathe kuononga ubale ndi kubvulaza umodzi wampingo. Kudzudzula

komwe mbale wofooka uja amachita mwa chisawawa kwa ena kungathenso kuononga ubale ndi umodzi. Ngati

mmodzi wa onsewa achita zimenezi mpaka kufika poti pakhale kulekana ndi kugawikana, Paulo akulamulira

Akhristu kuti tisamale naye ndi kupatuka pa iye. Munthu woteroyo angodzisangalatsa ndi zomkondweretsa iye

mwini (kukakamira kufuna kutchedwa wochita bwino mwa yekha kapena chakudya, kapena kuchita

mwangwiro). Iyeyo sakutumikira Khristu – Aroma 16:17,18.

Page 48: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 48

Bvuto la maganizo a mbale wolimbayo lingathe kuononga ubale ndi kubvulaza umodz wampingo. Kudzudzula

komwe mbale wofooka uja amachita mwa chisawawa kwa ena kungathenso kuononga ubale ndi umodzi. Ngati

mmodzi wa onsewa achita zimenezi mpaka kufika poti pakhale kulekana ndi kugawikana, Paulo akulamulira

Akhristu kuti tisamale naye ndi kupatuka pa iye. Munthu woteroyo angodzisangalatsa ndi zomkondweretsa iye

mwini (kukakamira kufuna kutchedwa wochita bwino mwa yekha kapena chakudya, kapena kuchita

mwangwiro). Iyeyo sakutumikira Khristu – Aroma 16:17,18.

Ndi kulakwa kuti mbale aliyense aweruze mbale wake (kumtsutsa kapena kumtenga ngati wopanda pake). Kodi

ndiwe yani woti ukaweruze wantchito wa mwini wake? Mbale aliyense amayang’aniridwa ndi kuyankha zonse

kwa Mulungu poyambirira. Sindiyenera kutenga udindo wa Mulungu wakuweruza. Munthu amaima kapena

kugwa kwa Ambuye wake (yemwe ndi Mulungu). Ndipo adzatha kuimanso, chifukwa Ambuye angathe

kumthandizanso kuti aime, ngakhale atakhala ndi zomwe zioneka ngati zolakwika, malingana ndi zomwe ine

ndiganiza ndi kukhulupirira pa nkhani zina zazing’ono.

Paulo atipatsa mitu itatu yoti ititsogolere pa khalidwe lathu mu ndime imeneyi:

1. Aliyense akhale wokhutitsidwa mumtima mwake (v5c). Aliyense wa ife ali ndi udindo womvetsa ndi

kuganizira mosamala kwambiri chomwe akukhulupirira kuti ndicho cholinga ndi chifuniro cha Mulungu pa

nkhani kapena mfundo iriyonse. Ngakhale sitingathe kumva mvemvemve monga amachitira Mulungu,

tiyenera kukhala ndi njala ya kumva malembo monga momwe tingathere. Tiri ndi udindo wophunzitsa

chikumbumtima chathu. Ife sitiri oweruza maganizo a wina aliyense ayi.

2. Ngati wina aliyense aona chinthu china monga chodetsedwa (choipa) ….. kwa iyeyo ndi chodetsedwa ……

munthu yemwe akaika achimwa ngati adya, chifukwa sadya ndi chikhulupiriro (vv. 14b,23). Ngati

ndilakalaka kuchita chinthu chomwe ndi kuchikaikira kapena kukhulupirira kuti ndi choipa, ndiye kuti ndiri

ndi mzimu wa wochimwa wa chilakolako ngakhale kuti Mulungu saletsa chinthu chomwe ndikuchitacho.

Ndiyenera kumalolera maganizo a ena pa nkhani ndi mfundo zazing’ono, koma ndiyenera kumvera

mosamalitsa chomwe chikumbumtima changa chindiuza kuti ndi chobvomerezeka.

3. Ganizirani kuti musaike chopunthwitsa kapena cholepheretsa chirichonse m’njira ya mbale wanu.

Malingana ndi kukhwima kwa chikumbumtima chanu, chingathe kukulolani kuchita zinthu zina zomwe ena

amaziona ngati zoipa ndi zolakwika, komabe musamangochita zimenezi nthawi iriyonse kapena pamalo

pena paliponse pomwe zingabvutitse ndi kuyambitsa mabvuto kwa mbale kapena mlongo wanu.

Iye yemwe aona tsiku limodzi ngati lofunika kuposa linzake, atero kwa Ambuye. Iye yemwe adya nyama kwa

Ambuye, chifukwa ayamikira Mulungu, ndipo iye yemwe sadya, atero kwa Mulungu. Ndi chinthu chofunika

kudziwa ndi kuchita chifuniro cha Mulungu molondola monga momwe tingathere, koma koposa zonse, ndi kofunikira kuchita zonse zomwe timachita ndi cholinga cholemekeza Mulungu. Ngakhale sitimvetsa

bwinobwino, Mulungu amazindikira cholinga chathu chofuna kumulemekeza ndi kumumvera. Kaya moyo

kaya imfa, ife ndife ake a Ambuye. Ife tiri m’manja ake mu zonse, pa zonse ndipo timayankha china chiri

chonse kwa iye, tiri pansi pa ulamuliro wake m’zonse, koposa wina aliyenseyo, ndipo tiyenera kuchita china

chirichonse chomwe tingathe kuti timkondweretse.

Uweruziranji mbale wako ….. upepusiranji mbale wako? Popeza tonse tidzaima pampando wachiweruzo wa

Mulungu. Ngati ndiweruza mbale wanga yemwe “ali womasuka” kusiyana ndi ine munkhani zazing’ono, ndiye

kuti ndi kutenga malo ndi udindo wa Mulungu wakuweruza. Ngati ndinyoza ndi kupepusa mbale wanga

womangiririka ku chikumbumtima chake, chimodzimodzinso ndiye kuti ine ndi kudzikweza koposa iyeyo,

chinthu chomwe ndi Mulungu yekha angathe kuchichita mwa mphamvu yake. Podziwa kuti tonsefe tidzaima

pampando wachifumu ndi kunena ntchito zathu zonse kwa Mulungu tiyenera kukhala odzichepetsa pochita ndi

anzathu pamene pabuka kusamvana. “Musaweruze pakuti inunso mungaweruzidwe. Popeza m’njira yomweyo

muweruzira ena, inunso mudzaweruzidwa nayo.” – Mateyu 7:1,2. “Choncho aliyense wa ife adzafotokoza

yekha ntchito zake kwa Mulungu. Choncho ziripotu zinthu zina zomwe ndiribe ufulu woweruza. Nditha

kungozisiyira pakati pa Akhristu anzanga ndi Mulungu.

Izitu sizitanthauza kuti sitiyenera kuweruza pa chirichonse chabwino kapena choipa. Mu Aroma 14, Paulo

sakunena za zinthu zazikulu, zodziwikiratu za zabwino ndi zoipa, koma iye akunena za zinthu zazing’ono

zomwe tiri nawo mpata wokambirana. Akhristu pamodzi ndi atsogoleri, nthawi zina amapatsidwa mwayi

Page 49: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 49

woweruza zina zazing’ono – 1 Yohane 4:1-3; 1 Akorinto 5; Mateyu 18:15-20; Machitidwe 17:11. Tiyenera

kukhala ndi luntha pamodzi ndi nzeru zotithandiza kusiyanitsa mfundo zazikulu zosayenera kusewera nazo

mwa uzimu ndi mfundo zazing’ono zomwe tingathe kuweruza. Kufooka kwathu pa mfundo imeneyi ndiko

kuwalowetsa “libolonje” m’mbiri ya mpingo.

14:13-23: Choncho (popeza tonse tidzaweruzidwa ndi Mulungu), tiyeni tisiye kumaweruzana (kaya ndi mbale wamphamvu kunyoza mbale wofooka, kapena wofooka kudzudzula ndi kuweruza wamphamvu ndi

wolimbayo) m’malo mwake sankhani kusaika chopunthwitsa kapena chokhumudwitsa, m’njira ya mbale wako.

Ngati ine mwa ufulu wanga, ndichita chomwe chioneka cholakwika ndi chosabvomerezeka kwa wofooka uja,

ndiye kuti ndingamupunthwitse munjira ziwiri:

1). Ndimupangitsa kuti kukhale kobvuta kwa iye kuti iye ndi ine tikhale “amodzi” – angathenso kusiya

kusonkhana ndi kupembedza;

2). Ndimupangitsa kupitiriza kuchita zomwe inenso ndi chitazo ngakhale zioneka zolakwika kwa iyeyo ndipo

potero adzaswa maganizo a chikumbumtima chake pochita zimenezi. 1 Akorinto 8:1-13 ndi 10:23-33 ndiwo

maziko a chaputala chimenechi omwe ayenera kuwerengedwa ndi mavesi omwe alembedwawo. Ine

ndikhulupirira kuti palibe chakudya chomwe ndi chodetsedwa mwa chokha. Koma ngati wina aona chinthu

china ngati chodetsedwa, ndiye kuti chinthucho ndi choipa kwa iyeyo ndipo zidzakhala chomwecho mpaka

pomwe chikumbumtima chake chidzamasuke chifukwa cha kukula mu chikhulupiriro. Taonani vesi 23 ndipo

mufanizire. Munthu yemwe akaikira aweruzidwa ngati adya, chifukwa sadya ndi chikhulupiriro; ndipo china

chirichonse chomwe sichichokera ku chikhulupiriro chiri tchimo.

Chikondi chenicheni sichikondwera kubvutitsa anthu ena. Ngati mbale wako akhumudwa ndi chomwe iwe

ukudya, ndiye kuti iwe suchita mwa chikondi. Chakudya chanu (kaya china chirichonse) pamenepa ndiye kuti

chafika pa ndime yofunikira koposa mtendere wa mbale kapena mlongo wanu komanso ndi ubale wanu.

Khristu anafa, anapereka moyo wake, kupulumutsa mbale wanuyo. Simaganizo abwino ngati simudzalolera

kusiya nyama ya nkhumba (kaya china chirichonse) ndi cholinga chofuna kupewa kumutengera kukuonongeka.

Taonaninso ndime 20: Musaononge ntchito ya Mulungu (Mzimu wa mbale wanu ndi ntchito yonse yomwe

Mulungu anachita kuti aipulumutse) chifukwa cha chakudya.

Musalole kuti chomwe muchiona ngati chabwino anthu anene kuti ndi choipa. Paulo sakunena kuti “musalole

mbale wanu wofooka kukuletsani chomwe chikumbumtima chanu chikulolani kuchita.” Koma akunena kuti

chomwe muchiona ngati choyenera ndi chabwino chingathe kukhala chodetsedwa ngati muchigwiritsa ntchito

yoti muvulaze moyo wa uzimu wa mbale wanuyo. Ngati khalidwe lanu limadalira kapena lilingana ndi ufumu

wakumwamba, chiyero, ufulu, chimwemwe ndi zokhazo zomwe mudzakhala mukuganizira kwambiri, osati

kaya mudya kaya mumwa chomwe mumakonda, kaya kubvala chirichonse, kaya kupita kuzikondwerero zina.

Ngati tiika chiyero, ufulu, chimwemwe ndi mtendere wa abale anthu ndi alongo athu patsogolo koposa zonse zodzikondweretsa tokha, ndiye kuti tikukondweretsa Mulungu ndipo tiri kubvomerezedwa ndi anthu.

Choncho tiyeni tiyesetse kulimbika ndithu kuchita chirichonse chomwe chikapherezere ku mtendere ndi kukula

koyenera. Ngati ichi chitanthauza kusiya zinthu zina zomwe ziri zobvomerezeka nane koma zokhumudwitsa

kwa mbale wanga wofookayo, zikhale chomwecho. Chakudya chonse ndi choyeretsedwa, koma sibwino kuti

munthu adye china chirichonse chomwe chingapunthwitse winayo.

Chirichonse chomwe mukhulupirira zinthu zimenezi (zakudya, masiku ndi zina zotero) zikhale pakati pa inu

eni ndi Mulungu wanu. Paulo sakutanthauza kuti nkosayenera kukambirana za zimenezi ndi mzimu wabwino

pakati panu ndi iwo omwe tisiyana nawo maganizo, kapena kuphunzira nawo pamodzi ndi cholinga chofuna

kuchepetsako kusamvanako. Iye akutanthauza kuti kaya maganizo anga “ndi omasuka” kaya omangika,

sindiyenera kumangoumirira pa maganizo anga omwewo ndi kulimbikitsa makangano. Maganizo athu

asadzadze ndi moyo wongofuna kulimbana pa mfundo zazing’ono koma adzadze ndi mfundo zazikulu ndi

zofunikira za Khristu. Paulo afuna kuti tonse tigwirire ntchito pamodzi ngakhale timasiyana m’maganizo ndi

mfundo zazing’ono ndikuti tisiyire kuweruza komaliza pa mfundo zazing’ono kwa Mulungu mwini.

15:1-3: kumbukirani kuti panalibe kulekanitsa machaputala ndi mavesi pamene Paulo anali kulemba kalata

imeneyi. Iye akupitirizabe kufotokozera maganizo ake pa bvuto limodzi lomweli mu chaputala 15. Ndipo ife

amene tiri olimba tiyenera kunyamula zofooka za opanda mphamvu ndi kusadzikondweretsa tokha - podya

kapena kuchita chirichonse chomwe chitikondweretsa. Ndi zoona kuti mbale wofooka womangidwa ndi

Page 50: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 50

chikumbumtima akulamulidwa kuti akhale wololera anzake ndi wosaweruza chimodzimodzi mbale wake

wamphamvu uja ndi wosamangika uja yemwe alamulidwanso kuti ataye ufulu wake chifukwa cha mbale wake

wofooka uja. Koma popeza mbale wolimbayo ndiye ali nazo mphamvu, ntchito yaikulu yosunga ndi kusamalira

mtendere ndi kupewa kulakwa iri kwa iyeyo. Thupi lathu lakale la uchimo lodzikonda silifuna kunyamula

ntchito imeneyi. Iyi ndi ntchito yotheka kwa munthu watsopano wopulumutsidwa. Munthu wakale uja ayenera

kupachikidwa ndi Yesu.

Yesu anati, “ngati wina afuna kunditsata ine, iye ayenera kudzikana yekha ndi kunyamula mtanda wake tsiku

ndi tsiku ndi kunditsata ine. Pakuti aliyense wofuna kupulumutsa moyo wake adzautaya, koma yense wotaya

moyo wake chifukwa cha ine adzaupeza – Luka 9:23-24. Mtanda uyimirira moyo wobvuta ndi wopweteka kwa

ife koma wobweza ndi kupulumutsa ena. Moyo wathu wakale umafuna kudzikondweretsa okha, osati

kukondweretsa enawo mwa kutaya ufulu wathu. Ichitu ndi chifukwa chake “kudzikana” liri monga gawo

loyamba pa ulendowu monganso anamchitira Yesu. Aliyense wa ife akondweretse mbale wake kuti

zimuyendere bwino, kuti amlimbikitse akule bwino.

Paulo anasiya ufulu wake wolandira thandizo lochokera kwa abale ampingo wa ku Korinto ndi cholinga choti

ntchito yofalitsa uthenga ikhale ndi mphamvu – 1 Akorinto 9:12. Iye anangokhala “chirichonse kwa anthu

amitundu ulionse,” kusiya zina zomwe iye anali kudzikonda koposa mu nkhani za miyambo yake ndi

chipembedzo kuti akathe kugwirizana bwino ndi gulu liri lonse lomwe iye akapezeke akugwirako ntchito ya

Mulungu – 1 Akorinto 9:19-23. Kuchotsa zizolowezi za miyambo yamakolo ake zomwe zikanakhoza

kulepheretsa uthenga kufika kwa anthu kunali kofunikira kwambiri kwa iye koposa kungochita zomsangalatsa

iye kumbali yake. Paulo anali wokonzeka “kuononga chirichonse chomwe anali nacho ngakhale kudzipereka

iye mwini kuphatikizaponso Akorinto aja mu uzimu – 2 Akorinto 12:15. Iye sanachite zimenezi chifukwa

zimamukondweretsa iye mwini, koma chifukwa anasamalira kwambiri za chipulumutso cha ena koposa zinthu

zina zodzikondweretsa nazo yekha mwini.

Paulo anafotokoza zikhulupiriro zake mu 1 Akorinto 10:31-33:

1 “Chifukwa chake mungakhale mudya, mungakhale mumwa, mungakhale muchita kanthu kena, chitani

zonse kuulemerero wa Mulungu”

2 “Musachimwitse wina aliyense, kaya ndi Myuda, Mhelene kapena mpingo wa Mulungu.”

3 “Ndimayeserera kukondweretsa aliyense m’zonse, chifukwa sindifuna kuti wopindula ndikhale ine koma

unyinjiwo, kuti apulumutsidwe. Ndiponso anati, “mutengere chitsanzo changa monganso ine nditsanzira

Khristu.” 11:1.

Popeza ngakhale Yesu sanadzikondweretsa yekha. Iye sanasiye malo ake abwino ndi ufulu wokhala

m’ulemerero wakumwamba chifukwa pansipano panali pomkomera, koma chifukwa chakuti Iye anali

wamphamvu ife tinali ofooka, ndipo sitikanatha kudzithandiza tokha. Khristu anali “Mulungu m’zonse,” koma

“anadzichepetsa kotheratu nakhala wapansipansi” (RSV: “anadzikhuthula yekha”) – Afilipi 2:5-8. Iye anakhala

kapolo wathu, potiganizira ife, osati yekha. (Ndi chifukwa chake timsirira koposa) Iye anatinyamulira machimo

athu ndi zolemetsa zathu. Ndipo mfundo yaikulu ya ife Akhristu m'moyo ndi makhalidwe athu ikhale yofuna

kufanana ndi Khristu munjira zomwe tichitira ndi anthu onse.

15:4-7: Pakuti zonse zomwe zinalembedwa kale, zinalembedwa ndi cholinga choti ife tiphunzire. Pamenepa

Paulo anangotenga malembo amenewa kuchokera mu Chipangano Chakale. Ife Akhristu sitiri omangidwa ndi

lamulo la m’Chipangano Chakale, koma malembo a m’Chipangano Chakale ali odzala ndi umulungu ndi

mfundo zake. Ife timaphunzira zambiri za Mulungu ndi makhalidwe ake kuchokera mu malemba amenewa.

Ndipo kuti tithe kumvetsa bwino Chipangano Chatsopano tiyenera kukumba kuchokera ku maziko a

Chipangano Chakale.

Mulungu yemwe amapereka chipiriro ndi chilimbikitso (zofunika ziwiri pa umodzi wa abale) akupatseni inu

Mzimu wa umodzi pakati panu pamene muli kutsata Yesu Khristu. Umodzi ndi chinthu cha uzimu monganso

cha chikhulupiriro. Mzimu wa umodzi ndi wofunikira monga kufunikiranso kwa kugwirizana pa zikhulupiriro

za mfundo zazikulu zikulu.

Page 51: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 51

Anthu atha kumabvomerezana pa zikhulupiriro ndi ziphunzitso komabe kumapezeka osiyana maganizo

m'zambiri chifukwa cha mtima wa makani ndi wodzitukumula. Malekano ambiri omwe anthu amati amayamba

chifukwa cha kusamvetsa bwino ziphunzitso ndi zikhulupiriro, ponena zoona amayambira pa uzimu

wodzikondweretsa makani ndi kulimbanira kupambana – “ndikhale wamkulu.” Nkhani ya ziphunzitso ndi

zikhulupiriro imangopangitsa kuti kulekanako kukhale ngati ndi kwabwino. Pakanakhala kuti panali chikondi ndi kudzichepetsa kwa mzimu, ndiye kuti abale akanatha kupeza njira yothetsera bvuto la kukhala ndi

ziphunztso ndi zikhulupiriro zosiyana yomwe ikanatha kuwathandiza kugwirira ntchito pamodzi.

Theka lamachimo omwe asanjidwa “m’ntchito za thupi” – Agalatiya 5:19-21 – nthawi zonse zimapezeka

m'kugawanika kwa mpingo. Kumbali inayi, “chipatso cha Mzimu ‘Woyera” – Agalatiya 5:22-23) ndicho

chenicheni chomwe chimapangitsa kuti abale ndi alongo athe kugwirira ntchito pamodzi ngakhale ali nazo

zofooka zawo aliyense payekha.

Mwa chidziwikirenso, choncho, umodzi mumpingo umadalira kwambiri pa “kufa kwa munthu wakale wa

uchimo, kubadwanso mwa uzimu, moyo watsopano monga momwe zimakhalira ndi momwe timvera

ziphunzitso ndi zikhulupiriro. “Mu chaputala chonena za umodzi” cholembedwa ndi Paulo Aefeso 4, Paulo

watenga nthawi m'mavesi atatu oyamba pofotokoza za mmodzi wa uzimu, ndipo mavesi ena atatu otsatiranawo

Paulo wafotokozera za ziphunzitso ndi zikhulupiriro.

Kuti ndi mtima umodzi ndi mawu amodzi mukalemekeze Mulungu ndi Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu.

Izi sizitanthauza kumangobvomerezana pa mfundo zirizonse zazing’ono; zitanthauza kukhala ‘amodzi’ mwa

Yesu ngakhale pakhale kusiyanako. Milomo yathu iyankhule mosasintha pa zinthu zazikulu zosayenera

kusinthidwa zofunikira. Timalemekeza ndi kutumikira Ambuye mmodzi yemweyo.

Choncho mulandirane wina ndi mnzake, monganso momwe Khristu analandira inu. Kodi Khristu

anakulandirani inu pokha pamene munaona ndi kubvomereza za choonadi chake chonse? Ngati kudali tero,

bwenzi pakali pano mu kudikirabe kuti mulandiridwe. Ayi iye anatifera ife pamene tinali ochimwabe ndipo

anatilandira ife ku thupi lake pamene tinali tiri makanda pa momwe tinali kumvetsera malemba ndi

kudzipereka kwathu. Ngati anatilandira mwa chisomo pamene tinali ochimwa kopambana, ifenso tiyenera

kulandira abale ndi alongo athu omwe ali osachita mwangwiro.

Ndi cholinga chofuna kuti Mulungu atamandidwe. Pamene Akhristu achitana mwa chisomo, Mulungu

adzatamandidwa chifukwa cha magwero a chisomocho pamene dziko liona momwe Akhristu akondanirana

ngakhale pamakhala kupunthwa ndi kulephera, dziko lidzadziwa kuti pali china chake choona ndi chamtengo

wapatali chomwe chikuchitika mumpingo. Pali munthu wina yemwe anadzacheza pa msonkhano wampingo la

Mulungu anati, “Ine ndi kuona ndinso kumva mumtima mwanga kuti kuno kuli mtendere ndi chikondi.”

15:8-13: Khristu wakhala kapolo wa Ayuda – Anabwera monga Myuda natumikira pakati pa Ayuda – m’malo

mwa choonadi cha Mulungu = kuti abweretse uthenga wa chipulumutso ku dziko lonse ndi kutionetsa ife Atate

– kukwaniritsa malonjezano operekedwa kwa makolo oyamba a m’Chipangano chakale kuti mafuko onse

adziko lapansi adzadalitsidwa kudzera mwa obadwa wochokera mwa iwo – Genesis 12:1-3 – kuti amitundu

akalemekeze Mulungu chifukwa cha chifundo chake.

Asanabwere Khristu, Israyeli yekha ndiye anali ndi phangano ndi Mulungu. Amitundu analibe gawo opanda

chiyembekezo – Aefeso 2:11,12. Koma Khristu anafera anthu onse natumiza uthenga wake kwa amitundu ndi

Ayuda omwe. Paulo anagwiritsa ntchito malemba anayi a m’Chipangano Chakale omwe anali kulosera za

chifundo cha Mulungu chomwe analandira nacho amitundu.

Kunakhala kobvuta kwambiri kubweretsa ndi kusunga umodzi pamene mpingo wapangidwa ndi anthu

ochokera ku zikhulupiriro ziwiri zosiyana za miyambo ya makolo, zipembedzo, chikhalidwe, mitundu kapena

kapezedwe kachuma. Nkhani zambiri zazing’ono mumpingo woyamba uja zinalimonso, ndipo izi zinali

chomwecho chifukwa kusiyana kwa zikhulupiriro ndi ziphunzitso kuja kumawatengera ku Mafunso

ochokeranso ku zikhulupiriro zosiyana. Izi zimaoneka kwambiri makamaka pakati pa Ayuda ndi amitundu

omwe anayamba kukhulupirira aja, monga afotokozera mu Aroma 14. Pa kuphunzitsa kwake, Paulo analimbika

kufotokoza cholinga cha Mulungu pa Ayuda ndi amitundu kuti akhale ogwirizana napanga munthu mmodzi

watsopano mwa Khristu. Anthu okhulupirika akukumanabe ndi mabvuto mumpingo amenewa lero, mabvuto

Page 52: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 52

amenewa olephera kuona zinthu mofanana chifukwa chakusiyana m’chikhalidwe, miyambo, zaka, maphunziro,

ndi zina zambiri.

Pali chinthu chimodzi chomwenso tiyenera kuchiona: Paulo akutitsimikizira ndi chiphunzitso choti pa mbale

ndi mbale, tiyenera tidzikhala okonzeka kusiya zathu zina monga nyama pa nthawi yomwe tikuona kuti

tingapunthwitse mbale wina yemwe ali womangidwa ndi chikumbumtima chake. Nthawi zambirinso takhala tikuganiza kuti tiyenera kusiya mchitidwe kapena njira ya kapembezedwe mumpingo kapena ntchito ina ya

mumpingo yomwe ikhumudwitsa mtima wa mbale aliyense mumpingo kuti mwina tingapangitse kuti wina

achimwe.

Izi zimachitika chifukwa cha chikondi cha kwa anthu chilakolako choonadi chofuna kupewa kulakwirana

kapena kupatukana. Chikondi chidzayesetsa kupewa kukhumudwitsa monga momwe chingathere. Komatu

tiyenera kusamalira kwambiri pogwiritsa ntchito mfundo za Paulozi pa nkhani za pa mpingo; sizikhala

zosabvuta monga momwe zikhalira pakati pa aliyense payekha, m'modzimodzi.

Mwa chitsanzo, ngati mpingo ukuganizira za ntchito yofalitsa uthenga ndi kutembenuza mizimu 50, ndipo

pafupifupi mpingo wonse ukukhulupirira kuti ntchitoyo ikugwirizana ndi malemba ndipo ndi yokhoza, kodi

mpingo usiye kugwira ntchitoyi chifukwa m’[bale mmodzi kapena akukhulupirira kuti ntchitoyi ikulakwira

mawu a Mulungu? Kodi nkwabwino kupunthwitsa osakhulupirira 50 (kuwalepheretsa kulandira ndi

kukhulupirira uthenga wabwino) ndi cholinga chofuna kupewa kukhumudwitsa mmodzi kapena awiri

mumpingo? Kodi ndi chifuniro cha Mulungu kuti chikumbumtima chofunikira cha abale ofooka

m’chikhulupiriro chidzingololedwa kulamulira njira zomwe mpingo udzigwirira ntchito zake? Kodi kusiya

ntchito yofunikira kwambiri mumpingo kukhala kosabvuta monga momwe zikhalira ndi kusiya kudya nyama?

Ngati mu Aroma 14 timaphunzira kuti mbale wolimba asachite china chirichonse chomwe chingapunthwitse

mbale wofooka, kodi pameneponso sakuphunzitsa mwa chimvekere kuti mbale wofookayo

asaweruze/asadzudzule iwo omwe chikumbumtima chawo chiwapatsa ufulu? Kodi kupembeza pa mpingo

kutanthauza kuti tibvomereze zonse zomwe mpingowo umachita? Kodi Aroma 14 sitiphunzira kuti tingathe

kugwira ntchito ndi mpingo, koma pewani kuchita nokha chirichonse chomwe chikumbumtima chanu

chikutsutsani, ndipo siyirani kuweruza pa zinthu zina kwa Mulungu?

Nkhani zina zazing’ono zimakhudza zochitika pa kupemphera mwangwirizano. Chikumbumtima cha wina

sichimlola kukhala nawo pa chipembedzo chosonkhana m'nyumba imodzi monga zikhalira masiku ano.

Pamenepa munthuyu angathe kuchoka pa mpingo umodzi ndi kukayamba kusonkhana kumpingo wina komwe

mapembezedwe ali obvomerezedwa ndi chikumbumtima chake. Komabe ngakhale ziri chomwechi, mipingo

iwiri ija itha kutsatira moyo wololerana wa mu Aroma 14 pakati pawo, kugwirizana mu zinthu zomwe afanana

m’maganizo ndi kusiyira zina zonsezo kwa Mulungu kuti aweruze. Mipingo isatayenso Chiyanjano chawo chifukwa cha nkhani zazing’ono zoti angasankhe kukambirana kapena kungosiyira Mulungu kuti aweruze

koposa Mkhristu payekha payekha/m'modzimodzi.

Mafunso Othandiza Pokambirana:

1. Kodi malemba amaphunzitsa zotani pakulimbana kosatha chifukwa cha nkhani zazing’ono za

chipembedzo? 2 Timoteo 2:14; Tito 3:9-12.

2. Tchulani zina za zitsanzo za masiku ano za “nkhani zazing’ono” zokhudza khalidwe la Mkhristu? Ntchito

ya mpingo ndi mapembedzedwe?

3. Kodi tidzalolera motani ngati wina apempha kumasonkhana nafe komanso nafuna kulemekeza Sabata

(Loweruka) pa iye yekha, kwinaku namasunga ndi kulemekeza tsiku la Ambuye Lamulungu, monganso

kunalili ndi Aroma aja?

4. Taganizirani mfundo, nkhani kapena chinthu china chirichonse chomwe abale anu a Chikhristu

amakhulupirira kuti ndi chobvomerezeka koma inu mumachikaikira?

5. Taganiziraninso china chirichonse chomwe mukhulupirira koma ena a Akhristu anzanu amakhulupirira kuti

ndi cholakwika?

Page 53: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 53

6. Kodi ndi chifukwa chiyani nthawi zambiri kumakhala kobvuta kwa basi kwa munthu yemwe amaumirira

zimene anazidziwa zokhazo, wokhala womangiririka pa chikumbumtima chake kuona nkhani yaing’ono

yoti mutha kukambirana ndi kusankha maganizo amodzi, ngati yoyenera kutero?

7. Nanga ndi zinthu ziti zomwe mumaziika pa mndandanda wanu wa zenizeni zomwe mumakhulupirira pa

Chikhristu chanu, zomwe kaya zitani simungalole kuzisintha mokambirana? Kodi ndi ziphunzitso ndi zikhulupiriro ziti zomwe tiyenera kugwirizana nazo pasanakhale umodzi? Kodi kapena nkhani yake ndi

yomwe iri pa Aefeso 4:4-6.

8. Kodi nthawi zina timatenga nkhani zazing’ono kukhala zofunikira koposa “Chiyero,” mtendere, ndi

chimwemwe mwa Mzimu Woyera?” Nanga tingapewe bwanji moyo umenewu?

9. Nanga tingachite chiyani kuti zitheke kumvera chiphunzitso cha Paulo chakulolerana mu Aroma 14 ndipo

panthawi yomweyo kusamalira ndi kusunga mzimu womvera malangizo onse a Mulungu aang’ono ndi

aakulu omwe? Kodi kungatheke kukhala wosalolera kusiya zomwe ukhulupirira iwe mwa wekha ndi

kukhala wololera za ena panthawi imodzi?

10. Ndi chiyani chomwe munayamba mwa chisiyapo m’nthawi ina yake pofuna kupewa kulakwira maganizo a

wina?

11. Kodi zimatheka kukhala kumbali yolondola “pankhani yomwe pali maganizo awiri” komabe ndi kukhala

woweruzidwa ndi Mulungu chifukwa akuonetsa kugawanitsa malinga ndi njira yomwe akutengera

nkhaniyo?

12. Nchifukwa chiyani umodzi uli wofunika? Yohane 17:20,21; 13:35.

MBALI ZOBVUTA POTANTHAUZIRA MALEMBA

Mawu oyamba: Matanthauzidwe a gulu lija lakubwezeretsa:

1) Ponena za chikhulupiriro ndi machitidwe athu onse, malembo ndiwo atitsogolera ndi kutilamulira.

2) Baibulo limalamulira popereka lamulo pomwepo, chitsanzo chobvomerezeka ndi maganizo

oyenera.

3) Pamene Baibulo linena, ifenso timanena ndipo pamene Baibulo likhala chete ifenso tikhala chete.

Ndi kukhulupirira kuti maganizo onsewa ndi omveka ndi obvomerezeka ndiponso kuti tonse tingathe

kugwirizana nawo. Komatu Sali osabvuta kuwagwiritsa ntchito m’machitidwe athu. Tamvani ndemanga ya

katwiri wina wotchedwa Dr. Bill Humble:

Nkosabvuta kungonena mfundo ya gulu lobwezeretsa lija yoti – mpingo uliwonse mumbadwo

uliwonse ukhale pafupifupi wofanana ndi mpingo wa m’Chipangano Chatsopano. Ndi chinthu

chobvuta kuti tizindikire ndi kuganizira zomwe Chipangano Chatsopano chifuna mu nthawi iri

yonse pa yokha. Mpingo uyenera kumafunsa, kodi ndi ziti zomwe ziri zoyenereka kutsatidwa

malinga ndi dongosolo la Chipangano Chatsopano? Nanga ndi ziti zomwe tingazichotse popeza

zinangokhala monga gawo la chikhalidwe ndi miyambo ya nthawi zakale ndipo kuti ndi

zosamangiririka ku mpingo mu m’badwo uliwonse? Iri ndi bvuto lokhudzana ndi

katanthauziridwe ka Baibulo ….. bvuto la njira ya kamasuliridwe ka malemba ndipo mayankho

ake sakhala okhweka nthawi zonse.

Ntchito yobwezeretsa inagawanikana chifukwa chabvuto lakamasuliridwe kamalembo. Phunziroli likhala

likuunika Madera a ena a mabvuto amenewa.

1. Kodi kukhala chete kwa malemba kumatiletsa kapena kumatiloleza?

A. Mu nthawi zakusintha ndi kukonzanso zinthu zija Martin Luther anakhulupirira kuti chirichonse

Page 54: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 54

chomwe sichinaletsedwa mwatchutchutchu m’malemba chiri chololedwa, pamene Ulrich Zwingli

anakhulupirira kuti chirichonse chomwe sichilamulidwa mwatchutchutchu nchosaloledwa. Munthawi

yakubwezeretsa, Barton W. Stone anabvomera kunyema ndikumwa pa mgonero pamodzi ndi

osabatizidwa mobizidwa chifukwa sanapeza lemba lenileni loletsa zimenezi. Koma Alexander

Campbell anatsutsa zimenezi, ponena kuti panalibe lemba lolamulira machitidwe amenewa Palinso

kusiyana kwa maganizo ngati komweku pokhudza za kugwiritsa ntchito zida poyimba nyimbo.

B. Zitsanzo za zochita zina zomwe gulu limodzi kapena gawo lina la anthu obwezeretsa aja anatsutsa

chifukwa sanazipeza m’malemba: amasiye Akhristu, makoleji Achikhristu, mgwirizano wodzera mu

mpingo umodzi wothandizira, mabungwe a amishinale, zikho zambiri pa mgonero wa Ambuye,

thumba la chuma cha mpingo, nyumba za mpingo, mabuku a nyimbo, mgonero wa madzulo

(wachiwiri) alembi ampingo, alaliki oyang’anira za achinyamata, alaliki a uthenga wabwino,

misonkhano ya achinyamata, anthu oyendetsa ntchito, makalasi ochitidwa m’nthawi zofanana, malaudi

sipikala, mabukhu ophunzitsira Baibulo, maholo achitira mafeloshipi, ndi zina zotero.

C. Ambiri akhulupirira kuti pamene Mulungu afotokoza mwapadera njira yochitira chinthu china, ichi

chitanthauza kuti pasachitikenso njira za mtundu winanso osakhala umenewu.

Zitsanzo:

1) Ubatizo wobiza sulola wina monga wotsira madzi pamutu, kapena kungowaza.

2) Mnjale, mtengo womwe anapangira chombo cha Nowa osati mkungudza kapena mitengo ina –

Genesis 6.

3) Moto woyera wokha pa guwa, osati miyoyo ina wamba – Levitiko 10.

4) Mkate ndi chipatso cha mpesas pa mgonero wa Ambuye osati chakudya china chirichonse kapena

chakumwa.

5) Akulu pa mpingo uliwonse osati utsogoleri wamtundu wosiyana ndi umenewu.

6) Mapembedzedwe a padera a m’Chipangano Chatsopano osatinso monga ena ali onsewo.

Ngati kukhale chete kwa malemba sikutiletsa, ndiye kuti machitidwe ena onse achilendo

adzakhalanso obvomerezedwa. Komanso palibe yemwe akhulupirira kuti machitidwe onse omwe

sitilamulidwa mwapadera kuchita ndi oletsedwa. Ambiri a ife timagwiritsa ntchito timakapu ting’onoting’ono tayekha tayekha pa mgonero ngakhale Khristu anagwiritsa ntchito chikho chimodzi.

Ambiri timakhulupirira kuti zothandizira zina kuti lamulo lina likwaniritsidwe ngakhale sizinachite

kutchulidwa kapena kufotokozedwa m’malemba, zimalamulidwa ndi chilamulo chongoganizira, koma

pokhapokhapo ngati chachita kuletsedwa mwapadera penapake.

Komanso, palibe yemwe amakhulupirira kuti machitidwe alionse omwe sanaletsedwe mwa dongosolo

ndi ololedwa. Mipingo yomwe imangwiritsa ntchito zida mu nyimbo zawo imatsutsa ponena kuti zidazi

zimaloledwa m’Chipembedzo chifukwa siziletsedwa mwapadera; koma amakana ubatizo wowaza

madzi pamutu ngakhale siziletsedwa mwapadera.

D. Dr. J.D. Thomas anapereka maganizo oti, “kukhala chete pamene malemba akhale chete” si mfundo

yaikulu ayi, koma amagwiritsidwa ntchito m’malo okhawo omwe malemba afuna kuti machitidwe

kapena m'chitidwewo usachitike. Naye Clinton Lockhart analemba kuti, “kutsimikizira pa choonadi

kumachotsadi chomwe chikutsutsana nacho basi.

2 Kodi ndi zitsanzo ziti zomwe zatimanga lero?

A. Pamene tiona atumwi kapena mpingo woyamba uja ukuchita kanthu, mwina uwu ungakhale umboni

wa atumwiwo pa lamulo lomwe iwo analamulidwa nalo ngakhale kuti lamulolo silifotokozedwa bwino

kwa ife m’malemba. Chitsanzo:

Page 55: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 55

1) Tiyenera kumvera Mulungu koposa anthu – Machitidwe 5:28,29.

2) Woyang’anira wa ndende yaku Filipi anatembenuka nthawi yomweyo – Machitidwe 16:33.

3) Paulo anamtumiza Onesimo, kapolo wathawa uja Filimoni mbuye wake.

4) Ambuye anawaonjezera tsiku ndi tsiku iwo omwe anali kupulumutsidwa – Machitidwe 2:47.

5) Paulo anakhala “chili chonse kwa anthu onsewo”, ndi cholinga chofuna kuti afalitse bwino

uthenga – 1 Akorinto 9:19-22.

6) Antchito ampingo anali kudzodzedwa “powaika manja” – Machitidwe 6:1-6.

7) Ophunzira oyamba anali kutchedwa Akhristu – Machitidwe 11:26.

8) Anthu omwe ubatizo wawo woyamba sanali watanthauzo anabatizidwanso – Machitidwe 19:1-6.

B. Koma ndi anthu ochepa omwe amakhulupirira kuti chitsanzo chirichonse mumpingo woyamba

chipereka lamulo lomwe tiyenera kulitsata m’masiku ano.

1) Alaliki ankapita awiriawiri – Luka 10:1-4.

2) Paulo anafotokozera chiphunzitso ndi ndakatulo ya osapembedza – Machitidwe 17:28.

3) Paulo analalika mu kachisi wa Ayuda – Machitidwe 13; 14:1; 17:1,2.

4) Analalika miyezi itatu m'kachisi mmodzi – Machitidwe 19:8.

5) Anali kuphunzitsa tsiku ndi tsiku pa “sukulu ya ku Turano” – Machitidwe 19:9,10.

6) Anasonkhana pa mgonero wa Ambuye usiku m’chipinda chapamwamba – Luka 22:7-20;

Machitidwe 20:7,8.

7) Paulo analalika mpaka usiku ndi kupitiriraponso – Machitidwe 20:7,11.

8) Mgonero wa Ambuye unachitika pogwiritsa ntchito chikho chimodzi – Mateyu 26:27.

9) Mpingo wa ku Yerusalemu unasankha atumiki 7 kuti athandize pa chakudya – Machitidwe 6:1-6.

10) Nthawi zambiri Paulo ankayenda pa ngalawa pokalalika.

C. Kuganizira chitsanzo chomwe chiri chomangirira inali ntchito yaikulu m’nthawi yobwezeretsa.

Zitsanzo:

1) Iwo omwe anatsutsa anaunikira pempho la alaliki ku chitsanzo cha Paulo chosalalikira kumalo

komwe Khristu akudziwidwa kale – Aroma 15:20.

2) Omwe amatsutsa kugwirira ntchito kwa mipingo pamodzi amati mumpingo woyamba uja,

chithandizo chimachokera kuchokera ku mpingo umodzi kupita ku winawo pa nthawi zamabvuto

zokha ndiponso kuchokera ku mpingo wopeza bwino kupita kumpingo wosauka.

3) Gawo lina la zitsanzo zomwe chithandizo chinali kupita kwa a mishonale osadzera ku mpingo

womwe unali kumthandiza – Afilipi 4:15,16; 2 Akorinto 11:8.

4) Omwe amatsutsa za Sunday sukulu amati chitsanzo chomwe timaona cha maphunziro a gulu ndi

chokhacho chomwe timaona mpingo wonse uli pamodzi, ndipo amati chimenechi ndicho

chimaletsa malasi otsatana – Machitidwe 11:26; 1 Akorinto 14:23.

Page 56: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 56

5) Dr. J.D. Thomas amapereka maganizo oti “pokhapokhapo ngati pali chisonyezo choonadi ndi

chomveka bwino choti machitidwewa anali oyenera kuchitidwa, [ndi Akhristu oyamba, ndi

ulamuliro wa atumwi]. Ifenso tidzachita koma mwa ufulu wosankha m’masiku ano. (mawu ali

m'mikutirowo ndi anga).

3 Ndi maganizo ati omwe ndi ofunikira?

A. Malembo ndi malamulo ena amphamvu opezeka, ngakhale sanafotokozeredwe mwatchutchutchu,

akhoza kungoganiziridwa mwa chilungamo kuchokera ku zonenedwa ndi mfundo zina. Zitsanzo:

1) Kaini ndi Abele anauzidwa mtundu wansembe yomwe Mulungu anafuna, - Genesis 4:3-5; Ahebri

11:4.

2) “Kulalikira Yesu” kunaphatikizana ndi kulalikira ubatizo – Machitidwe 8:36-39.

3) Ubatizo siwamakanda ayi – Marko 16:16, Machitidwe 2:38.

4) Kusiyana pakati pa mwamuna ndi mkazi chifukwa cha chigololo kumaloledwa kwa mwamuna

ngakhalenso mkazi – Mateyu 19:9; Marko 10:11,12.

5) Mpingo uliwonse wa pamalo udzikhala woima paokha monganso iriri mipingo ina yonse –

Machitidwe 14:23; Tito 1:5.

6) Kulibenso Atumwi padziko lapansi masiku ano – Machitidwe 1:21,22.

7) Munthu wathupi la uchimo sikuti ndiwongotaikiratu – Luka 8:15.

8) Oyang’anira ayenera ayambe ayesedwa ndi kubvomerezedwa asanaikidwe manja – 1 Timoteo

3:10.

9) Anthu ofuna ntchito ya oyang’anira ayenera asankhidwe ndi mpingo – Machitidwe 6:1-6.

B. Komabe pali kusiyana pakati pa ganizo lofunikira, ndi losatsimikizika kapena looneka ngati ndi loona.

1) Poti Ayuda patsiku la Pentekoste (Machitidwe 2) anauzidwa kuti alape nabatizidwe, ndi ganizo

lofunika kuti anthu amenewa anali achikulire kuti anatha kukhulupirira ndi kubatizidwa.

2) Likuoneka ngati ganizo loona koma losatsimikizika loti popeza anthu analipo zikwi zitatu ndiye

kuti mmaiwe ndi m'malo osamba anthu mu mzinda wa Yerusalemu.

3) Likuoneka kuti ndi ganizo loona ndipo lingatheke loti atumwi onse anagwira ntchito yobatiza

anthu zikwi zitatu aja mothandizana.

C. Nthawi zambiri pakhala pali bvuto pofuna kumvana ngati ganizo la anthu pa mfundo ina ndi lofunika

kapena losatsimikizika kapena ndi lotheka. Zitsanzo:

1) Mpingo wa ku Trowa unasonkhana pa tsiku loyamba la Sabata kunyema mkate – Machitidwe

20:7. Atsogoleri antchito yobwezeretsa anali naonso maganizo amenewa oti mipingo yonse,

kulikonse m’Chipangano Chatsopano amanyema lamulungu lirilonse. Komabe ena amafunsa

ngati limeneli liri ganizo lofunikira potengera pa ndime yake yokhayi.

2) Ganizo linanso likutengedwa mu 1 Timoteo 3:2, loti mwamuna mmodzi sangakhale mkulu

pamalo. Koma enanso amatsutsa zimenezi.

Page 57: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 57

3) Mkate womwe unkagwiritsidwa ntchito pa Pasika unali wopanda chotupitsira. Yesu

anagwiritsa ntchito mkate wapa Pasika pamene anali kuyambitsa mgonero wa Ambuye. Pakhala ganizo loti mkate wa pamgonero wa Ambuye ueyenera udzikhala wopanda

chotupitsa.

D. Tomasi Campbell, m’chikalata cha dongosolo lake analemba:

Ngakhale zoganizira chabe ndi zochotsedwa ku malemba, ngati zaganiziridwa

mwabwinoko, zingathe kumatchulidwa kuti ziphunzitso za mau opatulika a Mulungu,

koma kodi sizikumangiriridwa mmaganizo a Akhristu kopitirira. Komwe akanayenera

kuunika ndi kulumikiza bwino mgwirizano wake, ndipo mwaumboni natsimikizira kuti

ziri chonchodi; popeza chikhulupiriro chawo chisasamire pa nzeru za anthu, koma mu

mphamvu ndi ulamuliro wa Mulungu. Choncho palibe kuchotsa zinthu kwa mtundu

umenewu kungatengedwe monga choyanjanitsa, koma zimakhala ku zotsatira ndi

kumangirika kwa mpingo.

Iye analankhula zimenezi chifukwa anaona kuti panali kutsamiranso pa maganizo a munthu

potenga maganizo a choonadi cha m’malemba.

4. Kusiyanitsa pakati pa zofunikiradi ndi zongochitika.

Ngakhale chitsanzo cha mpingo woyamba uja chingakhale molingana ndi malamulo a atumwi aja, zichitika zawo zina zitha kungokhala monga zochitika chabe zomwe ziribe gawo lirilonse

ndi chifuniro cha Mulungu mu mpingo wake. Mwachitsanzo, cholinga, kutanthauza ndi magawo ena a mgonero wa Ambuye monga tionera mmalemba akuonetsa chifuniro cha

Mulungu kwa ife lero, koma malo kapena nthawi yochitira mgonerowo (m’chipinda chapamwamba usiku) ndi zinthu zoti zinangochitika basi.

5. Kusiyanitsa zochitika mdziko lathu kapena dera lathu, zokhala kanthawi kochepa ndinso

zachikhalidwe, ndi ziphunzitso zapadziko lonse ndi magwiritsidwe ntchito achikhalire.

A. Malamulo ngakhale zitsanzo zina zinaoneka ngati tanthauzo lake ndi cholinga chake kwa

kanthawi kochepa ndi malo ake. Zitsanzo:

1) Akazi kubveka mitu yawo popemphera – 1 Akorinto 11.

2) Kupsopsonana kopatulika – 1 Akorinto 16:20

3) Kusamba mmapazi – Yohane 13; 1 Timoteo 5:10.

4) Kupewa banja chifukwa cha masutso alinkudza – 1 Akorinto 7:25-31.

Izi siziri zotimanga ife lero ponena zoona, ngakhale kuti malamulowo akutero. Ena

samasiyanitsa ndipo akadagwiritsidwabe ntchito malamulowa lero.

B. Anthu a mgulu lobwezeretsa lija ndinso ena omwe sanali mgululi anatsutsa kuti mfundo ya m’Chipangano Chatsopano yoletsa akazi kutsogolera mmisonkhano yachipembedzo ndi

ntchito za mpingo linali monga mwambo ndi chikhalidwe komanso malinga ndi nthawiyo,

osati ndiyogwira ntchito padziko lonse mpaka kale ayi. Koma Paulo watengera malamulo ake

pa chilengedwe ndi kuchimwqa kwa munthu – 1 Akorinto 14:34-35; 1 Timoteo2:11-15.

C. Payenera kukhala kuganizira mozama bwino kuti tithe kusiyanitsa zofunikira kwambiri, ndi

Page 58: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 58

zongochitika chabe ndi zachikhalidwe, komanso ndi zogwira ntchito konsekonse.

6. Kusiyanitsa zoyambirira ndi zopitirira nazo pa chifuniro cha Mulungu.

Malamulo ndi zitsanzo zina zimakhazikika ndi kukhuza kwambiri ku nthawi zoyambirira ndi

zokhazikitsa mpingo, osati ku nthawi zonse. Zitsanzo: “Zizindikiro za mtumwi” – 2 Akorinto 12:12; udindo wa atumwi; Bungwe la ku Yerusalemu – Machitidwe 15.

7. Kusiyanitsa mawu okuluwika ndi oona.

A. Baibulo liri ndi mau ena omwe analembedwa kuti amveke monga momwe aliri mosabvuta

ndipo ena akamveke mokuluwika. Timasokoneza zomwe Baibulo litanthauza pamene titenga

mau olembedwa moona ngati mkuluwiko ndi olembedwa monga mkuluwiko ngati oona.

B. Mafunso ena okhudza chipembedzo omwe amafunsidwa pa nkhani imeneyi ndi aja a za

ulamuliro wa zaka chikwi (mileniamu) wa Khristu (Chibvumbulutso 20) ndinso zogwiritsa

ntchito zikho zambiri pamgonero wa Ambuye.

C. Maganizo othandiza kuti tizindikire mau okuluwika (olembedwa ndi J.R. Duncan):

1) Momwe nkhaniyo ikumvekera.

2) Ngati zonenedwazo zinena zachinthu choti sichingatheke mwachilengedwe.

3) Ngati tanthauzo lenileni la nkhaniyo litsutsana ndi malemba ena.

4) Ngati tanthauzo lake lenileni lidzafuna machitidwe omwe ali olakwika kapena oletsa

zinthu zoona.

5) Ngati tiuzidwa kuti ndi mau ophiphiritsa.

6) Ngati zotsimikizika ndi zokhazikika zilowa m’malo osatsimikizika ndi osakhazikika.

7) Ngati zinenedwa mongoseweretsa.

8) Kuona wekha momwe zinthu ziriri panthawiyo ndi nkhaniyo.

9) Malamulo amaperekedwa mmau omveka bwino.

7. Kodi zoyankhula za Yesu mnthawi za utumiki wake zikutilamula ife mumpingo lero?

A. Anthu ena amati ziphunzitso za Yesu pankhani za kulekana m’banja ndi kukwatiranso ndinso zomwe anayankhula pa chiphunzitso cha paphiri zinali za kwa mbadwo wapansi pa chilamulo

cha Mose omwe unatha panthawi yomwe Yesu anafa, ndipo sizigwiranso ntchito mumpingo lero.

B. Pamene zina za ziphunzitso za Yesu zinkagwirizana ndi momwe Ayuda ankamverera

chilamulo cha Mose (pita ukadzionetsere kwa ansembe; “Alembi ndi Afarisi amakhala

pampando wa Mose; choncho mverani ndikuchita zomwe akuuzani”), zambiri za ziphunztso

zakezi ndi za ufumu/mpingo ndipo ndi zokonzedwera mpingowo. Chiphunzitso cha paphiri

chinena za chiyero cha ufumu – Mateyu 5:20ff. Pankhani ya banja kulekana ndi kukwatiranso,

Yesu akusiyanitsa chiphunzitso chake ndi cha Mose – Mateyu 19:3-9.

Page 59: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 59

Mitu yofunika potsiriza:

1. Ambiri akufufuza matanthauzo ena atsopano pakati pa mipingo yonse yomwe iri mgawo

lobwezeretsa lija. Iwo amadzudzula kusagwiritsa bwino ntchito ndinso kusiyana maganizo mugululi pamomwe anamvera ndikutanthauzira machitidwe akale aja (malamulo, zitsanzo,

kuganizira kofunika). “Mamasuliridwe amasiku ano” amafunika kuti ife tisiye kufufuza za zoonadi za nkhaniyo kuchokera kunkhani yomwe siikhudza nkhaniyo ndipo tiganizire

mosamala zankhaniyo, mbiri ya nkhaniyo yalembedwera. Alangizi abwino ndinso omasulira

malemba okhwima akhala akulimbikitsa zimenezi. Mamasuliridwe atsopano amakana zitsanzo

ndi zoganizira kuti zisakhale zamphamvu yolamulira ndipo amangobvomereza malamulo

okhawo olembedwa mosakuluwika ndi mwwachindunji. Izi zakhala chomwechi chifukwa cha

mabvuto omwe takomana nawo pofuna kuzindikira kuti kodi ndi zitsanzo ziti kapena

zoganizira ziti zomwe ziri zomangirira. Koma mabvuto onsewa akatha, anthu adzakhalabe

akuyang’ana pa zotsanzo ndi zoganizira kuti apeze muuni wowaunikira kuti mpingo

ukhulupirire ndi kuchita ziti.

2. Zolimbana zathu zambiri za momwe tingagwirire ntchito ya mpingo zimabwera chifukwa

chokakamira dongosolo kapena machitidwe, zomwe zotsatira zake zimayamba kulamulidwa

ndi moyo wopendekera ku chilamulo. Mpingo woyamba womwe unachita potsatira utsogoleri

ndi malangizo a atumwi sunayenere kukhala chitsanzo chathu, koma timaona dongosolo la kachitidwe mmalo monse momwe Mulungu analibe nawo dongosololo. Timachita izi

chifukwa cha khalidwe lathu lomwelija lopendekera pa malamulo lofuna kukhala odziwitsitsa. Pamene tisiya moyo ndi khalidwe lopendekera ku malamulo ndikuyamba kumvera pansi pa

chisomo, pamenepo tidzatha kulemekeza chitsanzo cha m’Chipangano Chatsopano popanda kupitirira ndi kumasulira moonjezera.

3. Malembo amazindikira zambiri zomwe ndi mfundo zazing’ono zomwe zimatchedwa “mfundo,

kapena nkhani zazing’ono zoti titha kusiyana pa momwe tiziganizira” – Aroma 14,15 – nkhani

zomwe mpata umakhalapo anthu atha mwachilungamo, ndimokhulupirika kulolerana kusiyana

maganizo pakumasulira kwake. Tiyenera kulemekeza chikumbumtima chathu pazomwe ife eni

tichita, koma Baibulo litiphunzitsa kuti tingathe ndipo tiyenera kugwira ntchito pamodzi ndi

iwo omwe maganizo awo ndi athu asiyana kwambiri pa zinthu zina zazing’ono. Koma pali

mfundo za choonadi zina zazikulu za uthenga wabwino zomwe tiyenera kugwirizana kuti

tikhale amodzi (onani ndikuwerenga Aefeso 4:1-6). Mfundo zazikulu zachoonadi zimenezi

zalembedwa momveka bwino m’Baibulo. Choncho pamene tiri ofunikira kulimbikirabe

ntchito yofufuza zomwe Mulungu atilamulira m’malemba, sikuti tidzipeza mayankho onse

kapena kugwirizana pa mfundo zofunikira zazikulu kuti tithe kugwira ntchito pamodzi.

--B. Shelburne

South Texas Leader’ Meeting

September 30, 1989

Kusiyanitsa Malemba ndi Miyambo M’chipembedzo.

Mawu oyamba: Werengani Marko 7:1-13. Ayuda anadzipangira miyambo yaumunthu yambiri naipanga kukhala yamphamvu ndi ulamuliro kotero kuti anaika pambali chilamulo cha Mulungu

chifukwa cha miyambo yaoyo. Kodi nafenso tingachite zimenezi? Mipatuko yambiri mntchito yobwezeretsa ija inabweramo chifukwa cholemekeza kwambiri miyambo ndi kuitenga ngati yofunika

kwambiri kuposa malemba.

Malemba ndi mau a Mulungu. Sitingathe kumasula chomwe iwo amanga mwaqchimvekere. Miyambo

ndi mau a munthu. Imapangidwa ndi nzeru za munthu ndi zikhalidwe za makolo zosiyirana. Tiri ndi

ufulu wosintha miyambo ndi zizolowezizi.

Page 60: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 60

1. Kodi miyambo imayamba bwanji? Nanga imachokera kuti? Inayamba kudzera m’njira ziwiri:

A Pamene Mulungu wapereka lamulo lomwe sanafotokoze bwino momwe lamulolo

B ligwirira ntchito, iye watisiyira mwai woti tisankhe njira yabwino yogwirizana ndi nthawi

yathu komanso momwe zinthu ziriri panthawiyo.

1) Izi ziyenera kutero popeza uthenga waperekedwa ku mitundu yosiyanasiyana mzaka

mazana-mazana.

a) Ife timagwiritsa ntchito njira zosiyana siyana zofalitsira uthenga mosiyana ndi

mpingo woyamba uja.

b) Timasonkhana mmalo osiyanasiyana ko

c) Machitidwe ena a kapembedzedwe kathu ndi osiyana kwambiri ndi ampingo

woyamba uja.

2) Pamene malembo safotokozera bwinobwino njira ya machitidwe ake, ife timayang’ana

pa zofunikira za munthawi zathu zino ndi malo athu ndinso poganizira zomwe zingachitikedi kuchokera mmalemba, ndipo kenako timasankha njira yoyenera ndi

yabwino. Zizolowezi ndi zikhalidwe zimenezi, kaya njira zimenezi zoyambika kalezi, ndizo zimapanga miyambo.

3) Miyambo imatha kuyambanso posonkhanitsa nzeru zochokera kwa atsogoleri athu

omwe timawalemekeza ndinso anzeru ena amakedzana.

4) Sinkhani zonse zopezeka mmalemba zimamveka bwino. Mu zomwe sizimveka

bwinozo, mwai ulipo wololera mokhulupirika kusiyana kwa maganizo ndi

kutanthauzira. Kutanthauzira kwa mfundozi ndikosiyirana kuchokera ku mbadwo

umodzi kupita ku mbadwo winawo, ndipo sitimaphunziranso nkhanzo kwa ife tokha.

5) Malembo satchula pachokha mwachimodzichimodzi cha zonse zomwe tikumana nazo

munthawi zathu zalero (monga mankhwala ozunguza bongo). Tiyenera kumaona zoona

zenizeni za malemba pa zinthu zimenezi ndikuzigwiritsa ntchito pa zochitika ndi

zobvuta moyo wathu wa masiku amakono. Aphunzitsi athu ndi atsogoleri athu

amagwiritsa ntchito njira imeneyi poweruza zina ndi zina ndipo nafenso timasiyira ena.

Zonse zosonkhanitsidwa kuchokera ku maweruzo akalewo zimakhala miyambo yathu

kapena zizolowezi zathu ndi ziphunzitso zathu mumpingo. (kumbukirani, kuti

sitikunena za zinthu zolembedwa momveka bwino m’Baibulo, koma za maganizo athupi la munthu lopanda ungwiro.)

6) Izi zingathandize kupeza chifukwa chomwe gulu lathu lagawanika.

a. Chipangano Chatsopano chinalibe cholinga choti chikhale monga bukhu

la dongosolo la malamulo monga chinali Chipangano Chakale (ngakhale tiyenera kulemekeza malamulo omwe chitipatsa)

b. Kwakukulu Chipangano Chatsopano chiri ndi mfundo zazikulu za

choonadi zomwe zingagwiritsidwe ntchito pa bvuto liri lonse mu

chikhalidwe chiri chonse. Ndipo Mulungu ayembekezera kuti ife tikule

monga Khristu mu umunthu wathu kuti tithe mwaumunthu wathu

kuchita zinthu

Page 61: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 61

zobvomerezeka – Yeremiya 31:33; Aroma 13:10.

c. Koma thupi lathu lauchimo limakonda malamulo ooneka olembedwa

mofotokozedwa bwino monga a m’Chipangano Chakale aja.

1. Kuti titsimikizire zaungwiro wathu poona momwe tichitira bwino potsatira malamulo ena.

2. Kuti tisamaganizire ndikugwiritsa ntchito malamulo.

3. Kuti tisasinthike mkatimo.

d. Choncho tayesetsa kuika “mosamveka bwinomo” m’Chipangano

Chatsopano pongoganizira, kuchotsera, kuika maganizo athu

ndikumasulira malingana ndi zomwe tikuyembekezera. Timafuna

lamulo lapa chirichonse. Dongosolo lirimo m’Chipangano Chakale

lakayendetsedwe kampingo ndi ntchito zake, koma nthawi zina tatenga

ndikugwiritsa ntchito moyo wopendekera pa dongosolo lodziwika,

ndikufuna dongosolo la malamulo ena oti m’Chipangano Chakale

mulibe ata. Ndipo kuyambira pamene maganizo ndi nzeru zina za munthu zinayamba kugwiritsidwa ntchito kuti zitseke mmipata momwe

simumamveka bwino ndikuti apeze dongosolo lakayendetsedwe ka ntchito zina, nthawi zonse sitinakhala ndi maganizo ofanana mu

mchitidwe umenewu. Choncho tangokhala ogawikana mtimagulu, kagulu kali konse ndikumaganiza kuti ndikokhako komwe kayendetsa

ntchito zampingo mogwirizana ndi dongosolo la malemba.

e. Tikanatha kupewa kugawikanaku ngati tikanazindikira kuti kutsutsana

kwathu kulipo chifukwa cha mbali ya maganizo athu ndikutanthauzira

kwa umunthu wathu, osati chifukwa cha malemba omveka bwino.

Ndiyenera kumvera chikumbumtima changa, koma ndisamangirire

chikumbumtima changacho kwa ena ngati njira yoyesera Chiyanjano

chathu. Makolo athu am’ntchito yobwezeretsa ija anati,”

mchikhulupiriro,k umodzi; mmaganizo, ufulu; mzinthu zonse,

chikondi.”

2. Ndikofunikira kudziwa ndiikumvetsa kuti mmitundu yonse ya miyambo muli maganizo ena a

umunthu.

A. Miyambo ingathe kufaniziridwa ndi mau a Mulungu, koma ndi maganizo a munthu. (Miyambo ina ingathe kukhala ndi maziko ake ochokera ku malemba kuposa ina.)

B. Nkhani zomveka bwino ndi zofunikira za mau a Mulungu sizingaikidwe pambali kapena

kukaikiridwa. Ngati sitilemekeza mphamvu ya mau a Mulungu, ndiye kuti basi, tataya zonse. Tasokonekera.

C. Koma kusiyana maganizo pa miyambo kumafuna kulolerana chifukwa ife pamodzi ndi

amphunzitsi athu tonsefe ndi anthu omwe tingathe kuchimwanso. Choncho ndikofunikira

kwambiri kumadziwa kuti kodi ndi nkhani ziti zomwe ziri zammalembo ndipo ndiziti zomwe

siziri zammalembo koma zamiyambo chabe.

D. Miyambo ndi zizolowezi za chikhalidwe ndi mamvedwe a zinthu angathe kusiyidwa pambali

ndikusinthidwa ngati akusokoneza ndikulepheretsa ntchito ya Mulungu.

Page 62: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 62

(Zitsanzo: ganizo loti akazi samakhala pamodzi pophunzira Baibulo mwapadera; kugwiritsa

ntchito Baibulo

lotanthauziridwa kamodzi kokha basi; kusagwirizana ndi nyumba zopembezereramo; maganizo oti mlaliki sangalalike mmalo oposera amodzi pa nthawi imodzi; ganizo loti munthu

mmodzi ndiye adzilalika nthawi zambiri mumpingo;p ndi zina zotere.)

3. Zoona zina zomwe tiyenera kuzizindikira zokhudza kusintha mmiyambo yathu.

A. Tiri ndi miyambo monganso ena amachitira.

B. Tiyenera kumadziwa kusiyana pakati pa miyambo ndi malembo kuti tisalimbane chifukwa cha

miyambo monga momwe tingachitire chifukwa cha malemba. Akhristu ena olemekezeka

akupha mipingo yawo chifukwa chosadziwa za kusiyana kumeneku. Tidzalandira mphoto

chifukwa choima nji! Pa malemba; tidzaweruzidwa chifukwa chogawanitsa kapena kutchinga

mpingo chifukwa cha miyambo ndi zizolowezi.

C. Kawirikawiri kusintha sikukhala kwa phindu ngati kungokhala kapena kuchitika chifukwa

chongofuna kusintha basi (pokhapokha kukhale chifukwa chofuna kutidzutsa ndikutipangitsa

kuti tiganize zomwe tikuchitazo).

D. Ngati njira kapena maganizo omwe tazolowera kuchitira zinthu akulepheretsa ntchito ya

Mulungu, tiyenera kukonzekera ndikukhala ndi chidwi chofuna kusintha. Iripo mizimu yomwe ikapezeka kumwamba pokhapokha ngati titasintha magwiridwe athu antchito kuti ikhale

yamphamvu. Paulo mtumwi anali wokonzekera kusintha chirichonse chomwe sichinali chomangiririka ku mau ngati chinali choti chikapulumutse mizimu yotayika – 1 Akorinto 9:19-

23 – ndipo sakanakondwera ndi mitima yathu yosalola kusunthika koma kuumirira miyambo

ndi zizolowezi yomwe ikulepheretsa kufikira mizimu yotayika yomwe iri kunja.

E. Inde ndikobvuta kwambiri kusiyiratu mwambo wogwirira ntchito kapena kamasuliridwe,

ngakhale kuti kutero kuli kulimbana ndi mau a Mulungu kapena kulepheretsa ntchito ya

Mulungu. Komatu dziwani kuti sipakhala kukula muuzimu kapena kukula kwa mpingo ngati

palibe kusintha kwabwino.

F. Zambiri zomwe tichita mumpingo kuti tiyang’anitsitse tidzaona kuti ndi zizolowezi chabe

kaya miyambo chabe zosati zofotokozeredwa mu malemba. Zitsanzo:

Mapemphero a Lachitatu madzulo.

Misonkhano iwiri yamapemphero Lamulungu. Mapemphero a Lamulungu mmawa pa 10:30

Mgonero wa Lamulungu usiku. Pemphero lalikulu limodzi.

Nyimbo zitatu tisanapemphere kenako nyimbo litatha pemphero. Kusiya vesi yachitatu ya nyimbo.

Bukhu la nyimbo. Otsogolera nyimbo.

Madododo a nyimbo mmabuku a nyimbo.

Mayimbidwe okhala ndi magawo anayi onse a mau.

Kuimba mokoma monga momwe tidziwira.

Chikho chakechake pamgonero.

Madzi a chipatso champesa.

Kudutsitsa chifaniziro cha mgonero mmizere.

Page 63: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 63

Kutenga kochepa kwambiri ka mkate ndi chikho.

Pagome. Nyumba zopemphereramo.

Maofesi a nyumba zopemphereramo. Zizindikiro za mpingo.

Dzina loti “Mpingo wa Khristu” monga dzina lokhalo lobvomerezeka ndi lopambana. Nyumba zosonkhanirana.

Mobatizira.

Malaudi sipikala.

Zida za kanema ndi kanema.

MaBaibulo olembedwa ndi alembi osiyanasiyana.

Kagawidwe ka mitu ndi ndime m’Baibulo.

Othandizira ntchito zina.

Ulaliki wotenga mphindi wakumi atatu (30 mins)

Nyimbo zoitana.

Misonkhano yofalitsa uthenga yotenga sabata yatunthu.

Munthu mmodzi yekha wolalikira nthawi zambiri.

Alaliki a achinyamata, misonkhano ya achinyamata kuperekera mbale ya chopereka.

1) Miyambo yambiri yomwe tawerengayi inayamba yakanidwapo pamene inali kungoyambidwa kumene. Ina yaiyo mpaka lero ikuoneka ngati yabwino ndi

yobvomerezeka munthawi zathu zino. Inayo ingafune kuonedwanso ndikusinthidwa apa ndi apo. Mbali yaikulu kwambiri ya dongosolo la momwe

tichitira mumpingo lingathe kusinthidwa koma ndikumapitirirabe kumvera ndikulemekezabe zomwe malemba amaphunzitsa.

Zofotokozera:

• Kukhala mozungulira gome ndikumalandira mgonero monga tichitira

pakudya chakudya.

• Zosakhala ndi woyendetsa ntchito kutsogolo kapena ulaliki wokonzedwa.

• Kuwernga malembo ambiri.

• Alaliki osiyanasiyana pa misonkhano yosiyana.

• Msonkhano kugawidwaq mtimagulu khumi ting’ono ting’ono.

• Msonkhano wotenga maola awiri.

• Mapemphero asanu kapena khumi.

• Aliyense kupita kutsogolo kukalandira mgonero.

• Kumangoimba ndi mau amodzi ofanana osagawa mmau anayi aja ngati kwayala.

• Kuyamba ndi mgonero ulaliki usayambe.

• Akazi kukhala kwaokha mosiyana ndi amuna.

• Kukumana kwa kumidzi.

Izi sikuti ndiye zobvomerezekazo, koma zikusonyeza zomwe zinayenera

kuchitidwa malingandi ndi malemba.

2) Tikanabvutika kwambiri polandira ndikupembedza potengera dongosolo la

mpingo woyamba uja, ngakhale posanena za mphatso zao za Mzimu Woyera:

• Analibe nyumba yawoyawo yopembedzera.

• Oyankhula ambiri pamsonkhano – aliyense yemwe anali ndi choyankhula.

• Aliyense yemwe anali ndi nyimbo yake

Page 64: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 64

ankaimba osatinso zotokonzekera.

• Nthawi zambiri ankakweza manja mmwamba popemphera.

• Akazi ankabvala maduku, osangoti monga chipewa chabe.

• Kulibe kukonzekera ngakhale dongosolo lenileni.

• Kupembeza kwawo kumatenga nthawi yaitali kwambiri.

3) Akhristu ampingo woyamba uja nawonso akanabvutika kwambiri ndi miyambo yathu.

• Kutsiriza ikamafika 12 koloko.

• Zinthu zabwino, zamakono monga nyumba etc.

• Akazi osabvala maduku, obvala zobvala zionetsa mikono yawo.

• Amuna ndi akazi kukhala pamodzi (kumaiko ena)

• Nyimbo zoyimbidwa mokoma, ndinso mamvekedwe anayi munyimbo

monga mau onse aakulu, aang’ono, apakati ndi ena okometsera.

• Misonkhano yokhala ndi ndondomeko, yochepetsedwa mwina chifukwa

cha zina (?)

4) Mipingo yathu imene, yasintha zambiri mzaka zapitazi osazindikira kuti tasiya

malemba.

• Kusintha kuchokera ku Baibulo Lolembedwa m’chichewa chakale kupita

ku chichewa chamakono.

• Misonkhano ya achinyamata.

• Magulu ogwira ntchito zina.

• Kuyenderana pakati pa amayi.

• Madongosolo a mautumiki.

• Magulu apadera oyimba.

• Mautumiki a mapemphero apadera.

• Nkhani za mumpingo m’manyuzi.

• Kugwiritsa ntchito vidiyo ndi zithunzi zake.

• Kugwiritsa ntchito ndalama zampingo pogulira chakudya ndi mmisonkhano.

• Matimu a mpira a mpingo.

• Nyumba zochitira masewera olimbitsa thupi ndi zina za anthu abanja

lonse.

• Alaliki achigawo kapena pamalo.

• Misonkhano yokonzedweratu.

• Ubatizo wochitika mmadamu okonza osati ku mtsinje kapena dziwe.

• Kugwiritsa ntchito malaudi sipikala ochokera ku “misonkhano ina” mu

mpingo wa Khristu.

• Kuwawerengera ana nthano ya m’Baibulo nthawi yamapemphero a Lamulungu.

G. Miyambo ingathe kukhala ndi nzeru. Nthawi zina zimaonetsa kuphunzira ndi umulungu wa

atsogoleri anzeru, komabe miyamboyi ndi ya anthu basi.

H. Miyambo kawirikawiri imangothandiza kuti munthu adziwike mtundu wake. Kusintha

miyambo ndi zizolowezi sikulakwira Mulungu, komatu kwa ife kumaoneka ngati kusintha mpingo. Koma kusintha kwambiri kopanda tanthauzo kwa miyambo ndi zizolowezi

Page 65: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 65

kungasokoneze mpingo ndikubweretsa kusamvana.

I. Bvutoli pamenepa sikukhala ndi miyambo, koma kuilola kuti ikhale monga mfumu

yotilamulira ndikumabvutika kusamala monga momwe tikanachita ndi mau a Mulungu.

J. Miyambo imasonkhanitsa ndipo imafuna kuti tidziilemekeza. Njira yekhayo yomwe ingatithandize kupewa kulowerera ndi kuyamba kulamuliriridwa ndikufooketsedwa ndi

miyambo ndi zizolowezi zimenezi, ndi younikanso miyambo yathuyo m’mibadwo yonse

pogwiritsa ntchito kuunika kwabwino kwa mau a Mulungu powerenga liwulo ngati kuti

sitinamveponso zamiyambo yathu. Izitu zimafuna kulimba mtima ndikupirira zedi. Miyambo

iyenera kumaunikidwa ndi malemba, osati malemba kumawaunika ndi miyambo.

Mau otsiriza: Tayesani kufufuza ndikuzindikira momwe maganizo anu amangiriridwa ku miyambo.

Tapezani nthawi yoti muganizire mozama zazinthu, ndipo mosadzinyenga nokha muonemo zinthu

zangokhala monga miyambo chabe. Izi zidzakuthandizani ndipo mudzaona kusiyana pamomwe

mudzayambire kubvomera momwe mungalandirire kusintha. Nditha kukhala ndi zinthu zanga zomwe

ziri zokondedwa ndipo ndimazitenga ngati zofunika kwambiri, komanso ndiyenera kulemekeza

ndikuonetsetsa kuti thupi la Ambuye likulandira zonse zofunikira zake ndiponso ndiyenera

kulemekeza zosowa ndi zofunikira poyamba za ena. Tiyenera “kumverana wina ndi mnzake

mkumvera Mulungu” – Aefeso 5:21.

--- B. Shelburne, West Tate Seminar, Brownfield, TX, Apr. 1992.

Mndandanda wa zothandiza zina pa zotsutsana.

Ngati mutapezana ndi wina wokutsutsani muntchito ya Mulungu, nawa Mafunso ena oti mudzifunse

nokha.

1. Kodi ine ndikuonjesera gawo liti ku makanganowa chifukwa cha kufooka kwanga, kupusa

kwanga, kusakhala ndi maganizo abwino kapena machimo?

2. Kodi kusayankha bwino kwanga kwaonjezera bwanji pakulimbanaku? Ndingathe

kudziletsa pamomwe ndichitira wina akandikwiyitsa.

3. Kodi yemwe akunditsutsayu walakwitsa komabw ali wokhulupirika, kapena ndiwochimwa

kwenikweni? Izi zimathandiza mayankhidwe anga.

4. Kodi ndikupemphera motsimikiza chifukwa cha wonditsutsayo ndinso kuti papezeke njira

ya chilungamo ndi yachiyero yothetsera bvutoli? Kodi ndayesapo kusala pamodzi ndi mapemphero? Kodi ndikufunsa nzefu, kudzichepetsa ndichizindikiritso cha zolakwa

zakumbali yanga? Chithandizo cha Mzimu Woyera.

5. Ngati pali kulakwirana, kodi ndapitapo kwa m’bale wangayo kapena mlongoyo momvera bwino malinga ndi dongosolo losanjidwa ndi Yesu mu Mateyu 18:15-20; 5:23-24?

6. Kodi ndapita ndi mtima wodekha (Agalatiya 6:1-2)? Kodi ndakonda mtendere wokwanira

kuti nditha kuchitadi dongosolo lopitalo mmalo modikira kuti koma winayo ndiye

andipeze?

7. Kodi ndayesetsa kusunga chinsinsi choti makanganowo asakhudze anthu ena? Izi

zimateteza umodzi wa mpingo ndi banja.

Page 66: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 66

8. Kodi ndikuyesetsa kugonjetsa choipa ndi chabwino? (Aroma 12:21) kapena kodi

ndikubwezera choipa ndi choipa chinzake? Kodi ndalola kuti wotsutsana nayeyo anditsitse mpaka ndifike pakufanana ndi khalidwe lakelo?

9. Kodi ndakumbukira kuti kubvutika chifukwa chikhala ndi moyo wofanana ndi Yesu

ndicho chiphunzitso chachikulu chomwe ndiyenera kupereka?

10. Kodi ndiri ndimantha kuti ndikambirane zobvuta ndi wonditsutsayo? Mutha kukambirana

pa chirichonse, chingakhale chobvuta chotani, ngati muyankhulana munjira yoyenera.

Kodi ndabwera munjira zoti zimupangitsa woyambana nayeyo kudziteteza m’malo

mololera? Kodi ndikuoneka ngati ndifuna kumuputa?

11. Kodi ndafufuza njira zina zocchitira zomwe ndiyenera kuchita, zomwe woyambana nayeyo

angathe kubvomereza? Nthawi zonse njira imapezeka ngati tikondweretsedwa

ndikufufuzako.

12. Kodi ndikuyankhulayankhula za woyambana nayeyo ndi ena mmalo moyankhula kwa iye?

Izi zimangosonkhezera moto wa kulimbanako.

13. Kodi ndikuyesetsa kudandaulira pagawo lomwe wotsutsana nayeyo ndi ine tingagwirizane? Kodi ndikuyesetsa kukonza ubale wathu?

14. Kodi ndakhala ndi nthawi yophunzira momwe Yesu pamodzi ndi ophunzira ake

anamchitira pamene panabuka kusamvana?

15. Kodi ndikuweruza zolinga za mkati a wotsutsana nayeyo pamene sindingathe kuona za mumtima kapena kudziwa zonse zachitika? (Yohane 7:24; Mateyu 7:1-5; Yakobo 2:12,13).

Kodi ndingakondwere ndi muyezo womwewo wachiweruzo utaperekedwa kwa ine?

16. Kodi ndayesa kupempha malangizo ndi uphungu kuchokera kwa achikulire, anzeru ndi

odalilika?

17. Kodi ndakhala nayo nthawi yoganizira ngatidi ndikubvutika chifukwa cha ine mwini

kapena chifukwa cha Mulungu? Kumbukirani kuti ife sitimuona Yesu akubvutika

chifukwa cha iye mwini, popeza anali atadzikhutula nali wofafa ku thupi. Ifenso

tikufunsidwa kuchita chimodzimodzi.

18. Ngati wotsutsana nayeyo salola kusintha, kodi ndiri wokonzeka kutula nkhani yonseyi kwa

Mulungu mwini? 1 Yohane 4:4; 1 Petro 2:23; Masalmo 23:5. Kodi ndiri wokonzeka

kusiyira Mulungu kuti abwezere zonse? Aroma 12:19. Kodi ndiri ndi mzimu wokhululuka, pozindikira kuti nanenso ndilakalaka kukhululukidwa – Mateyu 6:12,14,15.

19. Ngati ndichoka ndikusiya malo kapena chinthu chifukwa chakulimbana ndikutsutsana,

kodi ndayesetsa kuchita mbali yanga yosiya ubale uli wosaonongeka?

Zochokera ku maphunziro okonzedwa ndi a Shelburne otchedwa “Moyo ndi ntchito ya Mlaliki”

Ndondomeko ya Moyo wa Mpingo

Mipingo ina imalowa pansi chifukwa cha chiwerengero cha anthu ndi mabvuto ndi maganizo.

Page 67: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 67

1. Kodi tikumuika Khristu ndi mtanda monga potsamira penipeni pa uthenga wathu? 1 Akorinto

2:2.

2. Kodi abusa akuwetadi mwauzimu, kapena angopanga maganizo ongoti bola ziziyenda malinga ndikukonda kwawo? 1 Petro 5:1-4; Yohane 10:1-18; Ahebri 13:17.

3. Kodi alaliki sanasiyitsidwe ntchito yawo yeniyeni yolalika malembo ku mizimu yosowa?

Machitidwe 6:1-6.

4. Kodi alaliki ndi atsogoleri ndi zitsa zokwanira za zomwe alalika? 1 Timoteo 3:1-13; 4:12.

5. Kodi tikukopa anthu kulowa mumpingo ndi mau a Mulungu, kapena ndi ntchito zina zathupi

zosangalatsa thupi ndi zina zadziko? 1 Akorinto 3:10-13.

6. Kodi timawakonda osochera kotero kuti titha kudzichepetsa molingana ndi momwe angalolere

Mulungu kuti tikawafikire, kapena timayembekezera kuti iwo ndiwo ayenera kutsatira zomwe

ife tifuna basi? 1 Akorinto 9:19-23.

7. Kodi timalimbika posamala otembenuka mwatsopano ndi anthu omwe anagwa naukanso,

kapena timangowasiya akumangodzigwera okha? Mateyu 28:19-20; 1 Atesalonika 5:14; Aroma 15:1; Aefeso 4:11-=16; Ahebri 5:11; 6:3.

8. Kodi tikugwiritsa ntchito mphatso ndi maluso a azimayi mokwanira ndi mogwirizana ndi

malemba? Aroma 16:1-3,6,12; Afilipi 4:2,3; 1 Timoteo5:3-16.

9. Kodi tiri ndi chidwi chofuna kuthandiza anthu “kupachika umunthu wao wakale” ndikukhala obadwa mwatsopano ngati ife kuti abatizidwe? Kodi tikuthandiza anthu, kuphatikizapo

atsogoleri kuti athane ndi kudzitukumula ndi kudzikondweretsa okha komwe kumagawanitsa

mipingo ndi mabanja? Aroma 6:1-14; 7:7-25; 8:1-17; Aefeso 4:22-24; Agalatiya 5:19-23.

10. Kodi timalimbikira chiphunzitso cha m’Chipangano Chatsopano pa zakusinthika kwa mkati

monganso momwe tichitira ndi chiphunzitso cha “kutsatira dongosolo labwino?” 2 Timoteo

3:5; Mateyu 18:1-3; 2 Akorinto 3:6.

11. Kodi tikati kumvera timachit mogwirizana ndi uphungu wa Mulungu watunthu kapena

chifuniro cha Mulungu, kapena timangochita pongotsata ziphunzitso zotikondweretsa –

Machitidwe 20:27; Mateyu 23:23,24.

12. Kodi timawakonda otayika koti mpaka tingalolere kusiya miyambo yathu ina ngati

ingatisokoneze ndikulepheretsa kuti tikawafikire? Kodi timasokoneza miyambo ndi zizolowezi za chikhalidwe chathu ndi zofunikira za

malemba? Mateyu 15:1-9.

13. Kodi Akhristu ena onse omwe tisonkhana nawo amasamala kwambiri mizimu ya otayika koposa zowakondweretsa iwo eni ndi zosawakondweretsa? Aroma 15:1-3.

14. Kodi pali maubale oipa mumpingo kapena pakati pa atsogoleri omwe chifukwa

chakudzitukumula sitingathe kuwathetsa, ngakhale akulepheretsa ntchito ya mpingo? Kodi

iripo njira yomwe mukupanga pakali pano yoti muthandize kukonza ndi kuchotsa kuwawirana

mitima komwe kwakhalapo kuyambira kale mumpingomo komwe kukufoketsa mpingo?

Mateyu 18:15; 5:23,24; Afilipi 2:14-16.

Page 68: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 68

15. Kodi pali machimo ena omwe angobisidwa mmitima ya Akhristu kapena atsogoleri omwe

akulepheretsa kuti chisomo cha Mulungu chichite nawo mpingo ndikuthandiza? Yoswa 7; 2 Akorinto 6:14-7:1; 2 Timoteo 2:19-22.

16. Kodi atsogoleri akupitirizabe kuphunzira ndikukula kuti athe kutsogolera osati kuti mpingo

uwapitrire? 2 Timoteo 2:15; 2 Petro 3:18; Kodi alipo atsogoleri ena omwe akulephera kugwira ntchito chifukwa cha mantha? Mateyu 25:14-30; Chibvumbulutso 21:8.

17. Kodi kusala pamodzi ndi mapemphero kumakonzekera njira zabwino zopanga maganizo ndi

machitidwe abwino? Machitidwe 13:1-3; 14:23.

18. Kodi tikuphunzitsa mnjira yoti imapherezera mkusinthika kwa miyoyo? Kodi anthu

akuthandizidwa kutuluka muuchimo ndi moyo wachionongeko? Luka 4:18,19; Aroma 12:1,2.

(miyoyo yosinthika imakhala ndichikoka)

19. Kodi utumiki wathu wophunzitsa umalingana bwanji ndi utumiki wa mapemphero owirikiza?

Kodi kapena tikuyeserera kuchita ndi utumiki ulionse popanda unzake? Machitidwe 6:4; 13:3.

Maganizo khumi ndi atatu (13) omwe Thomas Campbell analemba ndi kunena poyera.

Ganizo 1: Kuti mpingo wa Khristu pano pa dziko lapansi mofunikira, mwacholinga komanso

mwalamulo langwirizano ndi umodzi; wokhala ndi iwo onse opezeka ku malo konse omwe chikhulupiriro chawo chimatsamira pa Khristu ndikumumvera mu zonse molingana ndi malemba,

ndikuonetsera zomwezonso pa khalidwe lawo lodziletsa, osati kwa wina aliyenseyo; pakuti siwina aliyenseyo amene angatchulidwe kuti ndi Mkhristu woona ndi wolongosoka.

2. KutiKuti ngakhale Mpingo wa Khristu pa dzikoli ufunikira kukhalabe pakati pa anthu

osiyanasiyana, mosiyana ndi wina, koma sipayenera kukhala kusiyananso ndi magawano

pakati pake. Ayenera kumalandirana wina ndi mnzake monganso momwe Yesu Khristu

wawalandirira ku ulemerero wa Mulungu. Choncho ndicholinga chimenechi onse anayenera

kumayendera lamulo limodzi, kusamalira ndikumayankhula chinthu chimodzi; ndi kukhalanso

olumikizidwa pamodzi mu mtima umodzi, ndinso muchiweruzo chimodzi.

3. Kuti izi zitgheke, pasakhale chirichonse chomwe chikidwe ndikukakamiza Akhristu monga

mfundo zolembedwa zoti Akhristu azizilemekeza monga chikhulupiriro chawo, kapena

chomwe ayener kulamulidwqa nacho mona malamulo a mgonero, koma zokhazo zomwe

zaphunzitsidwa molongosoledwa bwino ndikuikidwa mwa iwo kuchokera mmawu a Mulungu.

Zosaloleranso china chirichonse, kutengedwa ngati lamulo la Mzimu Woyera, mu malamulo

oyendetsera mpingo wawo ndi ntchito zina zapakati pawo, koma zokhazo zomwe

zafotokozedwsa bwino ndi kuperekedwa kwa iwo mwa ulamuliro wa Ambuyathu Yesu Khristu pamodzi ndi Atumwi ake pa Mpingo wa m’Chipangano Chatsopano; kaya pa

kulongosolera kaya pakutsimikizira pa zomwe zinachitika kale.

4. Kuti ngakhale malemba am’Chipangano Chakale ndi Chatsopano ndi ogwirizana mosalekana, pamodzi ndikupanga bvumbulutso limodzi langwiro la chifuniro cha umulungu, lomangirira

ndikupulumutsa mpingo, choncho chifukwa chachimenechi sungagawanitsidwe; koma pa za chomwe chiri cha pacholinga chawo cha panthawi yomweyo, Chipangano Chatsopano chiri

changwiro monga Bukhu la malamulo a chipembedzo, khalidwe labwino, ndi kayendetsedwe

kampingo wa Chipangano Chatsopano, ndinso monga lamulo langwiro lapakagwiridwe

kantchito zina za anthu ake, monganso popeza Chipangano Chakale chinali mapembedzedwe,

kusunga khalidwe labwino, ndiponso kayendetsedwe kabwino ka ntchito za mpingo

waChipangano Chakale ndi ntchito zinanso zosankhikia za anthu ake.

Page 69: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 69

5. Kuti ndikulemekeza malamulo ndi zoikika za Ambuye wathu Yesu Khristu, pamene malembo

akhala chete pa za nthawi kapena machitidwe, ngati zoterozo ziripo, palibe ulamuliro wamunthu womwe uli ndi mphamvu yoikapo maganizo ake, ndicholinga chofuna kukwaniritsa

zooneka zoperewerazo podzipangira malamulo ampingo; kapena pasapezeke kuwaikira

Akhristu madongosolo ena munkhani ngati zimenezi, koma iwo ayenera kugwiritsa ntchito malamulo ndi zoikika za Ambuye Yesu monga momwe zingagwirizanire mwachidziwikire ndi

kuyankha cholinga cha mpingo wawo. Munthu alibe mwai waukulu woika ulamulo ndi

zoikika zake mu mpingo, zomwe Ambuyathu Yesu Khristu sanaike. Palibe chirichonse

chomwe chiyenera kulandiridwa mu chikhulupiriro kapena chipembedzo champingo, kapena

kupangidwa mona mfundo yoyanjanitsa pakati pa Akhristu, chomwe sichinakhalapo munthawi

ya Chipangano Chatsopano.

6. Kuti ngakhale zoganizira ndi zochotsedwa ku malemba, ngati ziganiziridwa mwabwino,

zingathe kutengedwa monga chiphunzitso cha malembo oyera a Mulungu, koma pamenepa

ndiye kuti sakumangirika ku chikumbumtima cha Akhristu kopitirira momwe amalandirira

choonadicho, ndikumaona ngati ndimmwne ziyenera kukhalira malinga ndi zomwe

akuwerengazo; popeza chikhulupiriro chawo sichiyenera kuima pa nzeru ya anthu, koma

mumphamvu ndi ulemerero wa Mulungu. Choncho, kuchotsera koteroko kusapangidwe

kukhala monga lamulo loyanjanitsira, koma akhalapo zonse zoyeretsa, kukonza chimangiriro cha mpingo. Choncho apa nchachidziwikire kuti kuchotserako zina za mmalemba kotereku,

ndikuganizira ndikuikirira maganizo ena omaoneka ngati oona sikuyenera kuchitika munkhani zonse zampingo.

7. Kuti ngakhale ziphunzitso za choonadi cha umulungu, ndi maumboni odzitetezera ku

zolakwikazi, akhale oti mwina tingataye nawo moyo, ndipo pamene ali okwanira ndi oyenera zolinga zimenezi, ndiye kuti ziri bwino; komabe, popeza zambiri za zimenezi zichitika

m’maganizo aumunthu, ndiponso zambiri zake zichokera ku zoganizira za munthu, siziyenera

kutengedwa ngati malamulo oyendetsera Chiyanjano cha Akhristu; pokhapokhapo tiganizira

zomwe ziri zotsutsana ndi zoonazo, zakuti palibe yemwe ali ndi ufulu pa zachiyanjano cha

mpingo, koma zokhazo zokhala ndi chiweruzo chokhala ndi maganizo omveka, kapena afikira

pa kudziwitsitsa za ziphunzitso; pamene mpingo unadziwa ndikukhala nazo kuyambira kale

lomwe, ndipo udzakhala nazo, zokhala ndi ana, ang’ono ndi achinyamata pamodzi ndi

abambo.

8. Kuti monga kuli kosafunikira kuti anthu ayenera kudziwa kapena kumvetsa bwino zoonadi za

umulungu zonse zobvumbulutsidwa kuti ziwayeneretse kukhala ndi udindo mumpingo;

pachifukwa chomwechi, asabvutike ndikukhala ndi luso la ntchito mwapadera koposa momwe

angadziwire; koma kuti posiyana ndi zimenezi, mwakuzindikira za moyo wao mwauzimu,

kusochera ndikuonongeka kwa moyo wao mwa chikhalidwe ndi zochita, ndinso za njira ya chipulumutso mwa Yesu Khristu, kuphatikizira pa luso la pa chikhulupiriro chawo ndi

kumvera iye mu zinthu zonse, molingana ndi mau ake, ndizomwe ziri zofunikira kwa iwo kuwayenereza kulandiridwa ku Mpingo wake.

9. Kuti osne amalandira luso limeneli chifukwa cha chisomo, ndipo amachitira umboni zonsezi

kudzera momwe achitira ndi khalidwe lawo ndi zopsetsa mtima zawo, aonane wina ndi mnzake oyeretsedwa amtengo wapatali a Mulungu, akondane wina ndi mnzake ngati abale,

ana am’banja limodzi ndi atate mmodzi, akachisi a mtima umodzi, anthu a mtchupi limodzi,

achisomo chimodzi, ziwalo za chikondi chimodzi cha umulungu, ogulidwa ndi dipo lamtengo

umodzi, ndiponso oyembekezera mwaumodzi kulowa cholowa chimodzi. Choncho omwe

Mulungu wawamanga pamodzi munthu wina asyeserere kuwalekanitsa.

Page 70: Umodzi Womwe Khristu Anaupemphereranamikangobibleschool.org/uploads/PDFS/UMODZI.pdf · Umodzi 11/29/12 Umodzi Womwe Khristu Anaupempherera Mawu oyamba: Titha kumadziwa malembo, titha

Umodzi 70

Kuti malekano pakati pa Akhristu ndichinthu chipitsitsa, chodzala ndi machimo ena

ambirimbiri. Malekano ndi chinthu chotsutsana ndi Chikhristu, popeza chimaononga umodi wooneka wa thupi laKhristu; ngati kuti iye anagawanika, kuchotsa ndikudula magawo ena

athupi lake. Malekano ndi kutsutsana ndi malemba, monga amaletsedwa ndi ulamuliro wa

Mulungu, kuphwanya lamulo lake. Malekano siumunthu, popeza amautsa Akhristu kuti azidzudzulana, adzizondana kapena kudana, omwe ali omangiriridwa ku lamulo lalikulu,

loposa, lokondana wina ndi mnzake ngati abale, makamaka monga momwe Khristunso

anawakondera. Mwachidule, malekano ndi chipatso cha kusokonekera maganizo ndinso cha

ntchito iriyonse yachoipa.

10. Kuti kunyalanyaza ndikusiyako zina za bvumbulutso la choonadi cha Mulungu, ndinso

kungoonjezera ulamuliro wina wopangitsa kuti maganizo a anthu ndizopeka zina kukhala njira

yoyanjanitsira, poziika mu malamulo, chikhulupiriro, kapena chipembedzo cha mpingo, ziri,

komanso zakhala zodziwika zomwe zayambitsa ndikubweretsa, kuyambitsa zonse

zachinyengo ndinso kugawanikana zomwe sizinachitikeponso mu Mpingo wa Mulungu.

11. Kuti zonse zomwe ndi zotumikira kwambiri ku ungwiro woposa ndi zoyeretsedwa za mpingo

pano pa dziko ziri, choyamba, kuti palibe womwe ukalandiridwe ngati woyanjana nafe, koma

monga wokhala ndi muyezo wa chidziwitso cha malemba chomwe chanenedwa pamwambapa, ngakhale, chachiwiri, kuti uliwonse ukhale pachiyanjano chake kopotirira koposa ngakhale

zoona za luso lake pa momwe achitira ndi zopsetsa mtima ndi khalidwe lake. Chachitatu, kuti oyang’anira ake okhala nazo zoyeneretsa monga mwa malemba, ogwiritsa ntchito mfundo

zokhazo zachikhulupiriro ndi chiyero zobvumbulutsidwa ndikuikidwa mmau a Mulungu osati zina ziri zonsezo zopangidwa ndi munthu. Potsiriza kuti mmagwiridwe ao onse a ntchito zawo

amakhala pafupi ndikusunga zonse zoikika ndi umulungu, chitatha chitsanzo cha mpingo wakalekale, kuonetseredwa m’Chipangano Chatsopano; popanda zoonjezera zina ziri zonse za

maganizo a munthu kapena zongotulukiridwa ndikuikidwa ndi anthu.

12. Potsiriza. Ngati pali zina zochitika malingana ndi nthawi zofunikira kuti zithandizane pochita

ndi zoikikika za umulungu zisapezeke mmasamba a bvumbulutso la Mulungu, koma, zokhazo

zomwe ziri zofunikira pachifukwa chimenechi ziikidwa pansi pa gulu za anthu, popanda

kukometsera kwa mtundu wina uliwonse kuti zioneke ngati gwero lake ndilopatulika, kotero

kuti kusinthika kulikonse komwe kungachitike kapena kusiyana pa masungidwe a zinthu

zimenezi kusabweretse kulimbana kapena kugawanikana mumpingo.

Translated from English by Rhodes Maluwa. © by G.B. Shelburne, III (except for any graphics and scripture quotations). May be reproduced for non-profit, non-publishing instructional purposes provided this entire copyright notice is included and document content is not altered. South Houston Bible

Institute, PO Box 891246, Houston, TX 77289-1246 USA, tel. 281-990-8899, Email [email protected], web site <www.shbi.org>. Scriptures, unless

othewise noted, are taken from theBukhu Loyera, lopangidwa ndi The Bible Society of Malawi, P.O. Box 740, Blantyre, Malawi, copyright @ 1999.